< Masalimo 105 >

1 Yamikani Yehova, itanani dzina lake; lalikirani pakati pa anthu a mitundu ina zimene Iye wachita.
Pris Herren, påkall hans navn, kunngjør blandt folkene hans store gjerninger!
2 Imbirani Iye, imbani matamando kwa Iyeyo; fotokozani za machitidwe ake onse odabwitsa.
Syng for ham, lovsyng ham, grund på alle hans undergjerninger!
3 Munyadire dzina lake loyera; mitima ya iwo amene amafunafuna Yehova ikondwere.
Ros eder av hans hellige navn! Deres hjerte glede sig som søker Herren!
4 Dalirani Yehova ndi mphamvu zake; funafunani nkhope yake nthawi yonse.
Spør efter Herren og hans makt, søk hans åsyn all tid!
5 Kumbukirani zodabwitsa zimene Iye anazichita, zozizwitsa zake ndi maweruzo amene anapereka,
Kom i hu hans undergjerninger som han har gjort, hans undere og hans munns dommer,
6 inu zidzukulu za Abrahamu mtumiki wake, inu ana a Yakobo, osankhika ake.
I, hans tjener Abrahams avkom, Jakobs barn, hans utvalgte!
7 Iye ndiye Yehova Mulungu wathu; maweruzo ake ali pa dziko lonse lapansi.
Han er Herren vår Gud, hans dommer er over all jorden.
8 Iyeyo amakumbukira pangano lake kwamuyaya, mawu amene analamula kwa mibado yonse,
Han kommer evindelig sin pakt i hu, det ord han fastsatte for tusen slekter,
9 pangano limene Iye anapanga ndi Abrahamu, lumbiro limene analumbira kwa Isake.
den pakt han gjorde med Abraham, og sin ed til Isak;
10 Iye analitsimikiza kwa Yakobo monga zophunzitsa, kwa Israeli monga pangano lamuyaya:
og han stadfestet den som en rett for Jakob, som en evig pakt for Israel,
11 “Ndidzapereka kwa iwe dziko la Kanaani ngati gawo la cholowa chako.”
idet han sa: Dig vil jeg gi Kana'ans land til arvelodd.
12 Pamene iwo anali ngati anthu ochepa mʼchiwerengero, ochepa ndithu, ndiponso alendo mʼdzikolo,
Da de var en liten flokk, få og fremmede der,
13 ankayendayenda kuchoka ku mtundu wina wa anthu ndi kupita ku mtundu wina, kuchoka mu ufumu wina kupita ku wina.
og vandret fra folk til folk, fra et rike til et annet folk,
14 Iye sanalole wina aliyense kuwapondereza; anadzudzula mafumu chifukwa cha iwo:
tillot han ikke noget menneske å gjøre vold imot dem, og han straffet konger for deres skyld:
15 “Musakhudze odzozedwa anga; musachitire choyipa aneneri anga.”
Rør ikke ved mine salvede, og gjør ikke mine profeter noget ondt!
16 Iye anabweretsa njala pa dziko ndipo anawononga chakudya chonse;
Og han kalte hunger inn over landet, han brøt sønder hver støtte av brød.
17 Iyeyo anatumiza munthu patsogolo pawo, Yosefe anagulitsidwa ngati kapolo.
Han sendte en mann foran dem, til træl blev Josef solgt.
18 Iwo anavulaza mapazi ake ndi matangadza, khosi lake analiyika mʼzitsulo,
De plaget hans føtter med lenker, hans sjel kom i jern,
19 mpaka zimene Iye ananeneratu zitakwaniritsidwa, mpaka mawu a Yehova ataonetsa kuti Iye ananena zoona.
inntil den tid da hans ord slo til, da Herrens ord viste hans uskyld.
20 Mfumu inatuma munthu kukamumasula, wolamulira wa mitundu ya anthu anamasula iyeyo.
Da sendte kongen bud og lot ham løs, herskeren over folkeslag gav ham fri.
21 Anamuyika kukhala wolamulira nyumba yake, wolamulira zonse zimene iye anali nazo,
Han satte ham til herre over sitt hus og til hersker over alt sitt gods,
22 kulangiza ana a mfumu monga ankafunira ndi kuphunzitsa nzeru akuluakulu.
forat han skulde binde hans fyrster efter sin vilje og lære hans eldste visdom.
23 Tsono Israeli analowa mu Igupto; Yakobo anakhala monga mlendo mʼdziko la Hamu.
Så kom Israel til Egypten, og Jakob bodde som fremmed i Kams land.
