< Masalimo 105 >

1 Yamikani Yehova, itanani dzina lake; lalikirani pakati pa anthu a mitundu ina zimene Iye wachita.
Preiset den HERRN, ruft seinen Namen an, macht seine Taten unter den Völkern bekannt!
2 Imbirani Iye, imbani matamando kwa Iyeyo; fotokozani za machitidwe ake onse odabwitsa.
Singt ihm, spielet ihm, redet von all seinen Wundern!
3 Munyadire dzina lake loyera; mitima ya iwo amene amafunafuna Yehova ikondwere.
Rühmt euch seines heiligen Namens! Es mögen herzlich sich freun, die da suchen den HERRN!
4 Dalirani Yehova ndi mphamvu zake; funafunani nkhope yake nthawi yonse.
Fragt nach dem HERRN und seiner Stärke, suchet sein Angesicht allezeit!
5 Kumbukirani zodabwitsa zimene Iye anazichita, zozizwitsa zake ndi maweruzo amene anapereka,
Gedenkt seiner Wunder, die er getan, seiner Zeichen und der Urteilssprüche seines Mundes,
6 inu zidzukulu za Abrahamu mtumiki wake, inu ana a Yakobo, osankhika ake.
ihr Kinder Abrahams, seines Knechtes, ihr Söhne Jakobs, seine Erwählten!
7 Iye ndiye Yehova Mulungu wathu; maweruzo ake ali pa dziko lonse lapansi.
Er, der HERR, ist unser Gott, über die ganze Erde ergehen seine Gerichte.
8 Iyeyo amakumbukira pangano lake kwamuyaya, mawu amene analamula kwa mibado yonse,
Er gedenkt seines Bundes auf ewig, des Wortes, das er geboten auf tausend Geschlechter,
9 pangano limene Iye anapanga ndi Abrahamu, lumbiro limene analumbira kwa Isake.
(des Bundes) den er mit Abraham geschlossen, und des Eides, den er Isaak geschworen,
10 Iye analitsimikiza kwa Yakobo monga zophunzitsa, kwa Israeli monga pangano lamuyaya:
den für Jakob er als Satzung bestätigt und für Israel als ewigen Bund,
11 “Ndidzapereka kwa iwe dziko la Kanaani ngati gawo la cholowa chako.”
da er sprach: »Dir will ich Kanaan geben, das Land, das ich euch als Erbbesitztum zugeteilt!«
12 Pamene iwo anali ngati anthu ochepa mʼchiwerengero, ochepa ndithu, ndiponso alendo mʼdzikolo,
Damals waren sie noch ein kleines Häuflein, gar wenige und nur Gäste im Lande;
13 ankayendayenda kuchoka ku mtundu wina wa anthu ndi kupita ku mtundu wina, kuchoka mu ufumu wina kupita ku wina.
sie mußten wandern von Volk zu Volk, von einem Reich zur andern Völkerschaft;
14 Iye sanalole wina aliyense kuwapondereza; anadzudzula mafumu chifukwa cha iwo:
doch keinem gestattete er, sie zu bedrücken, ja Könige strafte er ihretwillen:
15 “Musakhudze odzozedwa anga; musachitire choyipa aneneri anga.”
»Tastet meine Gesalbten nicht an und tut meinen Propheten nichts zuleide!«
16 Iye anabweretsa njala pa dziko ndipo anawononga chakudya chonse;
Dann, als er Hunger ins Land ließ kommen und jegliche Stütze des Brotes zerbrach,
17 Iyeyo anatumiza munthu patsogolo pawo, Yosefe anagulitsidwa ngati kapolo.
da hatte er schon einen Mann vor ihnen her gesandt: Joseph, der als Sklave verkauft war.
18 Iwo anavulaza mapazi ake ndi matangadza, khosi lake analiyika mʼzitsulo,
Man hatte seine Füße gezwängt in den Stock, in Eisen(-fesseln) war er gelegt,
19 mpaka zimene Iye ananeneratu zitakwaniritsidwa, mpaka mawu a Yehova ataonetsa kuti Iye ananena zoona.
bis zu der Zeit, wo seine Weissagung eintraf und der Ausspruch des HERRN ihn als echt erwies.
20 Mfumu inatuma munthu kukamumasula, wolamulira wa mitundu ya anthu anamasula iyeyo.
Da sandte der König und ließ ihn entfesseln, der Völkergebieter, und machte ihn frei;
21 Anamuyika kukhala wolamulira nyumba yake, wolamulira zonse zimene iye anali nazo,
er bestellte ihn über sein Haus zum Herrn, zum Gebieter über sein ganzes Besitztum;
22 kulangiza ana a mfumu monga ankafunira ndi kuphunzitsa nzeru akuluakulu.
er sollte über seine Fürsten schalten nach Belieben und seine höchsten Beamten Weisheit lehren.
23 Tsono Israeli analowa mu Igupto; Yakobo anakhala monga mlendo mʼdziko la Hamu.
So kam denn Israel nach Ägypten, und Jakob weilte als Gast im Lande Hams.
