< Masalimo 105 >

1 Yamikani Yehova, itanani dzina lake; lalikirani pakati pa anthu a mitundu ina zimene Iye wachita.
Give thanks unto the LORD, call upon his name; make known his doings among the peoples.
2 Imbirani Iye, imbani matamando kwa Iyeyo; fotokozani za machitidwe ake onse odabwitsa.
Sing unto him, sing praises unto him; talk ye of all his marvelous works.
3 Munyadire dzina lake loyera; mitima ya iwo amene amafunafuna Yehova ikondwere.
Glory ye in his holy name: let the heart of them rejoice that seek the LORD.
4 Dalirani Yehova ndi mphamvu zake; funafunani nkhope yake nthawi yonse.
Seek ye the LORD and his strength; seek his face evermore.
5 Kumbukirani zodabwitsa zimene Iye anazichita, zozizwitsa zake ndi maweruzo amene anapereka,
Remember his marvelous works that he hath done; his wonders, and the judgments of his mouth;
6 inu zidzukulu za Abrahamu mtumiki wake, inu ana a Yakobo, osankhika ake.
O ye seed of Abraham his servant, ye children of Jacob, his chosen ones.
7 Iye ndiye Yehova Mulungu wathu; maweruzo ake ali pa dziko lonse lapansi.
He is the LORD our God: his judgments are in all the earth.
8 Iyeyo amakumbukira pangano lake kwamuyaya, mawu amene analamula kwa mibado yonse,
He hath remembered his covenant for ever, the word which he commanded to a thousand generations;
9 pangano limene Iye anapanga ndi Abrahamu, lumbiro limene analumbira kwa Isake.
[The covenant] which he made with Abraham, and his oath unto Isaac;
10 Iye analitsimikiza kwa Yakobo monga zophunzitsa, kwa Israeli monga pangano lamuyaya:
And confirmed the same unto Jacob for a statute, to Israel for an everlasting covenant:
11 “Ndidzapereka kwa iwe dziko la Kanaani ngati gawo la cholowa chako.”
Saying, Unto thee will I give the land of Canaan, the lot of your inheritance:
12 Pamene iwo anali ngati anthu ochepa mʼchiwerengero, ochepa ndithu, ndiponso alendo mʼdzikolo,
When they were but a few men in number; yea, very few, and sojourners in it;
13 ankayendayenda kuchoka ku mtundu wina wa anthu ndi kupita ku mtundu wina, kuchoka mu ufumu wina kupita ku wina.
And they went about from nation to nation, from one kingdom to another people.
14 Iye sanalole wina aliyense kuwapondereza; anadzudzula mafumu chifukwa cha iwo:
He suffered no man to do them wrong; yea, he reproved kings for their sakes;
15 “Musakhudze odzozedwa anga; musachitire choyipa aneneri anga.”
[Saying], Touch not mine anointed ones, and do my prophets no harm.
16 Iye anabweretsa njala pa dziko ndipo anawononga chakudya chonse;
And he called for a famine upon the land; he brake the whole staff of bread.
17 Iyeyo anatumiza munthu patsogolo pawo, Yosefe anagulitsidwa ngati kapolo.
He sent a man before them; Joseph was sold for a servant:
18 Iwo anavulaza mapazi ake ndi matangadza, khosi lake analiyika mʼzitsulo,
His feet they hurt with fetters; he was laid in [chains of] iron:
19 mpaka zimene Iye ananeneratu zitakwaniritsidwa, mpaka mawu a Yehova ataonetsa kuti Iye ananena zoona.
Until the time that his word came to pass; the word of the LORD tried him.
20 Mfumu inatuma munthu kukamumasula, wolamulira wa mitundu ya anthu anamasula iyeyo.
The king sent and loosed him; even the ruler of peoples, and let him go free.
21 Anamuyika kukhala wolamulira nyumba yake, wolamulira zonse zimene iye anali nazo,
He made him lord of his house, and ruler of all his substance:
22 kulangiza ana a mfumu monga ankafunira ndi kuphunzitsa nzeru akuluakulu.
To bind his princes at his pleasure, and teach his senators wisdom.
23 Tsono Israeli analowa mu Igupto; Yakobo anakhala monga mlendo mʼdziko la Hamu.
Israel also came into Egypt; and Jacob sojourned in the land of Ham.
