< Masalimo 104 >
1 Tamanda Yehova, iwe moyo wanga. Inu Yehova Mulungu wanga, ndinu wamkulu kwambiri; mwavala ulemerero ndi ufumu.
Abençoa Yahweh, minha alma. Yahweh, meu Deus, você é muito grande. Você está vestida com honra e majestade.
2 Iye wadzifunditsa kuwala ngati chovala; watambasula miyamba ngati tenti
Ele se cobre de luz como com uma peça de vestuário. Ele estica os céus como uma cortina.
3 ndipo wayika pa madzi mitanda ya chipinda chake. Iye amasandutsa mitambo kukhala galeta lake, ndi kuwuluka pa mapiko a mphepo.
Ele coloca as vigas de seus quartos nas águas. Ele faz das nuvens sua carruagem. Ele caminha sobre as asas do vento.
4 Amapanga mphepo kukhala amithenga ake, malawi amoto kukhala atumiki ake.
Ele faz ventos de seus mensageiros, e seus servos chamas de fogo.
5 Anakhazikitsa dziko lapansi pa maziko ake; silingasunthike.
Ele lançou os alicerces da terra, que não deve ser movida para sempre.
6 Munaliphimba ndi nyanja yozama ngati chovala; madzi anayimirira pamwamba pa mapiri.
Você a cobriu com o fundo como com um manto. As águas ficavam acima das montanhas.
7 Koma pakudzudzula kwanu madzi anathawa, pa mkokomo wa bingu lanu iwo anamwazika;
Na sua repreensão eles fugiram. À voz de seu trovão, eles se apressaram.
8 Inu munamiza mapiri, iwo anatsikira ku zigwa kumalo kumene munawakonzera.
As montanhas subiram, os vales se afundaram, para o local que lhes havia sido designado.
9 Inu munayika malire ndipo sangathe kudutsa, iwo sadzamizanso dziko lapansi.
Você estabeleceu um limite que eles não podem ultrapassar, que eles não se viram novamente para cobrir a terra.
10 Iye achititsa akasupe kutulutsa madzi kupita ku zigwa; madziwo amayenda pakati pa mapiri.
Ele envia molas para os vales. Eles correm entre as montanhas.
11 Iwo amapereka madzi kwa zirombo zonse zakuthengo; abulu akuthengo amapha ludzu lawo.
Eles dão de beber a cada animal do campo. Os burros selvagens saciam sua sede.
12 Mbalame zamlengalenga zimayika zisa mʼmbali mwa madzi; zimayimba pakati pa thambo.
As aves do céu nidificam por elas. Eles cantam entre os galhos.
13 Iye amathirira mapiri kuchokera ku zipinda zake zapamwamba; dziko lapansi limakhutitsidwa ndi chipatso cha ntchito yake.
Ele rega as montanhas de seus quartos. A terra é preenchida com o fruto de suas obras.
14 Amameretsa udzu kuti ngʼombe zidye, ndi zomera, kuti munthu azilima kubweretsa chakudya kuchokera mʼdziko lapansi:
Ele faz com que a grama cresça para o gado, e plantas para o homem cultivar, que ele possa produzir alimentos a partir da terra:
15 vinyo amene amasangalatsa mtima wa munthu, mafuta amene amachititsa nkhope yake kuwala, ndi buledi amene amapereka mphamvu.
vinho que faz o coração do homem feliz, óleo para fazer seu rosto brilhar, e pão que fortalece o coração do homem.
16 Mitengo ya Yehova ndi yothiriridwa bwino, mikungudza ya ku Lebanoni imene Iye anadzala.
As árvores de Yahweh estão bem regadas, os cedros do Líbano, que ele plantou,
17 Mbalame zimamanga zisa zawo; kakowa ali ndi malo ake mʼmikungudzamo.
onde as aves fazem seus ninhos. A cegonha faz sua casa nos ciprestes.
18 Mapiri ataliatali ndi a mbalale; mʼmingʼalu ya miyala ndi mobisalamo mbira.
As altas montanhas são para os caprinos selvagens. As rochas são um refúgio para os texugos das rochas.
