< Masalimo 105 >

1 Yamikani Yehova, itanani dzina lake; lalikirani pakati pa anthu a mitundu ina zimene Iye wachita.
主に感謝し、そのみ名を呼び、そのみわざをもろもろの民のなかに知らせよ。
2 Imbirani Iye, imbani matamando kwa Iyeyo; fotokozani za machitidwe ake onse odabwitsa.
主にむかって歌え、主をほめうたえ、そのすべてのくすしきみわざを語れ。
3 Munyadire dzina lake loyera; mitima ya iwo amene amafunafuna Yehova ikondwere.
その聖なるみ名を誇れ。主を尋ね求める者の心を喜ばせよ。
4 Dalirani Yehova ndi mphamvu zake; funafunani nkhope yake nthawi yonse.
主とそのみ力とを求めよ、つねにそのみ顔を尋ねよ。
5 Kumbukirani zodabwitsa zimene Iye anazichita, zozizwitsa zake ndi maweruzo amene anapereka,
6 inu zidzukulu za Abrahamu mtumiki wake, inu ana a Yakobo, osankhika ake.
そのしもべアブラハムの子孫よ、その選ばれた者であるヤコブの子らよ、主のなされたくすしきみわざと、その奇跡と、そのみ口のさばきとを心にとめよ。
7 Iye ndiye Yehova Mulungu wathu; maweruzo ake ali pa dziko lonse lapansi.
彼はわれらの神、主でいらせられる。そのさばきは全地にある。
8 Iyeyo amakumbukira pangano lake kwamuyaya, mawu amene analamula kwa mibado yonse,
主はとこしえに、その契約をみこころにとめられる。これはよろず代に命じられたみ言葉であって、
9 pangano limene Iye anapanga ndi Abrahamu, lumbiro limene analumbira kwa Isake.
アブラハムと結ばれた契約、イサクに誓われた約束である。
10 Iye analitsimikiza kwa Yakobo monga zophunzitsa, kwa Israeli monga pangano lamuyaya:
主はこれを堅く立てて、ヤコブのために定めとし、イスラエルのために、とこしえの契約として
11 “Ndidzapereka kwa iwe dziko la Kanaani ngati gawo la cholowa chako.”
言われた、「わたしはあなたにカナンの地を与えて、あなたがたの受ける嗣業の分け前とする」と。
12 Pamene iwo anali ngati anthu ochepa mʼchiwerengero, ochepa ndithu, ndiponso alendo mʼdzikolo,
このとき彼らの数は少なくて、数えるに足らず、その所で旅びととなり、
13 ankayendayenda kuchoka ku mtundu wina wa anthu ndi kupita ku mtundu wina, kuchoka mu ufumu wina kupita ku wina.
この国からかの国へ行き、この国から他の民へ行った。
14 Iye sanalole wina aliyense kuwapondereza; anadzudzula mafumu chifukwa cha iwo:
主は人の彼らをしえたげるのをゆるさず、彼らのために王たちを懲しめて、
15 “Musakhudze odzozedwa anga; musachitire choyipa aneneri anga.”
言われた、「わが油そそがれた者たちにさわってはならない、わが預言者たちに害を加えてはならない」と。
16 Iye anabweretsa njala pa dziko ndipo anawononga chakudya chonse;
主はききんを地に招き、人のつえとするパンをことごとく砕かれた。
17 Iyeyo anatumiza munthu patsogolo pawo, Yosefe anagulitsidwa ngati kapolo.
また彼らの前にひとりをつかわされた。すなわち売られて奴隷となったヨセフである。
18 Iwo anavulaza mapazi ake ndi matangadza, khosi lake analiyika mʼzitsulo,
彼の足は足かせをもって痛められ、彼の首は鉄の首輪にはめられ、
19 mpaka zimene Iye ananeneratu zitakwaniritsidwa, mpaka mawu a Yehova ataonetsa kuti Iye ananena zoona.
彼の言葉の成る時まで、主のみ言葉が彼を試みた。
20 Mfumu inatuma munthu kukamumasula, wolamulira wa mitundu ya anthu anamasula iyeyo.
王は人をつかわして彼を解き放ち、民のつかさは彼に自由を与えた。
21 Anamuyika kukhala wolamulira nyumba yake, wolamulira zonse zimene iye anali nazo,
王はその家のつかさとしてその所有をことごとくつかさどらせ、
22 kulangiza ana a mfumu monga ankafunira ndi kuphunzitsa nzeru akuluakulu.
その心のままに君たちを教えさせ、長老たちに知恵を授けさせた。
23 Tsono Israeli analowa mu Igupto; Yakobo anakhala monga mlendo mʼdziko la Hamu.
その時イスラエルはエジプトにきたり、ヤコブはハムの地に寄留した。
24 Yehova anachulukitsa anthu ake; ndipo anachititsa kuti akhale ochuluka kwambiri kuposa adani awo;
主はその民を大いに増し加え、これをそのあだよりも強くされた。
25 amene mitima yawo anayitembenuza kuti idane ndi anthu ake, kukonzera chiwembu atumiki ake.
