< Masalimo 105 >
1 Yamikani Yehova, itanani dzina lake; lalikirani pakati pa anthu a mitundu ina zimene Iye wachita.
Louvai ao Senhor, e invocai o seu nome; fazei conhecidas as suas obras entre os povos.
2 Imbirani Iye, imbani matamando kwa Iyeyo; fotokozani za machitidwe ake onse odabwitsa.
Cantai-lhe, cantai-lhe salmos: falai de todas as suas maravilhas.
3 Munyadire dzina lake loyera; mitima ya iwo amene amafunafuna Yehova ikondwere.
Glóriai-vos no seu santo nome: alegre-se o coração daqueles que buscam ao Senhor.
4 Dalirani Yehova ndi mphamvu zake; funafunani nkhope yake nthawi yonse.
Buscai ao Senhor e a sua força: buscai a sua face continuamente.
5 Kumbukirani zodabwitsa zimene Iye anazichita, zozizwitsa zake ndi maweruzo amene anapereka,
Lembrai-vos das maravilhas que fez, dos seus prodígios e dos juízos da sua boca;
6 inu zidzukulu za Abrahamu mtumiki wake, inu ana a Yakobo, osankhika ake.
Vós, semente de Abraão, seu servo, vós, filhos de Jacob, seus escolhidos.
7 Iye ndiye Yehova Mulungu wathu; maweruzo ake ali pa dziko lonse lapansi.
Ele é o Senhor, nosso Deus; os seus juízos estão em toda a terra.
8 Iyeyo amakumbukira pangano lake kwamuyaya, mawu amene analamula kwa mibado yonse,
Lembrou-se do seu concerto para sempre, da palavra que mandou a milhares de gerações.
9 pangano limene Iye anapanga ndi Abrahamu, lumbiro limene analumbira kwa Isake.
O qual concerto fez com Abraão, e o seu juramento a Isaac.
10 Iye analitsimikiza kwa Yakobo monga zophunzitsa, kwa Israeli monga pangano lamuyaya:
E confirmou o mesmo a Jacob por estatuto, e a Israel por concerto eterno,
11 “Ndidzapereka kwa iwe dziko la Kanaani ngati gawo la cholowa chako.”
Dizendo: A ti darei a terra de Canaan, a sorte da vossa herança.
12 Pamene iwo anali ngati anthu ochepa mʼchiwerengero, ochepa ndithu, ndiponso alendo mʼdzikolo,
Quando eram poucos homens em número, sim, mui poucos e estrangeiros nela.
13 ankayendayenda kuchoka ku mtundu wina wa anthu ndi kupita ku mtundu wina, kuchoka mu ufumu wina kupita ku wina.
Quando andavam de nação em nação e dum reino para outro povo.
14 Iye sanalole wina aliyense kuwapondereza; anadzudzula mafumu chifukwa cha iwo:
Não permitiu a ninguém que os oprimisse, e por amor deles repreendeu a reis, dizendo:
15 “Musakhudze odzozedwa anga; musachitire choyipa aneneri anga.”
Não toqueis os meus ungidos, e não maltrateis os meus profetas.
16 Iye anabweretsa njala pa dziko ndipo anawononga chakudya chonse;
Chamou a fome sobre a terra, quebrantou todo o sustento do pão.
17 Iyeyo anatumiza munthu patsogolo pawo, Yosefe anagulitsidwa ngati kapolo.
Mandou perante eles um varão, José, que foi vendido por escravo:
18 Iwo anavulaza mapazi ake ndi matangadza, khosi lake analiyika mʼzitsulo,
Cujos pés apertaram com grilhões: foi metido em ferros:
19 mpaka zimene Iye ananeneratu zitakwaniritsidwa, mpaka mawu a Yehova ataonetsa kuti Iye ananena zoona.
Até ao tempo em que chegou a sua palavra; a palavra do Senhor o provou.
20 Mfumu inatuma munthu kukamumasula, wolamulira wa mitundu ya anthu anamasula iyeyo.
Mandou o rei, e o fez soltar; o governador dos povos, e o soltou.
21 Anamuyika kukhala wolamulira nyumba yake, wolamulira zonse zimene iye anali nazo,
Fê-lo senhor da sua casa, e governador de toda a sua fazenda;
22 kulangiza ana a mfumu monga ankafunira ndi kuphunzitsa nzeru akuluakulu.
Para sujeitar os seus príncipes a seu gosto, e instruir os seus anciãos.
23 Tsono Israeli analowa mu Igupto; Yakobo anakhala monga mlendo mʼdziko la Hamu.
Então Israel entrou no Egito, e Jacob peregrinou na terra de Cão.
