< Masalimo 105 >
1 Yamikani Yehova, itanani dzina lake; lalikirani pakati pa anthu a mitundu ina zimene Iye wachita.
O give thanks unto the LORD; Call upon his name; Make known his deeds among the people!
2 Imbirani Iye, imbani matamando kwa Iyeyo; fotokozani za machitidwe ake onse odabwitsa.
Sing unto him; sing psalms unto him; Tell ye of all his wondrous works!
3 Munyadire dzina lake loyera; mitima ya iwo amene amafunafuna Yehova ikondwere.
Glory ye in his holy name; Let the hearts of them that seek the LORD rejoice!
4 Dalirani Yehova ndi mphamvu zake; funafunani nkhope yake nthawi yonse.
Seek the LORD, and his majesty; Seek his face continually!
5 Kumbukirani zodabwitsa zimene Iye anazichita, zozizwitsa zake ndi maweruzo amene anapereka,
Remember the wonders he hath wrought, His miracles and the judgments of his mouth,
6 inu zidzukulu za Abrahamu mtumiki wake, inu ana a Yakobo, osankhika ake.
Ye offspring of Abraham his servant, Ye children of Jacob his chosen!
7 Iye ndiye Yehova Mulungu wathu; maweruzo ake ali pa dziko lonse lapansi.
Jehovah, he is our God, His judgments are over all the earth.
8 Iyeyo amakumbukira pangano lake kwamuyaya, mawu amene analamula kwa mibado yonse,
He remembereth his covenant for ever, And the promise to a thousand generations;
9 pangano limene Iye anapanga ndi Abrahamu, lumbiro limene analumbira kwa Isake.
The covenant which he made with Abraham, And the oath which he gave to Isaac;
10 Iye analitsimikiza kwa Yakobo monga zophunzitsa, kwa Israeli monga pangano lamuyaya:
Which he confirmed to Jacob for a decree, And to Israel for an everlasting covenant.
11 “Ndidzapereka kwa iwe dziko la Kanaani ngati gawo la cholowa chako.”
“To thee,” said he, “will I give the land of Canaan For the lot of your inheritance.”
12 Pamene iwo anali ngati anthu ochepa mʼchiwerengero, ochepa ndithu, ndiponso alendo mʼdzikolo,
When they were yet few in number, Very few, and strangers in the land;
13 ankayendayenda kuchoka ku mtundu wina wa anthu ndi kupita ku mtundu wina, kuchoka mu ufumu wina kupita ku wina.
When they went from nation to nation, From one kingdom to another people,
14 Iye sanalole wina aliyense kuwapondereza; anadzudzula mafumu chifukwa cha iwo:
He suffered no man to oppress them; Yea, he rebuked kings for their sakes.
15 “Musakhudze odzozedwa anga; musachitire choyipa aneneri anga.”
“Touch not,” said he, “mine anointed, And do my prophets no harm!”
16 Iye anabweretsa njala pa dziko ndipo anawononga chakudya chonse;
Again, when he commanded a famine in the land, And broke the whole staff of bread,
17 Iyeyo anatumiza munthu patsogolo pawo, Yosefe anagulitsidwa ngati kapolo.
He sent a man before them; Joseph was sold as a slave.
18 Iwo anavulaza mapazi ake ndi matangadza, khosi lake analiyika mʼzitsulo,
His feet they hurt with fetters; He was bound in chains of iron;
19 mpaka zimene Iye ananeneratu zitakwaniritsidwa, mpaka mawu a Yehova ataonetsa kuti Iye ananena zoona.
Until his prediction came to pass, And the word of the LORD proved him.
20 Mfumu inatuma munthu kukamumasula, wolamulira wa mitundu ya anthu anamasula iyeyo.
Then the king sent, and loosed him; The ruler of nations, and set him free;
21 Anamuyika kukhala wolamulira nyumba yake, wolamulira zonse zimene iye anali nazo,
He made him governor of his house, And lord of all his possessions;
22 kulangiza ana a mfumu monga ankafunira ndi kuphunzitsa nzeru akuluakulu.
To bind his princes at his pleasure, And teach his counsellors wisdom.