主は人々の心をかえて、その民を憎ませ、そのしもべたちを悪賢く扱わせられた。
26 Yehova anatuma Mose mtumiki wake, ndi Aaroni amene Iye anamusankha.
主はそのしもべモーセと、そのお選びになったアロンとをつかわされた。
27 Iwo anachita zizindikiro zozizwitsa pakati pawo, zodabwitsa zake mʼdziko la Hamu.
彼らはハムの地で主のしるしと、奇跡とを彼らのうちにおこなった。
28 Yehova anatumiza mdima nasandutsa dziko kuti likhale la mdima. Koma anthuwo anakaniratu mawu a Yehova.
主は暗やみをつかわして地を暗くされた。しかし彼らはそのみ言葉に従わなかった。
29 Yehova anasandutsa madzi awo kukhala magazi, kuchititsa kuti nsomba zawo zife.
主は彼らの水を血に変らせて、その魚を殺された。
30 Dziko lawo linadzaza ndi achule amene analowa mʼzipinda zogona za olamulira awo.
彼らの国には、かえるが群がり、王の寝間にまではいった。
31 Iye anayankhula, ndipo kunabwera ntchentche zochuluka ndi nsabwe mʼdziko lawo lonse.
主が言われると、はえの群れがきたり、ぶよが国じゅうにあった。
32 Iyeyo anatembenuza mvula yawo kukhala matalala, ndi zingʼaningʼani mʼdziko lawo lonse;
主は雨にかえて、ひょうを彼らに与え、きらめくいなずまを彼らの国に放たれた。
33 Anagwetsa mitengo yawo ya mpesa ndi mitengo yawo ya mkuyu, nawononganso mitengo ina ya mʼdziko lawolo.
主は彼らのぶどうの木と、いちじくの木とを撃ち、彼らの国のもろもろの木を折り砕かれた。
34 Iye anayankhula, ndipo dzombe linabwera, ziwala zosawerengeka;
主が言われると、いなごがきたり、無数の若いいなごが来て、
35 zinadya chilichonse chobiriwira cha mʼdziko lawo, zinadya zonse zotuluka mʼnthaka yawo.
彼らの国のすべての青物を食いつくし、その地の実を食いつくした。
36 Kenaka anakantha ana onse oyamba kubadwa a mʼdziko lawo, zipatso zoyamba za umunthu wawo wonse.
主は彼らの国のすべてのういごを撃ち、彼らのすべての力の初めを撃たれた。
37 Yehova anatulutsa Israeli, atatenga siliva ndi golide wambiri, ndipo pakati pa mafuko awo palibe mmodzi amene anafowoka.
そして金銀を携えてイスラエルを出て行かせられた。その部族のうちに、ひとりの倒れる者もなかった。
38 Dziko la Igupto linakondwa pamene iwo anachoka, pakuti kuopsa kwa Israeli kunawagwera iwo.
エジプトは彼らの去るのを喜んだ。彼らに対する恐れが彼らに臨んだからである。
39 Iye anatambasula mitambo ngati chofunda chawo, ndi moto owawunikira usiku.
主は雲をひろげておおいとし、夜は火をもって照された。
40 Iwo anapempha, ndipo Iye anawabweretsera zinziri ndipo anawakhutitsa ndi chakudya chochokera kumwamba.
また彼らの求めによって、うずらを飛びきたらせ、天から、かてを豊かに彼らに与えられた。
41 Iye anatsekula thanthwe, ndipo madzi anatuluka; ngati mtsinje anayenda mʼchipululu.
主が岩を開かれると、水がほとばしり出て、かわいた地に川のように流れた。
42 Pakuti anakumbukira lonjezo lake loyera limene linaperekedwa kwa Abrahamu mtumiki wake.
これは主がその聖なる約束と、そのしもべアブラハムを覚えられたからである。
43 Iye anatulutsa anthu ake akukondwera, osankhika ake akufuwula mwachimwemwe;
こうして主はその民を導いて喜びつつ出て行かせ、その選ばれた民を導いて歌いつつ出て行かせられた。
44 Iye anawapatsa mayiko a anthu a mitundu ina ndipo anakhala olowamʼmalo a zimene ena anazivutikira,
主はもろもろの国びとの地を彼らに与えられたので、彼らはもろもろの民の勤労の実を自分のものとした。
45 kuti iwo asunge malangizo ake ndi kutsatira malamulo ake. Tamandani Yehova.
これは彼らが主の定めを守り、そのおきてを行うためである。主をほめたたえよ。

< Masalimo 105 >