< Masalimo 105 >
1 Yamikani Yehova, itanani dzina lake; lalikirani pakati pa anthu a mitundu ina zimene Iye wachita.
Give the Lord thanks, worship his wonderful nature, let people know what he's done!
2 Imbirani Iye, imbani matamando kwa Iyeyo; fotokozani za machitidwe ake onse odabwitsa.
Sing to him, sing his praises; tell everyone the great things he's done!
3 Munyadire dzina lake loyera; mitima ya iwo amene amafunafuna Yehova ikondwere.
Be proud of his holy character; be happy, all who come to the Lord!
4 Dalirani Yehova ndi mphamvu zake; funafunani nkhope yake nthawi yonse.
Look for the Lord, and his strength; always look to be in his presence.
5 Kumbukirani zodabwitsa zimene Iye anazichita, zozizwitsa zake ndi maweruzo amene anapereka,
Remember all the wonderful things he's done, the miracles he's performed, and the judgments he's carried out,
6 inu zidzukulu za Abrahamu mtumiki wake, inu ana a Yakobo, osankhika ake.
descendants of Abraham, children of Israel, his chosen people.
7 Iye ndiye Yehova Mulungu wathu; maweruzo ake ali pa dziko lonse lapansi.
He is the Lord, our God, his judgments cover the whole earth.
8 Iyeyo amakumbukira pangano lake kwamuyaya, mawu amene analamula kwa mibado yonse,
He remembers his agreement forever, the promise he made lasts for a thousand generations;
9 pangano limene Iye anapanga ndi Abrahamu, lumbiro limene analumbira kwa Isake.
the agreement he made with Abraham, the vow he gave to Isaac.
10 Iye analitsimikiza kwa Yakobo monga zophunzitsa, kwa Israeli monga pangano lamuyaya:
The Lord legally confirmed it with Jacob, he made this binding agreement with Israel:
11 “Ndidzapereka kwa iwe dziko la Kanaani ngati gawo la cholowa chako.”
saying to you, “I will give the land of Canaan for you to possess.”
12 Pamene iwo anali ngati anthu ochepa mʼchiwerengero, ochepa ndithu, ndiponso alendo mʼdzikolo,
He said this when they were only a few, just a small group of foreigners in the land.
13 ankayendayenda kuchoka ku mtundu wina wa anthu ndi kupita ku mtundu wina, kuchoka mu ufumu wina kupita ku wina.
They wandered from country to country, from one kingdom to the next.
14 Iye sanalole wina aliyense kuwapondereza; anadzudzula mafumu chifukwa cha iwo:
He didn't let anyone one treat them badly; warning kings to leave them alone:
15 “Musakhudze odzozedwa anga; musachitire choyipa aneneri anga.”
“Don't touch my chosen people; don't harm my prophets!”
16 Iye anabweretsa njala pa dziko ndipo anawononga chakudya chonse;
He caused a famine in the Land of Canaan so that there was no food.
17 Iyeyo anatumiza munthu patsogolo pawo, Yosefe anagulitsidwa ngati kapolo.
Before that he sent a man, Joseph, who was sold as a slave.
18 Iwo anavulaza mapazi ake ndi matangadza, khosi lake analiyika mʼzitsulo,
They hurt his feet by placing them in shackles, and they put an iron collar around his neck,
19 mpaka zimene Iye ananeneratu zitakwaniritsidwa, mpaka mawu a Yehova ataonetsa kuti Iye ananena zoona.
until the time predicted came when the Lord tested him.
20 Mfumu inatuma munthu kukamumasula, wolamulira wa mitundu ya anthu anamasula iyeyo.
The king sent for him and released him; the king of the people set him free.
21 Anamuyika kukhala wolamulira nyumba yake, wolamulira zonse zimene iye anali nazo,
He put Joseph in charge of the royal household, manager of everything he had,
22 kulangiza ana a mfumu monga ankafunira ndi kuphunzitsa nzeru akuluakulu.
to teach the king's officials whatever he wanted, to make the king's advisors wise.
23 Tsono Israeli analowa mu Igupto; Yakobo anakhala monga mlendo mʼdziko la Hamu.
Then Israel entered Egypt—Jacob settled as a foreigner in the land of Ham.
