< Masalimo 105 >

1 Yamikani Yehova, itanani dzina lake; lalikirani pakati pa anthu a mitundu ina zimene Iye wachita.
Give thanks to the LORD. Call on his name. Make his deeds known among the peoples.
2 Imbirani Iye, imbani matamando kwa Iyeyo; fotokozani za machitidwe ake onse odabwitsa.
Sing to him, sing praises to him. Tell of all his marvelous works.
3 Munyadire dzina lake loyera; mitima ya iwo amene amafunafuna Yehova ikondwere.
Glory in his holy name. Let the heart of those who seek the LORD rejoice.
4 Dalirani Yehova ndi mphamvu zake; funafunani nkhope yake nthawi yonse.
Seek the LORD and his strength. Seek his face forever more.
5 Kumbukirani zodabwitsa zimene Iye anazichita, zozizwitsa zake ndi maweruzo amene anapereka,
Remember his marvelous works that he has done; his wonders, and the judgments of his mouth,
6 inu zidzukulu za Abrahamu mtumiki wake, inu ana a Yakobo, osankhika ake.
you offspring of Abraham, his servant, you descendants of Jacob, his chosen ones.
7 Iye ndiye Yehova Mulungu wathu; maweruzo ake ali pa dziko lonse lapansi.
He is the LORD, our God. His judgments are in all the earth.
8 Iyeyo amakumbukira pangano lake kwamuyaya, mawu amene analamula kwa mibado yonse,
He has remembered his covenant forever, the word which he commanded to a thousand generations,
9 pangano limene Iye anapanga ndi Abrahamu, lumbiro limene analumbira kwa Isake.
the covenant which he made with Abraham, his oath to Isaac,
10 Iye analitsimikiza kwa Yakobo monga zophunzitsa, kwa Israeli monga pangano lamuyaya:
and confirmed the same to Jacob for a statute; to Israel for an everlasting covenant,
11 “Ndidzapereka kwa iwe dziko la Kanaani ngati gawo la cholowa chako.”
saying, "To you I will give the land of Canaan, the lot of your inheritance;"
12 Pamene iwo anali ngati anthu ochepa mʼchiwerengero, ochepa ndithu, ndiponso alendo mʼdzikolo,
when they were but a few men in number, yes, very few, and foreigners in it.
13 ankayendayenda kuchoka ku mtundu wina wa anthu ndi kupita ku mtundu wina, kuchoka mu ufumu wina kupita ku wina.
They went about from nation to nation, from one kingdom to another people.
14 Iye sanalole wina aliyense kuwapondereza; anadzudzula mafumu chifukwa cha iwo:
He allowed no one to do them wrong. Yes, he reproved kings for their sakes,
15 “Musakhudze odzozedwa anga; musachitire choyipa aneneri anga.”
"Do not touch my anointed ones. Do my prophets no harm."
16 Iye anabweretsa njala pa dziko ndipo anawononga chakudya chonse;
He called for a famine on the land. He destroyed the food supplies.
17 Iyeyo anatumiza munthu patsogolo pawo, Yosefe anagulitsidwa ngati kapolo.
He sent a man ahead of them, Joseph, sold as a slave.
18 Iwo anavulaza mapazi ake ndi matangadza, khosi lake analiyika mʼzitsulo,
They bruised his feet with shackles. His neck was locked in irons,
19 mpaka zimene Iye ananeneratu zitakwaniritsidwa, mpaka mawu a Yehova ataonetsa kuti Iye ananena zoona.
until the time that his word happened, and the LORD's word proved him true.
20 Mfumu inatuma munthu kukamumasula, wolamulira wa mitundu ya anthu anamasula iyeyo.
The king sent and freed him; even the ruler of peoples, and let him go free.
21 Anamuyika kukhala wolamulira nyumba yake, wolamulira zonse zimene iye anali nazo,
He made him lord of his house, and ruler of all of his possessions;
22 kulangiza ana a mfumu monga ankafunira ndi kuphunzitsa nzeru akuluakulu.
to discipline his princes at his pleasure, and to teach his elders wisdom.
23 Tsono Israeli analowa mu Igupto; Yakobo anakhala monga mlendo mʼdziko la Hamu.
Israel also came into Egypt. Jacob sojourned in the land of Ham.
