< Masalimo 105 >
1 Yamikani Yehova, itanani dzina lake; lalikirani pakati pa anthu a mitundu ina zimene Iye wachita.
Славте Господа, кличте ім’я Його; серед народів звіщайте діяння Його!
2 Imbirani Iye, imbani matamando kwa Iyeyo; fotokozani za machitidwe ake onse odabwitsa.
Співайте Йому, грайте для Нього, звіщайте всі чудеса Його,
3 Munyadire dzina lake loyera; mitima ya iwo amene amafunafuna Yehova ikondwere.
хваліться іменем Його святим! Нехай веселиться серце тих, хто шукає Господа!
4 Dalirani Yehova ndi mphamvu zake; funafunani nkhope yake nthawi yonse.
Прагніть Господа й сили Його, шукайте обличчя Його завжди.
5 Kumbukirani zodabwitsa zimene Iye anazichita, zozizwitsa zake ndi maweruzo amene anapereka,
Пам’ятайте про чудеса Його, які Він здійснив, про знамення та суди Його.
6 inu zidzukulu za Abrahamu mtumiki wake, inu ana a Yakobo, osankhika ake.
О нащадки Авраама, слуги Його, сини Якова, Його обранці!
7 Iye ndiye Yehova Mulungu wathu; maweruzo ake ali pa dziko lonse lapansi.
Він – Господь, Бог наш; суди Його справедливі по всій землі.
8 Iyeyo amakumbukira pangano lake kwamuyaya, mawu amene analamula kwa mibado yonse,
Він вічно пам’ятає Завіт Свій, слово, яке Він заповів для тисяч поколінь, –
9 pangano limene Iye anapanga ndi Abrahamu, lumbiro limene analumbira kwa Isake.
[Завіт], який Він уклав з Авраамом, і присягу Його Ісааку.
10 Iye analitsimikiza kwa Yakobo monga zophunzitsa, kwa Israeli monga pangano lamuyaya:
Він встановив його статутом для Якова, як Завіт вічний для Ізраїля,
11 “Ndidzapereka kwa iwe dziko la Kanaani ngati gawo la cholowa chako.”
кажучи: «Тобі віддам Я землю Ханаану як долю вашого спадку».
12 Pamene iwo anali ngati anthu ochepa mʼchiwerengero, ochepa ndithu, ndiponso alendo mʼdzikolo,
Коли вони були людом нечисленним, незначним, і мешкали як приходьки на ній,
13 ankayendayenda kuchoka ku mtundu wina wa anthu ndi kupita ku mtundu wina, kuchoka mu ufumu wina kupita ku wina.
то мандрували вони від народу до народу, від одного царства до іншого племені.
14 Iye sanalole wina aliyense kuwapondereza; anadzudzula mafumu chifukwa cha iwo:
Він не дозволяв нікому їх гнобити й докоряв за них царям:
15 “Musakhudze odzozedwa anga; musachitire choyipa aneneri anga.”
«Не чіпайте помазанців Моїх і пророкам Моїм не робіть зла».
16 Iye anabweretsa njala pa dziko ndipo anawononga chakudya chonse;
Він накликав голод на землю, зламав стебло хлібне.
17 Iyeyo anatumiza munthu patsogolo pawo, Yosefe anagulitsidwa ngati kapolo.
Послав перед ними чоловіка – у рабство був проданий Йосиф.
18 Iwo anavulaza mapazi ake ndi matangadza, khosi lake analiyika mʼzitsulo,
Його ноги стисли кайданами, на шию йому наклали залізо,
19 mpaka zimene Iye ananeneratu zitakwaniritsidwa, mpaka mawu a Yehova ataonetsa kuti Iye ananena zoona.
до того часу, поки не здійснилося сказане Господом, поки слово Господа не очистило його.
20 Mfumu inatuma munthu kukamumasula, wolamulira wa mitundu ya anthu anamasula iyeyo.
Послав цар [слуг своїх] і розв’язав його; правитель народів звільнив його.
21 Anamuyika kukhala wolamulira nyumba yake, wolamulira zonse zimene iye anali nazo,
Він поставив його володарем над домом своїм і правителем над усім своїм майном,
22 kulangiza ana a mfumu monga ankafunira ndi kuphunzitsa nzeru akuluakulu.
щоб він князів його міг стримувати на свій розсуд і старійшин його повчав.
23 Tsono Israeli analowa mu Igupto; Yakobo anakhala monga mlendo mʼdziko la Hamu.
Тоді прийшов Ізраїль до Єгипту, оселився Яків у землі Хамовій.
