< Masalimo 104 >

1 Tamanda Yehova, iwe moyo wanga. Inu Yehova Mulungu wanga, ndinu wamkulu kwambiri; mwavala ulemerero ndi ufumu.
¡Bendice a Yahvé, alma mía! ¡Yahvé, Dios mío, cuán grande eres! Te has vestido de majestad y de belleza,
2 Iye wadzifunditsa kuwala ngati chovala; watambasula miyamba ngati tenti
envuelto en luz como en un manto. Extendiste el cielo como un cortinaje;
3 ndipo wayika pa madzi mitanda ya chipinda chake. Iye amasandutsa mitambo kukhala galeta lake, ndi kuwuluka pa mapiko a mphepo.
construiste tu morada superior sobre las aguas, haces de las nubes tu carroza, cabalgas sobre las alas del viento.
4 Amapanga mphepo kukhala amithenga ake, malawi amoto kukhala atumiki ake.
A los vientos haces tus mensajeros, y ministros tuyos los relámpagos centellantes.
5 Anakhazikitsa dziko lapansi pa maziko ake; silingasunthike.
Cimentaste la tierra sobre sus bases de suerte que no vacile jamás.
6 Munaliphimba ndi nyanja yozama ngati chovala; madzi anayimirira pamwamba pa mapiri.
La habías cubierto con el océano como de un manto; las aguas se posaban sobre los montes.
7 Koma pakudzudzula kwanu madzi anathawa, pa mkokomo wa bingu lanu iwo anamwazika;
Mas huyeron a un grito tuyo, —temblaron a la voz de tu trueno,
8 Inu munamiza mapiri, iwo anatsikira ku zigwa kumalo kumene munawakonzera.
surgieron los montes, bajaron los valles—, hasta el lugar que les habías destinado.
9 Inu munayika malire ndipo sangathe kudutsa, iwo sadzamizanso dziko lapansi.
Les fijaste un límite que no traspasarán, para que no vuelvan a cubrir la tierra.
10 Iye achititsa akasupe kutulutsa madzi kupita ku zigwa; madziwo amayenda pakati pa mapiri.
Haces correr en arroyos las fuentes que brotan entre los montes,
11 Iwo amapereka madzi kwa zirombo zonse zakuthengo; abulu akuthengo amapha ludzu lawo.
para que beban todas las bestias del campo y sacien su sed los asnos monteses.
12 Mbalame zamlengalenga zimayika zisa mʼmbali mwa madzi; zimayimba pakati pa thambo.
A sus orillas posan las aves del cielo, que cantan entre el ramaje.
13 Iye amathirira mapiri kuchokera ku zipinda zake zapamwamba; dziko lapansi limakhutitsidwa ndi chipatso cha ntchito yake.
Desde tu morada riegas los montes; la tierra se sacia del fruto de tus obras.
14 Amameretsa udzu kuti ngʼombe zidye, ndi zomera, kuti munthu azilima kubweretsa chakudya kuchokera mʼdziko lapansi:
Produces el heno para los ganados, y las plantas que sirven al hombre, para que saque pan de la tierra,
15 vinyo amene amasangalatsa mtima wa munthu, mafuta amene amachititsa nkhope yake kuwala, ndi buledi amene amapereka mphamvu.
y vino que alegre el corazón del hombre; para que el aceite dé brillo a su rostro y el pan vigorice su corazón.
16 Mitengo ya Yehova ndi yothiriridwa bwino, mikungudza ya ku Lebanoni imene Iye anadzala.
Satúranse los árboles de Yahvé, los cedros del Líbano que Él plantó.
17 Mbalame zimamanga zisa zawo; kakowa ali ndi malo ake mʼmikungudzamo.
Las aves anidan en ellos; en los abetos tiene su casa la cigüeña.
18 Mapiri ataliatali ndi a mbalale; mʼmingʼalu ya miyala ndi mobisalamo mbira.
Los altos montes dan refugio a los antílopes, las peñas, a los conejos.
