< Masalimo 104 >
1 Tamanda Yehova, iwe moyo wanga. Inu Yehova Mulungu wanga, ndinu wamkulu kwambiri; mwavala ulemerero ndi ufumu.
Blagoslavljaj, duša moja Gospoda. Gospod, Bog moj, velik si silno, lepoto in veličastvo si oblekel.
2 Iye wadzifunditsa kuwala ngati chovala; watambasula miyamba ngati tenti
Odevaš se z lučjo kakor z obleko; nebesa razpenjaš kakor zagrinjalo;
3 ndipo wayika pa madzi mitanda ya chipinda chake. Iye amasandutsa mitambo kukhala galeta lake, ndi kuwuluka pa mapiko a mphepo.
Kateri stavi v vode gornje hrame svoje; kateri nareja oblake za voz svoj, kateri hodéva po vetrov perotih,
4 Amapanga mphepo kukhala amithenga ake, malawi amoto kukhala atumiki ake.
Kateri dela vetrove za poslance svoje, za služabnike svoje ogenj plameneči,
5 Anakhazikitsa dziko lapansi pa maziko ake; silingasunthike.
Ustanovil je zemljo na podstave njene, da se ne gane na vedno večne čase.
6 Munaliphimba ndi nyanja yozama ngati chovala; madzi anayimirira pamwamba pa mapiri.
Z breznom si jo bil odél kakor z odejo, ko so vode stale čez gore.
7 Koma pakudzudzula kwanu madzi anathawa, pa mkokomo wa bingu lanu iwo anamwazika;
Na karanje tvoje so pobegnile, pred groma tvojega glasom bežale so urno.
8 Inu munamiza mapiri, iwo anatsikira ku zigwa kumalo kumene munawakonzera.
Dvignile so se gore, pogreznile se doline na mesto, katero si jim bil ustanovil.
9 Inu munayika malire ndipo sangathe kudutsa, iwo sadzamizanso dziko lapansi.
Mejo si postavil, da ne idejo čez, da se ne povrnejo, pokrit zemljo;
10 Iye achititsa akasupe kutulutsa madzi kupita ku zigwa; madziwo amayenda pakati pa mapiri.
Kateri izpuščaš studence po dolinah, da hodijo med gorami.
11 Iwo amapereka madzi kwa zirombo zonse zakuthengo; abulu akuthengo amapha ludzu lawo.
Napajajo naj vse poljske živali; žejo svojo gasé divji osli.
12 Mbalame zamlengalenga zimayika zisa mʼmbali mwa madzi; zimayimba pakati pa thambo.
Poleg njih prebivajo tice nebeške, glasijo se iz med listja.
13 Iye amathirira mapiri kuchokera ku zipinda zake zapamwamba; dziko lapansi limakhutitsidwa ndi chipatso cha ntchito yake.
Kateri móči goré iz gornjih hramov svojih, da se sè sadom dél tvojih zemlja pase.
14 Amameretsa udzu kuti ngʼombe zidye, ndi zomera, kuti munthu azilima kubweretsa chakudya kuchokera mʼdziko lapansi:
Daješ, da seno raste živini, in zelišče človeku za rabo, da jemlje hrano iz zemlje;
15 vinyo amene amasangalatsa mtima wa munthu, mafuta amene amachititsa nkhope yake kuwala, ndi buledi amene amapereka mphamvu.
Kateri z vinom razveseljuje srce človeku; z oljem svetlo dela čelo, in z jedjo podpira srce človeku.
16 Mitengo ya Yehova ndi yothiriridwa bwino, mikungudza ya ku Lebanoni imene Iye anadzala.
Siti se drevje Gospodovo; cedre na Libanonu, katere je vsadil;
17 Mbalame zimamanga zisa zawo; kakowa ali ndi malo ake mʼmikungudzamo.
(Kjer gnezdijo tički), jelke prebivališče štorklji,
18 Mapiri ataliatali ndi a mbalale; mʼmingʼalu ya miyala ndi mobisalamo mbira.
Gore previsoke divjim kozlom, skale prebivališče gorskim mišim.