24 Yehova anachulukitsa anthu ake; ndipo anachititsa kuti akhale ochuluka kwambiri kuposa adani awo;
He increased his people greatly, and made them stronger than their adversaries.
25 amene mitima yawo anayitembenuza kuti idane ndi anthu ake, kukonzera chiwembu atumiki ake.
He turned their heart to hate his people, to conspire against his servants.
26 Yehova anatuma Mose mtumiki wake, ndi Aaroni amene Iye anamusankha.
He sent Moses, his servant, and Aaron, whom he had chosen.
27 Iwo anachita zizindikiro zozizwitsa pakati pawo, zodabwitsa zake mʼdziko la Hamu.
They performed miracles among them, and wonders in the land of Ham.
28 Yehova anatumiza mdima nasandutsa dziko kuti likhale la mdima. Koma anthuwo anakaniratu mawu a Yehova.
He sent darkness, and made it dark, but they rebelled against his words.
29 Yehova anasandutsa madzi awo kukhala magazi, kuchititsa kuti nsomba zawo zife.
He turned their waters into blood, and killed their fish.
30 Dziko lawo linadzaza ndi achule amene analowa mʼzipinda zogona za olamulira awo.
Their land swarmed with frogs, even in the chambers of their kings.
31 Iye anayankhula, ndipo kunabwera ntchentche zochuluka ndi nsabwe mʼdziko lawo lonse.
He spoke, and swarms of flies came, and gnats in all their territory.
32 Iyeyo anatembenuza mvula yawo kukhala matalala, ndi zingʼaningʼani mʼdziko lawo lonse;
He gave them hail for rain, flaming fire in their land.
33 Anagwetsa mitengo yawo ya mpesa ndi mitengo yawo ya mkuyu, nawononganso mitengo ina ya mʼdziko lawolo.
He struck their vines and also their fig trees, and shattered the trees of their country.
34 Iye anayankhula, ndipo dzombe linabwera, ziwala zosawerengeka;
He spoke, and the locusts came, and the grasshoppers, without number,
35 zinadya chilichonse chobiriwira cha mʼdziko lawo, zinadya zonse zotuluka mʼnthaka yawo.
ate up every plant in their land; and ate up the fruit of their ground.
36 Kenaka anakantha ana onse oyamba kubadwa a mʼdziko lawo, zipatso zoyamba za umunthu wawo wonse.
He struck also all the firstborn in their land, the first fruits of all their manhood.
37 Yehova anatulutsa Israeli, atatenga siliva ndi golide wambiri, ndipo pakati pa mafuko awo palibe mmodzi amene anafowoka.
And he brought them out with silver and gold, and there was no one among their tribes who stumbled.
38 Dziko la Igupto linakondwa pamene iwo anachoka, pakuti kuopsa kwa Israeli kunawagwera iwo.
Egypt was glad when they departed, for the fear of them had fallen on them.
39 Iye anatambasula mitambo ngati chofunda chawo, ndi moto owawunikira usiku.
He spread a cloud for a covering, fire to give light in the night.
40 Iwo anapempha, ndipo Iye anawabweretsera zinziri ndipo anawakhutitsa ndi chakudya chochokera kumwamba.
They asked, and he brought quails, and satisfied them with the bread of the sky.
41 Iye anatsekula thanthwe, ndipo madzi anatuluka; ngati mtsinje anayenda mʼchipululu.
He opened the rock, and waters gushed out. They ran as a river in the dry places.
42 Pakuti anakumbukira lonjezo lake loyera limene linaperekedwa kwa Abrahamu mtumiki wake.
For he remembered his holy word, and Abraham, his servant.
43 Iye anatulutsa anthu ake akukondwera, osankhika ake akufuwula mwachimwemwe;
He brought forth his people with joy, his chosen with singing.
44 Iye anawapatsa mayiko a anthu a mitundu ina ndipo anakhala olowamʼmalo a zimene ena anazivutikira,
He gave them the lands of the nations. They took the labor of the peoples in possession,
45 kuti iwo asunge malangizo ake ndi kutsatira malamulo ake. Tamandani Yehova.
that they might keep his statutes, and observe his laws. Praise the LORD.

< Masalimo 105 >