< Masalimo 105 >

1 Yamikani Yehova, itanani dzina lake; lalikirani pakati pa anthu a mitundu ina zimene Iye wachita.
Give thanks to Yahweh, call on his name; make known his deeds among the nations.
2 Imbirani Iye, imbani matamando kwa Iyeyo; fotokozani za machitidwe ake onse odabwitsa.
Sing to him, sing praises to him; speak of all his marvelous deeds.
3 Munyadire dzina lake loyera; mitima ya iwo amene amafunafuna Yehova ikondwere.
Boast in his holy name; let the heart of those who seek Yahweh rejoice.
4 Dalirani Yehova ndi mphamvu zake; funafunani nkhope yake nthawi yonse.
Seek Yahweh and his strength; seek his presence continually.
5 Kumbukirani zodabwitsa zimene Iye anazichita, zozizwitsa zake ndi maweruzo amene anapereka,
Recall the marvelous things he has done, his miracles and the decrees from his mouth,
6 inu zidzukulu za Abrahamu mtumiki wake, inu ana a Yakobo, osankhika ake.
you descendants of Abraham his servant, you people of Jacob, his chosen ones.
7 Iye ndiye Yehova Mulungu wathu; maweruzo ake ali pa dziko lonse lapansi.
He is Yahweh, our God. His decrees are on all the earth.
8 Iyeyo amakumbukira pangano lake kwamuyaya, mawu amene analamula kwa mibado yonse,
He keeps in mind his covenant forever, the word that he commanded for a thousand generations.
9 pangano limene Iye anapanga ndi Abrahamu, lumbiro limene analumbira kwa Isake.
He calls to mind the covenant that he made with Abraham and his oath to Isaac.
10 Iye analitsimikiza kwa Yakobo monga zophunzitsa, kwa Israeli monga pangano lamuyaya:
This is what he confirmed to Jacob as a statute and to Israel as an everlasting covenant.
11 “Ndidzapereka kwa iwe dziko la Kanaani ngati gawo la cholowa chako.”
He said, “I will give you the land of Canaan as your share of your inheritance.”
12 Pamene iwo anali ngati anthu ochepa mʼchiwerengero, ochepa ndithu, ndiponso alendo mʼdzikolo,
He said this when they were only few in number, so very few, and were strangers in the land.
13 ankayendayenda kuchoka ku mtundu wina wa anthu ndi kupita ku mtundu wina, kuchoka mu ufumu wina kupita ku wina.
They went from nation to nation and from one kingdom to another.
14 Iye sanalole wina aliyense kuwapondereza; anadzudzula mafumu chifukwa cha iwo:
He did not allow anyone to oppress them; he rebuked kings for their sakes.
15 “Musakhudze odzozedwa anga; musachitire choyipa aneneri anga.”
He said, “Do not touch my anointed ones, and do not harm my prophets.”
16 Iye anabweretsa njala pa dziko ndipo anawononga chakudya chonse;
He called for a famine on the land; he cut off the whole supply of bread.
17 Iyeyo anatumiza munthu patsogolo pawo, Yosefe anagulitsidwa ngati kapolo.
He sent a man ahead of them; Joseph was sold as a servant.
18 Iwo anavulaza mapazi ake ndi matangadza, khosi lake analiyika mʼzitsulo,
His feet were bound by shackles; on his neck was put an iron collar,
19 mpaka zimene Iye ananeneratu zitakwaniritsidwa, mpaka mawu a Yehova ataonetsa kuti Iye ananena zoona.
until what he had said came to pass. The word of Yahweh tested him.
20 Mfumu inatuma munthu kukamumasula, wolamulira wa mitundu ya anthu anamasula iyeyo.
The king sent servants to release him; the ruler of the people set him free.
21 Anamuyika kukhala wolamulira nyumba yake, wolamulira zonse zimene iye anali nazo,
He put him in charge of his house as ruler of all his possessions
22 kulangiza ana a mfumu monga ankafunira ndi kuphunzitsa nzeru akuluakulu.
to instruct his princes as he wished and to teach his elders wisdom.
23 Tsono Israeli analowa mu Igupto; Yakobo anakhala monga mlendo mʼdziko la Hamu.
Then Israel came into Egypt, and Jacob lived for a time in the land of Ham.
