< Masalimo 105 >

1 Yamikani Yehova, itanani dzina lake; lalikirani pakati pa anthu a mitundu ina zimene Iye wachita.
Tacken HERREN, åkallen hans namn, gören hans gärningar kunniga bland folken.
2 Imbirani Iye, imbani matamando kwa Iyeyo; fotokozani za machitidwe ake onse odabwitsa.
Sjungen till hans ära, lovsägen honom, talen om alla hans under.
3 Munyadire dzina lake loyera; mitima ya iwo amene amafunafuna Yehova ikondwere.
Berömmen eder av hans heliga namn; glädje sig av hjärtat de som söka HERREN.
4 Dalirani Yehova ndi mphamvu zake; funafunani nkhope yake nthawi yonse.
Frågen efter HERREN och hans makt, söken hans ansikte beständigt.
5 Kumbukirani zodabwitsa zimene Iye anazichita, zozizwitsa zake ndi maweruzo amene anapereka,
Tänken på de underbara verk som han har gjort, på hans under och hans muns domar,
6 inu zidzukulu za Abrahamu mtumiki wake, inu ana a Yakobo, osankhika ake.
I Abrahams, hans tjänares, säd, I Jakobs barn, hans utvalda.
7 Iye ndiye Yehova Mulungu wathu; maweruzo ake ali pa dziko lonse lapansi.
Han är HERREN, vår Gud; över hela jorden gå hans domar.
8 Iyeyo amakumbukira pangano lake kwamuyaya, mawu amene analamula kwa mibado yonse,
Han tänker evinnerligen på sitt förbund, intill tusen släkten på vad han har stadgat,
9 pangano limene Iye anapanga ndi Abrahamu, lumbiro limene analumbira kwa Isake.
på det förbund han slöt med Abraham och på sin ed till Isak.
10 Iye analitsimikiza kwa Yakobo monga zophunzitsa, kwa Israeli monga pangano lamuyaya:
Han fastställde det för Jakob till en stadga, för Israel till ett evigt förbund;
11 “Ndidzapereka kwa iwe dziko la Kanaani ngati gawo la cholowa chako.”
han sade: »Åt dig vill jag giva Kanaans land, det skall bliva eder arvedels lott.»
12 Pamene iwo anali ngati anthu ochepa mʼchiwerengero, ochepa ndithu, ndiponso alendo mʼdzikolo,
Då voro de ännu en liten hop, de voro ringa och främlingar därinne.
13 ankayendayenda kuchoka ku mtundu wina wa anthu ndi kupita ku mtundu wina, kuchoka mu ufumu wina kupita ku wina.
Och de vandrade åstad ifrån folk till folk, ifrån ett rike bort till ett annat.
14 Iye sanalole wina aliyense kuwapondereza; anadzudzula mafumu chifukwa cha iwo:
Han tillstadde ingen att göra dem skada, han straffade konungar för deras skull:
15 “Musakhudze odzozedwa anga; musachitire choyipa aneneri anga.”
»Kommen icke vid mina smorda, och gören ej mina profeter något ont.»
16 Iye anabweretsa njala pa dziko ndipo anawononga chakudya chonse;
Och när han bjöd hungersnöd komma över landet och fördärvade allt deras livsuppehälle,
17 Iyeyo anatumiza munthu patsogolo pawo, Yosefe anagulitsidwa ngati kapolo.
då sände han åstad en man framför dem: Josef blev såld till träl.
18 Iwo anavulaza mapazi ake ndi matangadza, khosi lake analiyika mʼzitsulo,
Man slog hans fötter i bojor, i järn fick han ligga fjättrad,
19 mpaka zimene Iye ananeneratu zitakwaniritsidwa, mpaka mawu a Yehova ataonetsa kuti Iye ananena zoona.
till den tid då hans ord uppfylldes, då HERRENS tal bevisade hans oskuld.
20 Mfumu inatuma munthu kukamumasula, wolamulira wa mitundu ya anthu anamasula iyeyo.
Då sände konungen och lät släppa honom lös, folkens behärskare gav honom fri.
21 Anamuyika kukhala wolamulira nyumba yake, wolamulira zonse zimene iye anali nazo,
Han satte honom till herre över sitt hus, till att råda över all hans egendom;
22 kulangiza ana a mfumu monga ankafunira ndi kuphunzitsa nzeru akuluakulu.
han skulle binda hans furstar efter sin vilja och lära hans äldste vishet.
23 Tsono Israeli analowa mu Igupto; Yakobo anakhala monga mlendo mʼdziko la Hamu.
Och Israel kom till Egypten, Jakob blev en gäst i Hams land.