19 Mwezi umasiyanitsa nyengo ndipo dzuwa limadziwa nthawi yake yolowera.
Postavil je mesec za čase gotove, solnce, ki pozna záhod svoj.
20 Inu mumabweretsa mdima nukhala usiku, ndipo zirombo zonse za ku nkhalango zimatuluka.
Temé narejaš, da je noč, ko prilezejo vse gozdne živali.
21 Mikango imabangula kufuna nyama, ndi kufunafuna chakudya chawo kuchokera kwa Mulungu.
Mladi levi rjoveč po plenu, in iskajoč od Boga mogočnega hrane svoje.
22 Dzuwa limatuluka ndipo iyo imapita kukabisala; imabwerera kukagona pansi mʼmapanga awo.
O solnčnem vzhodu se poskrijejo in ležé v brlogih svojih.
23 Pamenepo munthu amapita ku ntchito yake, kukagwira ntchito yake mpaka madzulo.
Človek gre na delo svoje, in na polje svoje do večera.
24 Ntchito zanu ndi zochulukadi Inu Yehova! Munazipanga zonse mwanzeru, dziko lapansi ladzaza ndi zolengedwa zanu.
Kako veličastna so dela tvoja, o Gospod; kako modro si jih naredil vsa; kako polna je zemlja posesti tvoje!
25 Kuli nyanja yayikulu ndi yotambalala, yodzaza ndi zolengedwa zosawerengeka, zamoyo zanu zazikulu ndi zazingʼono zomwe.
V morji samem velikem in prostornem: tu so lazeče živali, in brez števila živali z velikimi male.
26 Kumeneko sitima zapamadzi zimayenda uku ndi uku, ndiponso Leviyatani amene munamulenga kuti asewere kumeneko.
Tod hodijo ladije; som, katerega si ustvaril, igrá se v njem.
27 Zonsezi zimayangʼana kwa Inu kuti muzipatse chakudya chawo pa nthawi yake yoyenera.
Vse tó čaka tebe, da jim daš živeža o svojem času.
28 Mukazipatsa, zimachisonkhanitsa pamodzi; mukatsekula dzanja lanu, izo zimakhutitsidwa ndi zinthu zabwino.
Ko jim daješ ti, pobirajo; ko jim odpreš roko svojo sitijo se z dobroto.
29 Mukabisa nkhope yanu, izo zimachita mantha aakulu; mukachotsa mpweya wawo, zimafa ndi kubwerera ku fumbi.
Ko jim skriješ obličje svoje, zbegajo se; ko jim vzameš sapo, ginejo in povračajo se v svoj prah.
30 Mukatumiza mzimu wanu, izo zimalengedwa ndipo mumakozanso maonekedwe a dziko lapansi.
Ko izpuščaš sapo svojo, oživljajo se, obličje obnavljaš zemlji.
31 Ulemerero wa Yehova ukhalebe mpaka muyaya; Yehova akondwere ndi ntchito ya manja ake;
Čast bodi Gospodu vekomaj; raduj se, Gospod, v delih svojih!
32 Iye amene amayangʼana dziko lapansi ndipo limanjenjemera, amene amakhudza mapiri ndipo amatuluka utsi.
Ko pogleda na zemljo, trese se ona; ko se dotakne gorâ, kadé se.
33 Ine ndidzayimbira Yehova moyo wanga wonse; ndidzayimbira matamando Mulungu wanga nthawi yonse imene ndili ndi moyo.
Pel bodem Gospodu v življenji svojem; prepeval Bogu svojemu, dokler bodem.
34 Zolingalira zanga zikhale zomukomera Iye, pamene ndikusangalala mwa Yehova.
Prijetno bode o njem premišljevanje moje, radoval se bodem jaz v Gospodu.
35 Koma anthu ochimwa awonongeke pa dziko lapansi ndipo anthu oyipa asapezekenso. Tamanda Yehova, Iwe moyo wanga. Tamandani Yehova.
Izginejo naj grešniki sè zemlje, in krivičnih več ne bódi; blagoslavljaj, duša moja, Gospoda. Aleluja!