< Masalimo 105 >

1 Yamikani Yehova, itanani dzina lake; lalikirani pakati pa anthu a mitundu ina zimene Iye wachita.
Alleluia. Confess to the Lord, and invoke his name. Announce his works among the nations.
2 Imbirani Iye, imbani matamando kwa Iyeyo; fotokozani za machitidwe ake onse odabwitsa.
Sing to him, and sing psalms to him. Describe all his wonders.
3 Munyadire dzina lake loyera; mitima ya iwo amene amafunafuna Yehova ikondwere.
Be praised in his holy name. Let the heart of those who seek the Lord rejoice.
4 Dalirani Yehova ndi mphamvu zake; funafunani nkhope yake nthawi yonse.
Seek the Lord, and be confirmed. Seek his face always.
5 Kumbukirani zodabwitsa zimene Iye anazichita, zozizwitsa zake ndi maweruzo amene anapereka,
Remember his miracles, which he has done, his portents and the judgments of his mouth:
6 inu zidzukulu za Abrahamu mtumiki wake, inu ana a Yakobo, osankhika ake.
you offspring of Abraham his servant, you sons of Jacob his elect.
7 Iye ndiye Yehova Mulungu wathu; maweruzo ake ali pa dziko lonse lapansi.
He is the Lord our God. His judgments are throughout the entire earth.
8 Iyeyo amakumbukira pangano lake kwamuyaya, mawu amene analamula kwa mibado yonse,
He has remembered his covenant for all ages: the word that he entrusted to a thousand generations,
9 pangano limene Iye anapanga ndi Abrahamu, lumbiro limene analumbira kwa Isake.
which he assigned to Abraham, and his oath to Isaac.
10 Iye analitsimikiza kwa Yakobo monga zophunzitsa, kwa Israeli monga pangano lamuyaya:
And he stationed the same for Jacob with a precept, and for Israel with an eternal testament,
11 “Ndidzapereka kwa iwe dziko la Kanaani ngati gawo la cholowa chako.”
saying: To you, I will give the land of Canaan, the allotment of your inheritance.
12 Pamene iwo anali ngati anthu ochepa mʼchiwerengero, ochepa ndithu, ndiponso alendo mʼdzikolo,
Though they may have been but a small number, very few and foreigners there,
13 ankayendayenda kuchoka ku mtundu wina wa anthu ndi kupita ku mtundu wina, kuchoka mu ufumu wina kupita ku wina.
and though they passed from nation to nation, and from one kingdom to another people,
14 Iye sanalole wina aliyense kuwapondereza; anadzudzula mafumu chifukwa cha iwo:
he allowed no man to harm them, and he reproved kings on their behalf.
15 “Musakhudze odzozedwa anga; musachitire choyipa aneneri anga.”
Do not be willing to touch my Christ, and do not be willing to malign my prophets.
16 Iye anabweretsa njala pa dziko ndipo anawononga chakudya chonse;
And he called a famine upon the land, and he crushed every foundation of the bread.
17 Iyeyo anatumiza munthu patsogolo pawo, Yosefe anagulitsidwa ngati kapolo.
He sent a man before them: Joseph, who had been sold as a slave.
18 Iwo anavulaza mapazi ake ndi matangadza, khosi lake analiyika mʼzitsulo,
They humbled his feet in shackles; the iron pierced his soul,
19 mpaka zimene Iye ananeneratu zitakwaniritsidwa, mpaka mawu a Yehova ataonetsa kuti Iye ananena zoona.
until his word arrived. The eloquence of the Lord inflamed him.
20 Mfumu inatuma munthu kukamumasula, wolamulira wa mitundu ya anthu anamasula iyeyo.
The king sent and released him; he was the ruler of the people, and he dismissed him.
21 Anamuyika kukhala wolamulira nyumba yake, wolamulira zonse zimene iye anali nazo,
He established him as master of his house and ruler of all his possessions,
22 kulangiza ana a mfumu monga ankafunira ndi kuphunzitsa nzeru akuluakulu.
so that he might instruct his princes as himself, and teach his elders prudence.
23 Tsono Israeli analowa mu Igupto; Yakobo anakhala monga mlendo mʼdziko la Hamu.
And Israel entered into Egypt, and Jacob became a sojourner in the land of Ham.