24 Yehova anachulukitsa anthu ake; ndipo anachititsa kuti akhale ochuluka kwambiri kuposa adani awo;
E aumentou o seu povo em grande maneira, e o fez mais poderoso do que os seus inimigos.
25 amene mitima yawo anayitembenuza kuti idane ndi anthu ake, kukonzera chiwembu atumiki ake.
Virou o coração deles para que aborrecessem o seu povo, para que tratassem astutamente aos seus servos.
26 Yehova anatuma Mose mtumiki wake, ndi Aaroni amene Iye anamusankha.
Enviou Moisés, seu servo, e Aarão, a quem escolhera.
27 Iwo anachita zizindikiro zozizwitsa pakati pawo, zodabwitsa zake mʼdziko la Hamu.
Mostraram entre eles os seus sinais e prodígios, na terra de Cão.
28 Yehova anatumiza mdima nasandutsa dziko kuti likhale la mdima. Koma anthuwo anakaniratu mawu a Yehova.
Mandou trevas, e a fez escurecer; e não foram rebeldes à sua palavra.
29 Yehova anasandutsa madzi awo kukhala magazi, kuchititsa kuti nsomba zawo zife.
Converteu as suas águas em sangue, e matou os seus peixes.
30 Dziko lawo linadzaza ndi achule amene analowa mʼzipinda zogona za olamulira awo.
A sua terra produziu rãs em abundância, até nas câmaras dos seus reis.
31 Iye anayankhula, ndipo kunabwera ntchentche zochuluka ndi nsabwe mʼdziko lawo lonse.
Falou ele, e vieram enxames de moscas e piolhos em todo o seu termo.
32 Iyeyo anatembenuza mvula yawo kukhala matalala, ndi zingʼaningʼani mʼdziko lawo lonse;
Converteu as suas chuvas em saraiva, e fogo abrazador na sua terra.
33 Anagwetsa mitengo yawo ya mpesa ndi mitengo yawo ya mkuyu, nawononganso mitengo ina ya mʼdziko lawolo.
Feriu as suas vinhas e os seus figueirais, e quebrou as árvores dos seus termos.
34 Iye anayankhula, ndipo dzombe linabwera, ziwala zosawerengeka;
Falou ele, e vieram gafanhotos e pulgão sem número.
35 zinadya chilichonse chobiriwira cha mʼdziko lawo, zinadya zonse zotuluka mʼnthaka yawo.
E comeram toda a erva da sua terra, e devoraram o fruto dos seus campos.
36 Kenaka anakantha ana onse oyamba kubadwa a mʼdziko lawo, zipatso zoyamba za umunthu wawo wonse.
Feriu também a todos os primogênitos da sua terra, as primícias de todas as suas forças.
37 Yehova anatulutsa Israeli, atatenga siliva ndi golide wambiri, ndipo pakati pa mafuko awo palibe mmodzi amene anafowoka.
E tirou-os para fora com prata e ouro, e entre as suas tribos não houve um só fraco.
38 Dziko la Igupto linakondwa pamene iwo anachoka, pakuti kuopsa kwa Israeli kunawagwera iwo.
O Egito se alegrou quando eles sairam, porque o seu temor caira sobre eles.
39 Iye anatambasula mitambo ngati chofunda chawo, ndi moto owawunikira usiku.
Estendeu uma nuvem por coberta, e um fogo para alumiar de noite.
40 Iwo anapempha, ndipo Iye anawabweretsera zinziri ndipo anawakhutitsa ndi chakudya chochokera kumwamba.
Oraram, e ele fez vir codornizes, e os fartou de pão do céu.
41 Iye anatsekula thanthwe, ndipo madzi anatuluka; ngati mtsinje anayenda mʼchipululu.
Abriu a penha, e dela correram águas; correram pelos lugares secos como um rio.
42 Pakuti anakumbukira lonjezo lake loyera limene linaperekedwa kwa Abrahamu mtumiki wake.
Porque se lembrou da sua santa palavra, e de Abraão, seu servo.
43 Iye anatulutsa anthu ake akukondwera, osankhika ake akufuwula mwachimwemwe;
E tirou dali o seu povo com alegria, e os seus escolhidos com regozijo.
44 Iye anawapatsa mayiko a anthu a mitundu ina ndipo anakhala olowamʼmalo a zimene ena anazivutikira,
E deu-lhes as terras das nações; e herdaram o trabalho dos povos;
45 kuti iwo asunge malangizo ake ndi kutsatira malamulo ake. Tamandani Yehova.
Para que guardassem os seus preceitos, e observassem as suas leis. louvai ao Senhor.