< Masalimo 105 >

1 Yamikani Yehova, itanani dzina lake; lalikirani pakati pa anthu a mitundu ina zimene Iye wachita.
Célébrez l’Éternel, invoquez son nom; faites connaître parmi les peuples ses actes!
2 Imbirani Iye, imbani matamando kwa Iyeyo; fotokozani za machitidwe ake onse odabwitsa.
Chantez-lui, chantez-lui des cantiques! Méditez toutes ses œuvres merveilleuses.
3 Munyadire dzina lake loyera; mitima ya iwo amene amafunafuna Yehova ikondwere.
Glorifiez-vous de son saint nom; que le cœur de ceux qui cherchent l’Éternel se réjouisse!
4 Dalirani Yehova ndi mphamvu zake; funafunani nkhope yake nthawi yonse.
Recherchez l’Éternel et sa force, cherchez continuellement sa face;
5 Kumbukirani zodabwitsa zimene Iye anazichita, zozizwitsa zake ndi maweruzo amene anapereka,
Souvenez-vous de ses œuvres merveilleuses qu’il a faites, de ses prodiges, et des jugements de sa bouche,
6 inu zidzukulu za Abrahamu mtumiki wake, inu ana a Yakobo, osankhika ake.
Vous, semence d’Abraham, son serviteur; vous, fils de Jacob, ses élus.
7 Iye ndiye Yehova Mulungu wathu; maweruzo ake ali pa dziko lonse lapansi.
Lui, l’Éternel, est notre Dieu; ses jugements sont en toute la terre.
8 Iyeyo amakumbukira pangano lake kwamuyaya, mawu amene analamula kwa mibado yonse,
Il s’est souvenu pour toujours de son alliance, de la parole qu’il commanda pour mille générations,
9 pangano limene Iye anapanga ndi Abrahamu, lumbiro limene analumbira kwa Isake.
[De l’alliance] qu’il a faite avec Abraham, et qu’il a jurée à Isaac,
10 Iye analitsimikiza kwa Yakobo monga zophunzitsa, kwa Israeli monga pangano lamuyaya:
Et qu’il a établie pour Jacob comme statut, pour Israël comme alliance perpétuelle,
11 “Ndidzapereka kwa iwe dziko la Kanaani ngati gawo la cholowa chako.”
Disant: Je te donnerai le pays de Canaan, le lot de votre héritage;
12 Pamene iwo anali ngati anthu ochepa mʼchiwerengero, ochepa ndithu, ndiponso alendo mʼdzikolo,
Quand ils étaient un petit nombre d’hommes, peu de chose, et étrangers dans le [pays],
13 ankayendayenda kuchoka ku mtundu wina wa anthu ndi kupita ku mtundu wina, kuchoka mu ufumu wina kupita ku wina.
Et allant de nation en nation, d’un royaume vers un autre peuple.
14 Iye sanalole wina aliyense kuwapondereza; anadzudzula mafumu chifukwa cha iwo:
Il ne permit à personne de les opprimer, et il reprit des rois à cause d’eux,
15 “Musakhudze odzozedwa anga; musachitire choyipa aneneri anga.”
[Disant]: Ne touchez pas à mes oints, et ne faites pas de mal à mes prophètes.
16 Iye anabweretsa njala pa dziko ndipo anawononga chakudya chonse;
Et il appela la famine sur la terre; il brisa tout le bâton du pain.
17 Iyeyo anatumiza munthu patsogolo pawo, Yosefe anagulitsidwa ngati kapolo.
Il envoya un homme devant eux: Joseph fut vendu pour être esclave.
18 Iwo anavulaza mapazi ake ndi matangadza, khosi lake analiyika mʼzitsulo,
On lui serra les pieds dans les ceps, son âme entra dans les fers,
19 mpaka zimene Iye ananeneratu zitakwaniritsidwa, mpaka mawu a Yehova ataonetsa kuti Iye ananena zoona.
Jusqu’au temps où arriva ce qu’il avait dit: la parole de l’Éternel l’éprouva.
20 Mfumu inatuma munthu kukamumasula, wolamulira wa mitundu ya anthu anamasula iyeyo.
Le roi envoya, et il le mit en liberté; le dominateur des peuples le relâcha.
21 Anamuyika kukhala wolamulira nyumba yake, wolamulira zonse zimene iye anali nazo,
Il l’établit seigneur sur sa maison, et gouverneur sur toutes ses possessions,
22 kulangiza ana a mfumu monga ankafunira ndi kuphunzitsa nzeru akuluakulu.
Pour lier ses princes à son plaisir, et pour rendre sages ses anciens.
23 Tsono Israeli analowa mu Igupto; Yakobo anakhala monga mlendo mʼdziko la Hamu.
Alors Israël entra en Égypte, et Jacob séjourna dans le pays de Cham.