24 Yehova anachulukitsa anthu ake; ndipo anachititsa kuti akhale ochuluka kwambiri kuposa adani awo;
Och HERREN gjorde sitt folk mycket fruktsamt och mäktigare än dess ovänner voro,
25 amene mitima yawo anayitembenuza kuti idane ndi anthu ake, kukonzera chiwembu atumiki ake.
de vilkas hjärtan han vände till att hata hans folk, till att lägga onda råd mot hans tjänare.
26 Yehova anatuma Mose mtumiki wake, ndi Aaroni amene Iye anamusankha.
Han sände Mose, sin tjänare, och Aron, som han hade utvalt.
27 Iwo anachita zizindikiro zozizwitsa pakati pawo, zodabwitsa zake mʼdziko la Hamu.
De gjorde hans tecken ibland dem och under i Hams land.
28 Yehova anatumiza mdima nasandutsa dziko kuti likhale la mdima. Koma anthuwo anakaniratu mawu a Yehova.
Han sände mörker och lät allt bliva mörkt; och de stodo icke emot hans ord.
29 Yehova anasandutsa madzi awo kukhala magazi, kuchititsa kuti nsomba zawo zife.
Han förvandlade deras vatten till blod och lät så deras fiskar dö.
30 Dziko lawo linadzaza ndi achule amene analowa mʼzipinda zogona za olamulira awo.
Deras land kom att vimla av paddor, ända in i deras konungars kamrar.
31 Iye anayankhula, ndipo kunabwera ntchentche zochuluka ndi nsabwe mʼdziko lawo lonse.
Han bjöd, och flugsvärmar kommo, mygg i hela deras land.
32 Iyeyo anatembenuza mvula yawo kukhala matalala, ndi zingʼaningʼani mʼdziko lawo lonse;
Han gav dem hagel för regn, eldslågor sände han i deras land.
33 Anagwetsa mitengo yawo ya mpesa ndi mitengo yawo ya mkuyu, nawononganso mitengo ina ya mʼdziko lawolo.
Och han slog deras vinträd och fikonträd och bröt sönder träden i deras land.
34 Iye anayankhula, ndipo dzombe linabwera, ziwala zosawerengeka;
Han bjöd, och gräshoppor kommo, och gräsmaskar i tallös mängd.
35 zinadya chilichonse chobiriwira cha mʼdziko lawo, zinadya zonse zotuluka mʼnthaka yawo.
De åto upp alla örter i deras land, de åto upp frukten på deras mark.
36 Kenaka anakantha ana onse oyamba kubadwa a mʼdziko lawo, zipatso zoyamba za umunthu wawo wonse.
Och han slog allt förstfött i deras land, förstlingen av all deras kraft.
37 Yehova anatulutsa Israeli, atatenga siliva ndi golide wambiri, ndipo pakati pa mafuko awo palibe mmodzi amene anafowoka.
Så förde han dem ut, med silver och guld, och i hans stammar var ingen som stapplade.
38 Dziko la Igupto linakondwa pamene iwo anachoka, pakuti kuopsa kwa Israeli kunawagwera iwo.
Egyptierna gladde sig, när de drogo ut; ty förskräckelse för Israel hade fallit över dem.
39 Iye anatambasula mitambo ngati chofunda chawo, ndi moto owawunikira usiku.
Han bredde ut ett moln till skygd, och en eld för att lysa om natten.
40 Iwo anapempha, ndipo Iye anawabweretsera zinziri ndipo anawakhutitsa ndi chakudya chochokera kumwamba.
De begärde, då lät han vaktlar komma, och med bröd från himmelen mättade han dem.
41 Iye anatsekula thanthwe, ndipo madzi anatuluka; ngati mtsinje anayenda mʼchipululu.
Han öppnade klippan, och vatten flödade; det gick genom öknen såsom en ström.
42 Pakuti anakumbukira lonjezo lake loyera limene linaperekedwa kwa Abrahamu mtumiki wake.
Ty han tänkte på sitt heliga ord, på sin tjänare Abraham.
43 Iye anatulutsa anthu ake akukondwera, osankhika ake akufuwula mwachimwemwe;
Så förde han ut sitt folk med fröjd, med jubel dem som han hade utvalt.
44 Iye anawapatsa mayiko a anthu a mitundu ina ndipo anakhala olowamʼmalo a zimene ena anazivutikira,
Han gav åt dem hedningarnas länder, och folkens förvärv fingo de till besittning,
45 kuti iwo asunge malangizo ake ndi kutsatira malamulo ake. Tamandani Yehova.
för att de skulle hålla hans stadgar och taga hans lagar i akt. Halleluja!

< Masalimo 105 >