24 Yehova anachulukitsa anthu ake; ndipo anachititsa kuti akhale ochuluka kwambiri kuposa adani awo;
Da machte Gott sein Volk gar fruchtbar und ließ es stärker werden als seine Bedränger;
25 amene mitima yawo anayitembenuza kuti idane ndi anthu ake, kukonzera chiwembu atumiki ake.
er wandelte ihren Sinn, sein Volk zu hassen und Arglist an seinen Knechten zu üben.
26 Yehova anatuma Mose mtumiki wake, ndi Aaroni amene Iye anamusankha.
Dann sandte er Mose, seinen Knecht, und Aaron, den er erkoren;
27 Iwo anachita zizindikiro zozizwitsa pakati pawo, zodabwitsa zake mʼdziko la Hamu.
die richteten seine Zeichen unter ihnen aus und die Wunder im Lande Hams:
28 Yehova anatumiza mdima nasandutsa dziko kuti likhale la mdima. Koma anthuwo anakaniratu mawu a Yehova.
Er sandte Finsternis und ließ es dunkel werden; doch sie achteten nicht auf seine Worte;
29 Yehova anasandutsa madzi awo kukhala magazi, kuchititsa kuti nsomba zawo zife.
er verwandelte ihre Gewässer in Blut und ließ ihre Fische sterben;
30 Dziko lawo linadzaza ndi achule amene analowa mʼzipinda zogona za olamulira awo.
es wimmelte ihr Land von Fröschen bis hinein in ihre Königsgemächer;
31 Iye anayankhula, ndipo kunabwera ntchentche zochuluka ndi nsabwe mʼdziko lawo lonse.
er gebot, da kamen Bremsenschwärme, Stechfliegen über ihr ganzes Gebiet;
32 Iyeyo anatembenuza mvula yawo kukhala matalala, ndi zingʼaningʼani mʼdziko lawo lonse;
er gab ihnen Hagelschauer als Regen, sandte flammendes Feuer in ihr Land;
33 Anagwetsa mitengo yawo ya mpesa ndi mitengo yawo ya mkuyu, nawononganso mitengo ina ya mʼdziko lawolo.
er schlug ihre Reben und Feigenbäume und zerbrach die Bäume in ihrem Gebiet;
34 Iye anayankhula, ndipo dzombe linabwera, ziwala zosawerengeka;
er gebot, da kamen die Heuschrecken und die Grillen in zahlloser Menge,
35 zinadya chilichonse chobiriwira cha mʼdziko lawo, zinadya zonse zotuluka mʼnthaka yawo.
die verzehrten alle Gewächse im Land und fraßen die Früchte ihrer Felder.
36 Kenaka anakantha ana onse oyamba kubadwa a mʼdziko lawo, zipatso zoyamba za umunthu wawo wonse.
Dann schlug er alle Erstgeburt im Lande, die Erstlinge all ihrer Manneskraft.
37 Yehova anatulutsa Israeli, atatenga siliva ndi golide wambiri, ndipo pakati pa mafuko awo palibe mmodzi amene anafowoka.
Nun ließ er sie ausziehn mit Silber und Gold, und kein Strauchelnder war in seinen Stämmen;
38 Dziko la Igupto linakondwa pamene iwo anachoka, pakuti kuopsa kwa Israeli kunawagwera iwo.
Ägypten war ihres Auszugs froh, denn Angst vor ihnen hatte sie befallen.
39 Iye anatambasula mitambo ngati chofunda chawo, ndi moto owawunikira usiku.
Er breitete Gewölk aus als Decke und Feuer, um ihnen die Nacht zu erhellen;
40 Iwo anapempha, ndipo Iye anawabweretsera zinziri ndipo anawakhutitsa ndi chakudya chochokera kumwamba.
auf Moses Bitte ließ er Wachteln kommen und sättigte sie mit Himmelsbrot;
41 Iye anatsekula thanthwe, ndipo madzi anatuluka; ngati mtsinje anayenda mʼchipululu.
er spaltete einen Felsen: da rannen Wasser und flossen durch die Steppen als Strom;
42 Pakuti anakumbukira lonjezo lake loyera limene linaperekedwa kwa Abrahamu mtumiki wake.
denn er gedachte seines heiligen Wortes, dachte an Abraham, seinen Knecht.
43 Iye anatulutsa anthu ake akukondwera, osankhika ake akufuwula mwachimwemwe;
So ließ er sein Volk in Freuden ausziehn, unter Jubel seine Erwählten;
44 Iye anawapatsa mayiko a anthu a mitundu ina ndipo anakhala olowamʼmalo a zimene ena anazivutikira,
dann gab er ihnen die Länder der Heiden, und was die Völker erworben, das nahmen sie in Besitz,
45 kuti iwo asunge malangizo ake ndi kutsatira malamulo ake. Tamandani Yehova.
auf daß sie seine Gebote halten möchten und seine Gesetze bewahrten. Halleluja!

< Masalimo 105 >