24 Yehova anachulukitsa anthu ake; ndipo anachititsa kuti akhale ochuluka kwambiri kuposa adani awo;
Og han gjorde sitt folk såre fruktbart og gjorde det sterkere enn dets motstandere.
25 amene mitima yawo anayitembenuza kuti idane ndi anthu ake, kukonzera chiwembu atumiki ake.
Han vendte deres hjerte til å hate hans folk, til å gå frem med svik mot hans tjenere.
26 Yehova anatuma Mose mtumiki wake, ndi Aaroni amene Iye anamusankha.
Han sendte Moses, sin tjener, Aron som han hadde utvalgt.
27 Iwo anachita zizindikiro zozizwitsa pakati pawo, zodabwitsa zake mʼdziko la Hamu.
De gjorde hans tegn iblandt dem og undere i Kams land.
28 Yehova anatumiza mdima nasandutsa dziko kuti likhale la mdima. Koma anthuwo anakaniratu mawu a Yehova.
Han sendte mørke og gjorde det mørkt, og de var ikke gjenstridige mot hans ord.
29 Yehova anasandutsa madzi awo kukhala magazi, kuchititsa kuti nsomba zawo zife.
Han gjorde deres vann til blod, og han drepte deres fisker.
30 Dziko lawo linadzaza ndi achule amene analowa mʼzipinda zogona za olamulira awo.
Deres land vrimlet av frosk, endog i deres kongers saler.
31 Iye anayankhula, ndipo kunabwera ntchentche zochuluka ndi nsabwe mʼdziko lawo lonse.
Han talte, og det kom fluesvermer, mygg innen hele deres landemerke.
32 Iyeyo anatembenuza mvula yawo kukhala matalala, ndi zingʼaningʼani mʼdziko lawo lonse;
Han gav dem hagl for regn, luende ild i deres land,
33 Anagwetsa mitengo yawo ya mpesa ndi mitengo yawo ya mkuyu, nawononganso mitengo ina ya mʼdziko lawolo.
og han slo ned deres vintrær og deres fikentrær, og brøt sønder trærne innen deres landemerke.
34 Iye anayankhula, ndipo dzombe linabwera, ziwala zosawerengeka;
Han talte, og det kom gresshopper og gnagere uten tall,
35 zinadya chilichonse chobiriwira cha mʼdziko lawo, zinadya zonse zotuluka mʼnthaka yawo.
og de åt op hver urt i deres land, og de åt op frukten på deres mark.
36 Kenaka anakantha ana onse oyamba kubadwa a mʼdziko lawo, zipatso zoyamba za umunthu wawo wonse.
Og han slo alt førstefødt i deres land, førstegrøden av all deres kraft.
37 Yehova anatulutsa Israeli, atatenga siliva ndi golide wambiri, ndipo pakati pa mafuko awo palibe mmodzi amene anafowoka.
Og han førte dem ut med sølv og gull, og det fantes ingen i hans stammer som snublet.
38 Dziko la Igupto linakondwa pamene iwo anachoka, pakuti kuopsa kwa Israeli kunawagwera iwo.
Egypten gledet sig da de drog ut; for frykt for dem var falt på dem.
39 Iye anatambasula mitambo ngati chofunda chawo, ndi moto owawunikira usiku.
Han bredte ut en sky til dekke og ild til å lyse om natten.
40 Iwo anapempha, ndipo Iye anawabweretsera zinziri ndipo anawakhutitsa ndi chakudya chochokera kumwamba.
De krevde, og han lot vaktler komme og mettet dem med himmelbrød.
41 Iye anatsekula thanthwe, ndipo madzi anatuluka; ngati mtsinje anayenda mʼchipululu.
Han åpnet klippen, og det fløt vann; det løp gjennem det tørre land som en strøm.
42 Pakuti anakumbukira lonjezo lake loyera limene linaperekedwa kwa Abrahamu mtumiki wake.
For han kom i hu sitt hellige ord, Abraham, sin tjener,
43 Iye anatulutsa anthu ake akukondwera, osankhika ake akufuwula mwachimwemwe;
og han førte sitt folk ut med glede, sine utvalgte med fryderop,
44 Iye anawapatsa mayiko a anthu a mitundu ina ndipo anakhala olowamʼmalo a zimene ena anazivutikira,
og han gav dem hedningefolks land, og hvad folkeslag med møie hadde vunnet, tok de til eie,
45 kuti iwo asunge malangizo ake ndi kutsatira malamulo ake. Tamandani Yehova.
forat de skulde holde hans forskrifter og ta vare på hans lover. Halleluja!

< Masalimo 105 >