24 Yehova anachulukitsa anthu ake; ndipo anachititsa kuti akhale ochuluka kwambiri kuposa adani awo;
І дуже розмножив [Бог] народ Свій і зробив його сильнішим від супротивників його,
25 amene mitima yawo anayitembenuza kuti idane ndi anthu ake, kukonzera chiwembu atumiki ake.
чиї серця Він налаштував, щоб ненавиділи Його народ, щоб лукавили вони з Його рабами.
26 Yehova anatuma Mose mtumiki wake, ndi Aaroni amene Iye anamusankha.
Він послав Мойсея, слугу Свого, і Аарона, якого обрав Собі.
27 Iwo anachita zizindikiro zozizwitsa pakati pawo, zodabwitsa zake mʼdziko la Hamu.
Вони з’явили знамення Його серед них і чудеса – у землі Хамовій.
28 Yehova anatumiza mdima nasandutsa dziko kuti likhale la mdima. Koma anthuwo anakaniratu mawu a Yehova.
Він послав морок, і стало темно, і вони не посміли суперечити Його слову.
29 Yehova anasandutsa madzi awo kukhala magazi, kuchititsa kuti nsomba zawo zife.
Він перетворив води їхні на кров і умертвив рибу в них.
30 Dziko lawo linadzaza ndi achule amene analowa mʼzipinda zogona za olamulira awo.
Закишіла земля їхня жабами, навіть у покоях царів їхніх [були вони].
31 Iye anayankhula, ndipo kunabwera ntchentche zochuluka ndi nsabwe mʼdziko lawo lonse.
Він сказав, і прийшли рої мух, комарі були на всіх теренах їхніх.
32 Iyeyo anatembenuza mvula yawo kukhala matalala, ndi zingʼaningʼani mʼdziko lawo lonse;
Він дав їм замість дощу град, палючий вогонь – на землю їхню;
33 Anagwetsa mitengo yawo ya mpesa ndi mitengo yawo ya mkuyu, nawononganso mitengo ina ya mʼdziko lawolo.
він побив у них виноград та смоковницю, зламав дерева в їхньому краї.
34 Iye anayankhula, ndipo dzombe linabwera, ziwala zosawerengeka;
Сказав Він, і прийшла сарана і гусінь – немає їм ліку!
35 zinadya chilichonse chobiriwira cha mʼdziko lawo, zinadya zonse zotuluka mʼnthaka yawo.
І з’їли вони всю траву в землі їхній, пожерли плоди їхніх ґрунтів.
36 Kenaka anakantha ana onse oyamba kubadwa a mʼdziko lawo, zipatso zoyamba za umunthu wawo wonse.
Тоді вразив Він усіх первістків у землі їхній – першоплоди сили чоловічої.
37 Yehova anatulutsa Israeli, atatenga siliva ndi golide wambiri, ndipo pakati pa mafuko awo palibe mmodzi amene anafowoka.
І вивів Він ізраїльтян зі сріблом і золотом, не було серед племен їхніх того, хто спотикався.
38 Dziko la Igupto linakondwa pamene iwo anachoka, pakuti kuopsa kwa Israeli kunawagwera iwo.
Зрадів Єгипет, коли вони вийшли, бо страх напав на нього через них.
39 Iye anatambasula mitambo ngati chofunda chawo, ndi moto owawunikira usiku.
Розгорнув [Бог] хмару, як покривало, [вдень], і вогонь, щоб світити вночі.
40 Iwo anapempha, ndipo Iye anawabweretsera zinziri ndipo anawakhutitsa ndi chakudya chochokera kumwamba.
Просив [народ], і послав їм [Господь] перепілок і хлібом небесним наситив їх.
41 Iye anatsekula thanthwe, ndipo madzi anatuluka; ngati mtsinje anayenda mʼchipululu.
Відкрив Він скелю – і полилися води, потекли рікою в сухій землі.
42 Pakuti anakumbukira lonjezo lake loyera limene linaperekedwa kwa Abrahamu mtumiki wake.
Бо згадав Він слово Своє святе, [що дав] Авраамові, слузі Своєму.
43 Iye anatulutsa anthu ake akukondwera, osankhika ake akufuwula mwachimwemwe;
І вивів Він народ Свій у радості, обраних Своїх – із вигуком переможним.
44 Iye anawapatsa mayiko a anthu a mitundu ina ndipo anakhala olowamʼmalo a zimene ena anazivutikira,
Він дав їм землі народів, і вспадкували здобутки праці їхньої,
45 kuti iwo asunge malangizo ake ndi kutsatira malamulo ake. Tamandani Yehova.
щоб вони дотримувалися Його постанов і берегли закони Його. Алілуя!