24 Yehova anachulukitsa anthu ake; ndipo anachititsa kuti akhale ochuluka kwambiri kuposa adani awo;
Et [l’Éternel] fit beaucoup multiplier son peuple, et le rendit plus puissant que ses oppresseurs.
25 amene mitima yawo anayitembenuza kuti idane ndi anthu ake, kukonzera chiwembu atumiki ake.
Il changea leur cœur pour qu’ils haïssent son peuple, pour qu’ils complotent contre ses serviteurs.
26 Yehova anatuma Mose mtumiki wake, ndi Aaroni amene Iye anamusankha.
Il envoya Moïse, son serviteur, Aaron qu’il avait choisi.
27 Iwo anachita zizindikiro zozizwitsa pakati pawo, zodabwitsa zake mʼdziko la Hamu.
Ils opérèrent au milieu d’eux ses signes, et des prodiges dans le pays de Cham.
28 Yehova anatumiza mdima nasandutsa dziko kuti likhale la mdima. Koma anthuwo anakaniratu mawu a Yehova.
Il envoya des ténèbres, et fit une obscurité; et ils ne se rebellèrent pas contre sa parole.
29 Yehova anasandutsa madzi awo kukhala magazi, kuchititsa kuti nsomba zawo zife.
Il changea leurs eaux en sang, et fit mourir leurs poissons.
30 Dziko lawo linadzaza ndi achule amene analowa mʼzipinda zogona za olamulira awo.
Leur terre fourmilla de grenouilles, [jusque] dans les chambres de leurs rois.
31 Iye anayankhula, ndipo kunabwera ntchentche zochuluka ndi nsabwe mʼdziko lawo lonse.
Il parla, et il vint des mouches venimeuses, [et] des moustiques dans tous leurs confins.
32 Iyeyo anatembenuza mvula yawo kukhala matalala, ndi zingʼaningʼani mʼdziko lawo lonse;
Il leur donna pour pluie de la grêle, un feu de flammes dans leur pays;
33 Anagwetsa mitengo yawo ya mpesa ndi mitengo yawo ya mkuyu, nawononganso mitengo ina ya mʼdziko lawolo.
Et il frappa leurs vignes et leurs figuiers, et brisa les arbres de leur contrée.
34 Iye anayankhula, ndipo dzombe linabwera, ziwala zosawerengeka;
Il parla, et les sauterelles vinrent, et des yéleks sans nombre;
35 zinadya chilichonse chobiriwira cha mʼdziko lawo, zinadya zonse zotuluka mʼnthaka yawo.
Et ils dévorèrent toutes les plantes dans leur pays, et dévorèrent le fruit de leur sol.
36 Kenaka anakantha ana onse oyamba kubadwa a mʼdziko lawo, zipatso zoyamba za umunthu wawo wonse.
Et il frappa tout premier-né dans leur pays, les prémices de toute leur vigueur.
37 Yehova anatulutsa Israeli, atatenga siliva ndi golide wambiri, ndipo pakati pa mafuko awo palibe mmodzi amene anafowoka.
Et il les fit sortir avec de l’argent et de l’or, et il n’y eut aucun infirme dans ses tribus.
38 Dziko la Igupto linakondwa pamene iwo anachoka, pakuti kuopsa kwa Israeli kunawagwera iwo.
L’Égypte se réjouit à leur sortie, car la frayeur d’Israël était tombée sur eux.
39 Iye anatambasula mitambo ngati chofunda chawo, ndi moto owawunikira usiku.
Il étendit une nuée pour couverture, et un feu pour éclairer de nuit.
40 Iwo anapempha, ndipo Iye anawabweretsera zinziri ndipo anawakhutitsa ndi chakudya chochokera kumwamba.
Ils demandèrent, et il fit venir des cailles, et il les rassasia du pain des cieux.
41 Iye anatsekula thanthwe, ndipo madzi anatuluka; ngati mtsinje anayenda mʼchipululu.
Il ouvrit le rocher, et les eaux en découlèrent; elles allèrent par les lieux secs, comme une rivière.
42 Pakuti anakumbukira lonjezo lake loyera limene linaperekedwa kwa Abrahamu mtumiki wake.
Car il se souvint de sa parole sainte, [et] d’Abraham, son serviteur.
43 Iye anatulutsa anthu ake akukondwera, osankhika ake akufuwula mwachimwemwe;
Et il fit sortir son peuple avec joie, ses élus avec chant de triomphe;
44 Iye anawapatsa mayiko a anthu a mitundu ina ndipo anakhala olowamʼmalo a zimene ena anazivutikira,
Et il leur donna les pays des nations, et ils possédèrent le travail des peuples;
45 kuti iwo asunge malangizo ake ndi kutsatira malamulo ake. Tamandani Yehova.
Afin qu’ils gardent ses statuts, et qu’ils observent ses lois. Louez Jah!

< Masalimo 105 >