24 Yehova anachulukitsa anthu ake; ndipo anachititsa kuti akhale ochuluka kwambiri kuposa adani awo;
Yahweh made his people fruitful, and made them stronger than their enemies.
25 amene mitima yawo anayitembenuza kuti idane ndi anthu ake, kukonzera chiwembu atumiki ake.
He caused their enemies to hate his people, to mistreat his servants.
26 Yehova anatuma Mose mtumiki wake, ndi Aaroni amene Iye anamusankha.
He sent Moses, his servant, and Aaron, whom he had chosen.
27 Iwo anachita zizindikiro zozizwitsa pakati pawo, zodabwitsa zake mʼdziko la Hamu.
They performed his signs among the Egyptians, his wonders in the land of Ham.
28 Yehova anatumiza mdima nasandutsa dziko kuti likhale la mdima. Koma anthuwo anakaniratu mawu a Yehova.
He sent darkness and made that land dark, but its people did not obey his commands.
29 Yehova anasandutsa madzi awo kukhala magazi, kuchititsa kuti nsomba zawo zife.
He turned their water into blood and killed their fish.
30 Dziko lawo linadzaza ndi achule amene analowa mʼzipinda zogona za olamulira awo.
Their land swarmed with frogs, even in the rooms of their rulers.
31 Iye anayankhula, ndipo kunabwera ntchentche zochuluka ndi nsabwe mʼdziko lawo lonse.
He spoke, and swarms of flies and gnats came throughout their country.
32 Iyeyo anatembenuza mvula yawo kukhala matalala, ndi zingʼaningʼani mʼdziko lawo lonse;
He turned their rain into hail, with fire flaming on their land.
33 Anagwetsa mitengo yawo ya mpesa ndi mitengo yawo ya mkuyu, nawononganso mitengo ina ya mʼdziko lawolo.
He destroyed their vines and fig trees; he broke the trees of their country.
34 Iye anayankhula, ndipo dzombe linabwera, ziwala zosawerengeka;
He spoke, and the locusts came, so many locusts.
35 zinadya chilichonse chobiriwira cha mʼdziko lawo, zinadya zonse zotuluka mʼnthaka yawo.
The locusts ate up all of the vegetation in their land; They ate up all the crops of the ground.
36 Kenaka anakantha ana onse oyamba kubadwa a mʼdziko lawo, zipatso zoyamba za umunthu wawo wonse.
He killed every firstborn in their land, the firstfruits of all their strength.
37 Yehova anatulutsa Israeli, atatenga siliva ndi golide wambiri, ndipo pakati pa mafuko awo palibe mmodzi amene anafowoka.
He brought the Israelites out with silver and gold; none of his tribes stumbled on the way.
38 Dziko la Igupto linakondwa pamene iwo anachoka, pakuti kuopsa kwa Israeli kunawagwera iwo.
Egypt was glad when they went away, for the Egyptians were afraid of them.
39 Iye anatambasula mitambo ngati chofunda chawo, ndi moto owawunikira usiku.
He spread a cloud for a covering and made a fire to light up the night.
40 Iwo anapempha, ndipo Iye anawabweretsera zinziri ndipo anawakhutitsa ndi chakudya chochokera kumwamba.
The Israelites asked for food, and he brought quail and satisfied them with bread from heaven.
41 Iye anatsekula thanthwe, ndipo madzi anatuluka; ngati mtsinje anayenda mʼchipululu.
He split the rock, and waters gushed from it; they flowed in the wilderness like a river.
42 Pakuti anakumbukira lonjezo lake loyera limene linaperekedwa kwa Abrahamu mtumiki wake.
For he called to mind his holy promise that he made to Abraham his servant.
43 Iye anatulutsa anthu ake akukondwera, osankhika ake akufuwula mwachimwemwe;
He led his people out with joy, his chosen with shouts of triumph.
44 Iye anawapatsa mayiko a anthu a mitundu ina ndipo anakhala olowamʼmalo a zimene ena anazivutikira,
He gave them the lands of the nations; they took possession of the wealth of the peoples
45 kuti iwo asunge malangizo ake ndi kutsatira malamulo ake. Tamandani Yehova.
so that they might keep his statutes and obey his laws. Praise Yahweh.

< Masalimo 105 >