24 Yehova anachulukitsa anthu ake; ndipo anachititsa kuti akhale ochuluka kwambiri kuposa adani awo;
And he helped his people greatly, and he strengthened them over their enemies.
25 amene mitima yawo anayitembenuza kuti idane ndi anthu ake, kukonzera chiwembu atumiki ake.
He turned their heart to hate his people, and to deal deceitfully with his servants.
26 Yehova anatuma Mose mtumiki wake, ndi Aaroni amene Iye anamusankha.
He sent Moses, his servant, and Aaron, the one whom he chose.
27 Iwo anachita zizindikiro zozizwitsa pakati pawo, zodabwitsa zake mʼdziko la Hamu.
He placed with them signs of his word, and portents in the land of Ham.
28 Yehova anatumiza mdima nasandutsa dziko kuti likhale la mdima. Koma anthuwo anakaniratu mawu a Yehova.
He sent darkness and made it conceal, and he did not afflict them with his speech.
29 Yehova anasandutsa madzi awo kukhala magazi, kuchititsa kuti nsomba zawo zife.
He turned their waters into blood, and he slaughtered their fish.
30 Dziko lawo linadzaza ndi achule amene analowa mʼzipinda zogona za olamulira awo.
Their land brought forth frogs, even in the inner chambers of their kings.
31 Iye anayankhula, ndipo kunabwera ntchentche zochuluka ndi nsabwe mʼdziko lawo lonse.
He spoke, and there came forth common flies and gnats, in every region.
32 Iyeyo anatembenuza mvula yawo kukhala matalala, ndi zingʼaningʼani mʼdziko lawo lonse;
He gave them a shower of hail and a burning fire, in the same land.
33 Anagwetsa mitengo yawo ya mpesa ndi mitengo yawo ya mkuyu, nawononganso mitengo ina ya mʼdziko lawolo.
And he struck their vineyards and their fig trees, and he crushed the trees of their region.
34 Iye anayankhula, ndipo dzombe linabwera, ziwala zosawerengeka;
He spoke, and the locust came forth, and the caterpillar, of which there was no number.
35 zinadya chilichonse chobiriwira cha mʼdziko lawo, zinadya zonse zotuluka mʼnthaka yawo.
And it devoured all the grass in their land, and it consumed all the fruit of their land.
36 Kenaka anakantha ana onse oyamba kubadwa a mʼdziko lawo, zipatso zoyamba za umunthu wawo wonse.
And he struck all the first-born in their land, the first-fruits of all their labor.
37 Yehova anatulutsa Israeli, atatenga siliva ndi golide wambiri, ndipo pakati pa mafuko awo palibe mmodzi amene anafowoka.
And he led them out with silver and gold, and there was not an infirm one among their tribes.
38 Dziko la Igupto linakondwa pamene iwo anachoka, pakuti kuopsa kwa Israeli kunawagwera iwo.
Egypt was joyful at their departure, for the fear of them lay heavy upon them.
39 Iye anatambasula mitambo ngati chofunda chawo, ndi moto owawunikira usiku.
He spread a cloud for their protection, and a fire, to give them light through the night.
40 Iwo anapempha, ndipo Iye anawabweretsera zinziri ndipo anawakhutitsa ndi chakudya chochokera kumwamba.
They petitioned, and the quail came; and he satisfied them with the bread of heaven.
41 Iye anatsekula thanthwe, ndipo madzi anatuluka; ngati mtsinje anayenda mʼchipululu.
He ruptured the rock and the waters flowed: rivers gushed in the dry land.
42 Pakuti anakumbukira lonjezo lake loyera limene linaperekedwa kwa Abrahamu mtumiki wake.
For he had called to mind his holy word, which he kept near to his servant Abraham.
43 Iye anatulutsa anthu ake akukondwera, osankhika ake akufuwula mwachimwemwe;
And he led forth his people in exultation, and his elect in rejoicing.
44 Iye anawapatsa mayiko a anthu a mitundu ina ndipo anakhala olowamʼmalo a zimene ena anazivutikira,
And he gave them the regions of the Gentiles, and they possessed the labors of the peoples,
45 kuti iwo asunge malangizo ake ndi kutsatira malamulo ake. Tamandani Yehova.
so that they might observe his justifications, and inquire about his law.

< Masalimo 105 >