24 Yehova anachulukitsa anthu ake; ndipo anachititsa kuti akhale ochuluka kwambiri kuposa adani awo;
The Lord made his people more fertile and more powerful than their enemies.
25 amene mitima yawo anayitembenuza kuti idane ndi anthu ake, kukonzera chiwembu atumiki ake.
He made the Egyptians change their minds and hate his people and act deceptively towards them.
26 Yehova anatuma Mose mtumiki wake, ndi Aaroni amene Iye anamusankha.
He sent his servant Moses, together with Aaron, whom he had chosen.
27 Iwo anachita zizindikiro zozizwitsa pakati pawo, zodabwitsa zake mʼdziko la Hamu.
They carried out his miraculous signs among the Egyptians, his wonders in the land of Ham.
28 Yehova anatumiza mdima nasandutsa dziko kuti likhale la mdima. Koma anthuwo anakaniratu mawu a Yehova.
He plunged the country into darkness—for hadn't they defied what the Lord had said?
29 Yehova anasandutsa madzi awo kukhala magazi, kuchititsa kuti nsomba zawo zife.
He turned their water into blood, killing all the fish.
30 Dziko lawo linadzaza ndi achule amene analowa mʼzipinda zogona za olamulira awo.
Then he sent a plague of frogs across the land that even entered the bedrooms of their rulers.
31 Iye anayankhula, ndipo kunabwera ntchentche zochuluka ndi nsabwe mʼdziko lawo lonse.
He gave the command, and flies spread throughout their land; mosquitoes were everywhere.
32 Iyeyo anatembenuza mvula yawo kukhala matalala, ndi zingʼaningʼani mʼdziko lawo lonse;
He rained down hail on them, and lightning flashed across their land.
33 Anagwetsa mitengo yawo ya mpesa ndi mitengo yawo ya mkuyu, nawononganso mitengo ina ya mʼdziko lawolo.
He struck down their grape vines, and tore down their trees.
34 Iye anayankhula, ndipo dzombe linabwera, ziwala zosawerengeka;
He gave the command, and swarms of locusts came—countless locusts:
35 zinadya chilichonse chobiriwira cha mʼdziko lawo, zinadya zonse zotuluka mʼnthaka yawo.
they ate up all the vegetation in their land; they consumed all the growing crops.
36 Kenaka anakantha ana onse oyamba kubadwa a mʼdziko lawo, zipatso zoyamba za umunthu wawo wonse.
He killed all the firstborn in Egypt, the first to be produced in their vigor and strength.
37 Yehova anatulutsa Israeli, atatenga siliva ndi golide wambiri, ndipo pakati pa mafuko awo palibe mmodzi amene anafowoka.
Then he led his people out of Egypt, carrying silver and gold—not one among the tribes was stumbling along.
38 Dziko la Igupto linakondwa pamene iwo anachoka, pakuti kuopsa kwa Israeli kunawagwera iwo.
The Egyptians were delighted to see them go, for they were frightened of the Israelites.
39 Iye anatambasula mitambo ngati chofunda chawo, ndi moto owawunikira usiku.
He spread a cloud above them as a covering, and at night a fire to give them light.
40 Iwo anapempha, ndipo Iye anawabweretsera zinziri ndipo anawakhutitsa ndi chakudya chochokera kumwamba.
He gave them quails to eat when they asked him; he fed them with the bread of heaven until they were full.
41 Iye anatsekula thanthwe, ndipo madzi anatuluka; ngati mtsinje anayenda mʼchipululu.
He split the rock open, and water gushed out—a river flowing through the desert.
42 Pakuti anakumbukira lonjezo lake loyera limene linaperekedwa kwa Abrahamu mtumiki wake.
For he remembered his holy promise to his servant Abraham.
43 Iye anatulutsa anthu ake akukondwera, osankhika ake akufuwula mwachimwemwe;
So he led his people out, his chosen ones, as they sang for joy.
44 Iye anawapatsa mayiko a anthu a mitundu ina ndipo anakhala olowamʼmalo a zimene ena anazivutikira,
He gave them the lands of the heathen nations, and they inherited what other people had worked for.
45 kuti iwo asunge malangizo ake ndi kutsatira malamulo ake. Tamandani Yehova.
The Lord did this so they could follow his instructions and keep his laws. Praise the Lord!