23 Tsono Israeli analowa mu Igupto; Yakobo anakhala monga mlendo mʼdziko la Hamu.
Israel also came into Egypt, And Jacob sojourned in the land of Ham;
24 Yehova anachulukitsa anthu ake; ndipo anachititsa kuti akhale ochuluka kwambiri kuposa adani awo;
Where God increased his people greatly, And made them stronger than their enemies.
25 amene mitima yawo anayitembenuza kuti idane ndi anthu ake, kukonzera chiwembu atumiki ake.
He turned their hearts to hate his people, And form devices against his servants.
26 Yehova anatuma Mose mtumiki wake, ndi Aaroni amene Iye anamusankha.
Then sent he Moses his servant, And Aaron, whom he had chosen.
27 Iwo anachita zizindikiro zozizwitsa pakati pawo, zodabwitsa zake mʼdziko la Hamu.
They showed his signs among them, And his wonders in the land of Ham.
28 Yehova anatumiza mdima nasandutsa dziko kuti likhale la mdima. Koma anthuwo anakaniratu mawu a Yehova.
He sent darkness upon them, and made it dark; And they did not disobey his word.
29 Yehova anasandutsa madzi awo kukhala magazi, kuchititsa kuti nsomba zawo zife.
He turned their waters into blood, And caused their fish to die.
30 Dziko lawo linadzaza ndi achule amene analowa mʼzipinda zogona za olamulira awo.
Their land brought forth frogs in abundance, Even in the chambers of their kings.
31 Iye anayankhula, ndipo kunabwera ntchentche zochuluka ndi nsabwe mʼdziko lawo lonse.
He spake, and there came flies, And lice in all their coasts.
32 Iyeyo anatembenuza mvula yawo kukhala matalala, ndi zingʼaningʼani mʼdziko lawo lonse;
Instead of rain he gave them hail, And flaming fire in their land.
33 Anagwetsa mitengo yawo ya mpesa ndi mitengo yawo ya mkuyu, nawononganso mitengo ina ya mʼdziko lawolo.
He smote also their vines and fig-trees, And broke the trees of their coasts.
34 Iye anayankhula, ndipo dzombe linabwera, ziwala zosawerengeka;
He spake, and the locusts came. Destructive locusts without number,
35 zinadya chilichonse chobiriwira cha mʼdziko lawo, zinadya zonse zotuluka mʼnthaka yawo.
Which ate up all the herbage in their land, And devoured the fruits of their fields.
36 Kenaka anakantha ana onse oyamba kubadwa a mʼdziko lawo, zipatso zoyamba za umunthu wawo wonse.
Then he smote all the first-born in their land, The first-fruits of all their strength.
37 Yehova anatulutsa Israeli, atatenga siliva ndi golide wambiri, ndipo pakati pa mafuko awo palibe mmodzi amene anafowoka.
He led forth his people with silver and gold; Nor was there one feeble person in all their tribes.
38 Dziko la Igupto linakondwa pamene iwo anachoka, pakuti kuopsa kwa Israeli kunawagwera iwo.
Egypt was glad when they departed, For their terror had fallen upon them.
39 Iye anatambasula mitambo ngati chofunda chawo, ndi moto owawunikira usiku.
He spread out a cloud for a covering, And fire to give light by night.
40 Iwo anapempha, ndipo Iye anawabweretsera zinziri ndipo anawakhutitsa ndi chakudya chochokera kumwamba.
They asked, and he brought quails, And satisfied them with the bread of heaven.
41 Iye anatsekula thanthwe, ndipo madzi anatuluka; ngati mtsinje anayenda mʼchipululu.
He opened the rock, and the waters gushed forth, And ran in the dry places like a river.
42 Pakuti anakumbukira lonjezo lake loyera limene linaperekedwa kwa Abrahamu mtumiki wake.
For he remembered his holy promise, Which he had made to Abraham his servant;
43 Iye anatulutsa anthu ake akukondwera, osankhika ake akufuwula mwachimwemwe;
And he led forth his people with joy, And his chosen with gladness.
44 Iye anawapatsa mayiko a anthu a mitundu ina ndipo anakhala olowamʼmalo a zimene ena anazivutikira,
He gave to them the lands of the nations, And they inherited the labor of the peoples;
45 kuti iwo asunge malangizo ake ndi kutsatira malamulo ake. Tamandani Yehova.
That they might observe his statutes, And obey his laws. Praise ye the LORD!