19 Mwezi umasiyanitsa nyengo ndipo dzuwa limadziwa nthawi yake yolowera.
Para señalar los tiempos, hiciste la luna; el sol conoce la hora de su ocaso.
20 Inu mumabweretsa mdima nukhala usiku, ndipo zirombo zonse za ku nkhalango zimatuluka.
Mandas las tinieblas, y viene la noche; en ellas rondan todas las fieras de las selvas.
21 Mikango imabangula kufuna nyama, ndi kufunafuna chakudya chawo kuchokera kwa Mulungu.
Los leoncillos rugen en pos de la presa, e imploran de Dios el sustento;
22 Dzuwa limatuluka ndipo iyo imapita kukabisala; imabwerera kukagona pansi mʼmapanga awo.
al salir el sol se retiran, y se tienden en sus madrigueras;
23 Pamenepo munthu amapita ku ntchito yake, kukagwira ntchito yake mpaka madzulo.
y el hombre acude a su trabajo, a su labranza, hasta la tarde.
24 Ntchito zanu ndi zochulukadi Inu Yehova! Munazipanga zonse mwanzeru, dziko lapansi ladzaza ndi zolengedwa zanu.
¡Cuán variadas son tus obras, oh Yahvé! Todo lo hiciste con sabiduría; llena está la tierra de tus riquezas.
25 Kuli nyanja yayikulu ndi yotambalala, yodzaza ndi zolengedwa zosawerengeka, zamoyo zanu zazikulu ndi zazingʼono zomwe.
Mira el mar, grande y anchuroso: allí un hormiguear sin número, de animales pequeños y grandes.
26 Kumeneko sitima zapamadzi zimayenda uku ndi uku, ndiponso Leviyatani amene munamulenga kuti asewere kumeneko.
Allí transitan las naves, y ese leviatán que creaste para que en él juguetease.
27 Zonsezi zimayangʼana kwa Inu kuti muzipatse chakudya chawo pa nthawi yake yoyenera.
Todos esperan de Ti que a su tiempo les des el alimento.
28 Mukazipatsa, zimachisonkhanitsa pamodzi; mukatsekula dzanja lanu, izo zimakhutitsidwa ndi zinthu zabwino.
Se lo das y ellos lo toman; al abrir Tú la mano se hartan de bienes.
29 Mukabisa nkhope yanu, izo zimachita mantha aakulu; mukachotsa mpweya wawo, zimafa ndi kubwerera ku fumbi.
Si Tú escondes el rostro, desfallecen; si retiras Tú su aliento, expiran, y vuelven a su polvo.
30 Mukatumiza mzimu wanu, izo zimalengedwa ndipo mumakozanso maonekedwe a dziko lapansi.
Cuando envías tu soplo, son creados, y renuevas la faz de la tierra.
31 Ulemerero wa Yehova ukhalebe mpaka muyaya; Yehova akondwere ndi ntchito ya manja ake;
Sea eterna la gloria de Yahvé; gócese Yahvé en sus obras.
32 Iye amene amayangʼana dziko lapansi ndipo limanjenjemera, amene amakhudza mapiri ndipo amatuluka utsi.
Mira Él a la tierra, y ella tiembla; toca Él los montes, y humean.
33 Ine ndidzayimbira Yehova moyo wanga wonse; ndidzayimbira matamando Mulungu wanga nthawi yonse imene ndili ndi moyo.
A Yahvé cantaré mientras viva; tañeré salmos a mi Dios mientras yo tenga el ser.
34 Zolingalira zanga zikhale zomukomera Iye, pamene ndikusangalala mwa Yehova.
Séanle gratos mis acentos! Yo en Yahvé me gozaré.
35 Koma anthu ochimwa awonongeke pa dziko lapansi ndipo anthu oyipa asapezekenso. Tamanda Yehova, Iwe moyo wanga. Tamandani Yehova.
¡Sean quitados de la tierra los pecadores y no haya más impíos! ¡Bendice, alma mía, a Yahvé! ¡Hallelú Yah!

< Masalimo 104 >