19 Mwezi umasiyanitsa nyengo ndipo dzuwa limadziwa nthawi yake yolowera.
Ele indicou a lua para as estações do ano. O sol sabe quando se pôr.
20 Inu mumabweretsa mdima nukhala usiku, ndipo zirombo zonse za ku nkhalango zimatuluka.
Você faz escuridão, e é noite, em que todos os animais da floresta rondam.
21 Mikango imabangula kufuna nyama, ndi kufunafuna chakudya chawo kuchokera kwa Mulungu.
Os jovens leões rugem depois de suas presas, e buscar seu alimento de Deus.
22 Dzuwa limatuluka ndipo iyo imapita kukabisala; imabwerera kukagona pansi mʼmapanga awo.
O sol nasce, e eles roubam, e deitar-se em suas covas.
23 Pamenepo munthu amapita ku ntchito yake, kukagwira ntchito yake mpaka madzulo.
O homem sai para o seu trabalho, ao seu trabalho até a noite.
24 Ntchito zanu ndi zochulukadi Inu Yehova! Munazipanga zonse mwanzeru, dziko lapansi ladzaza ndi zolengedwa zanu.
Yahweh, quantos são seus trabalhos! Em sabedoria, você os fez todos. A terra está cheia de suas riquezas.
25 Kuli nyanja yayikulu ndi yotambalala, yodzaza ndi zolengedwa zosawerengeka, zamoyo zanu zazikulu ndi zazingʼono zomwe.
Há o mar, grande e largo, em que são inumeráveis seres vivos, tanto pequenos como grandes animais.
26 Kumeneko sitima zapamadzi zimayenda uku ndi uku, ndiponso Leviyatani amene munamulenga kuti asewere kumeneko.
Lá vão os navios, e leviatã, que você formou para tocar lá.
27 Zonsezi zimayangʼana kwa Inu kuti muzipatse chakudya chawo pa nthawi yake yoyenera.
Todos estes aguardam por você, que você pode dar-lhes seus alimentos na época certa.
28 Mukazipatsa, zimachisonkhanitsa pamodzi; mukatsekula dzanja lanu, izo zimakhutitsidwa ndi zinthu zabwino.
Você dá a eles; eles se reúnem. Você abre sua mão; eles estão satisfeitos com o bem.
29 Mukabisa nkhope yanu, izo zimachita mantha aakulu; mukachotsa mpweya wawo, zimafa ndi kubwerera ku fumbi.
Você esconde seu rosto; eles são perturbados. Você lhes tira o fôlego; eles morrem e voltam para o pó.
30 Mukatumiza mzimu wanu, izo zimalengedwa ndipo mumakozanso maonekedwe a dziko lapansi.
Você envia seu Espírito e eles são criados. Você renova a face do chão.
31 Ulemerero wa Yehova ukhalebe mpaka muyaya; Yehova akondwere ndi ntchito ya manja ake;
Que a glória de Yahweh perdure para sempre. Que Yahweh se regozije com suas obras.
32 Iye amene amayangʼana dziko lapansi ndipo limanjenjemera, amene amakhudza mapiri ndipo amatuluka utsi.
Ele olha para a terra, e ela treme. Ele toca as montanhas, e elas fumam.
33 Ine ndidzayimbira Yehova moyo wanga wonse; ndidzayimbira matamando Mulungu wanga nthawi yonse imene ndili ndi moyo.
Vou cantar para Yahweh enquanto viver. Cantarei louvores ao meu Deus enquanto eu tiver qualquer ser.
34 Zolingalira zanga zikhale zomukomera Iye, pamene ndikusangalala mwa Yehova.
Que minha meditação seja doce para ele. Eu me regozijarei em Yahweh.
35 Koma anthu ochimwa awonongeke pa dziko lapansi ndipo anthu oyipa asapezekenso. Tamanda Yehova, Iwe moyo wanga. Tamandani Yehova.
Que os pecadores sejam consumidos fora da terra. Que os ímpios não sejam mais. Abençoado Yahweh, minha alma. Louvado seja Yah!