24 Yehova anachulukitsa anthu ake; ndipo anachititsa kuti akhale ochuluka kwambiri kuposa adani awo;
And he increased his people greatly, and made them stronger than their adversaries.
25 amene mitima yawo anayitembenuza kuti idane ndi anthu ake, kukonzera chiwembu atumiki ake.
He turned their heart to hate his people, to deal subtilly with his servants.
26 Yehova anatuma Mose mtumiki wake, ndi Aaroni amene Iye anamusankha.
He sent Moses his servant, [and] Aaron whom he had chosen.
27 Iwo anachita zizindikiro zozizwitsa pakati pawo, zodabwitsa zake mʼdziko la Hamu.
They set among them his signs, and wonders in the land of Ham.
28 Yehova anatumiza mdima nasandutsa dziko kuti likhale la mdima. Koma anthuwo anakaniratu mawu a Yehova.
He sent darkness, and made it dark; and they rebelled not against his words.
29 Yehova anasandutsa madzi awo kukhala magazi, kuchititsa kuti nsomba zawo zife.
He turned their waters into blood, and slew their fish.
30 Dziko lawo linadzaza ndi achule amene analowa mʼzipinda zogona za olamulira awo.
Their land swarmed with frogs, in the chambers of their kings.
31 Iye anayankhula, ndipo kunabwera ntchentche zochuluka ndi nsabwe mʼdziko lawo lonse.
He spake, and there came swarms of flies, and lice in all their borders.
32 Iyeyo anatembenuza mvula yawo kukhala matalala, ndi zingʼaningʼani mʼdziko lawo lonse;
He gave them hail for rain, [and] flaming fire in their land.
33 Anagwetsa mitengo yawo ya mpesa ndi mitengo yawo ya mkuyu, nawononganso mitengo ina ya mʼdziko lawolo.
He smote their vines also and their fig trees; and brake the trees of their borders.
34 Iye anayankhula, ndipo dzombe linabwera, ziwala zosawerengeka;
He spake, and the locust came, and the cankerworm, and that without number,
35 zinadya chilichonse chobiriwira cha mʼdziko lawo, zinadya zonse zotuluka mʼnthaka yawo.
And did eat up every herb in their land, and did eat up the fruit of their ground.
36 Kenaka anakantha ana onse oyamba kubadwa a mʼdziko lawo, zipatso zoyamba za umunthu wawo wonse.
He smote also all the firstborn in their land, the chief of all their strength.
37 Yehova anatulutsa Israeli, atatenga siliva ndi golide wambiri, ndipo pakati pa mafuko awo palibe mmodzi amene anafowoka.
And he brought them forth with silver and gold: and there was not one feeble person among his tribes.
38 Dziko la Igupto linakondwa pamene iwo anachoka, pakuti kuopsa kwa Israeli kunawagwera iwo.
Egypt was glad when they departed; for the fear of them had fallen upon them.
39 Iye anatambasula mitambo ngati chofunda chawo, ndi moto owawunikira usiku.
He spread a cloud for a covering; and fire to give light in the night.
40 Iwo anapempha, ndipo Iye anawabweretsera zinziri ndipo anawakhutitsa ndi chakudya chochokera kumwamba.
They asked, and he brought quails, and satisfied them with the bread of heaven.
41 Iye anatsekula thanthwe, ndipo madzi anatuluka; ngati mtsinje anayenda mʼchipululu.
He opened the rock, and waters gushed out; they ran in the dry places [like] a river.
42 Pakuti anakumbukira lonjezo lake loyera limene linaperekedwa kwa Abrahamu mtumiki wake.
For he remembered his holy word, [and] Abraham his servant.
43 Iye anatulutsa anthu ake akukondwera, osankhika ake akufuwula mwachimwemwe;
And he brought forth his people with joy, [and] his chosen with singing.
44 Iye anawapatsa mayiko a anthu a mitundu ina ndipo anakhala olowamʼmalo a zimene ena anazivutikira,
And he gave them the lands of the nations; and they took the labour of the peoples in possession:
45 kuti iwo asunge malangizo ake ndi kutsatira malamulo ake. Tamandani Yehova.
That they might keep his statutes, and observe his laws. Praise ye the LORD.

< Masalimo 105 >