< Masalimo 104 >

1 Tamanda Yehova, iwe moyo wanga. Inu Yehova Mulungu wanga, ndinu wamkulu kwambiri; mwavala ulemerero ndi ufumu.
ای جان من، خداوند را متبارک بخوان! ای یهوه خدای من توبی نهایت عظیم هستی! به عزت و جلال ملبس هستی.۱
2 Iye wadzifunditsa kuwala ngati chovala; watambasula miyamba ngati tenti
خویشتن را به نور مثل ردا پوشانیده‌ای.۲
3 ndipo wayika pa madzi mitanda ya chipinda chake. Iye amasandutsa mitambo kukhala galeta lake, ndi kuwuluka pa mapiko a mphepo.
آن که غرفات خود را بر آبها بنا کرده است و ابرها رامرکب خود نموده و بر بالهای باد می‌خرامد.۳
4 Amapanga mphepo kukhala amithenga ake, malawi amoto kukhala atumiki ake.
فرشتگان خود را بادها می‌گرداند و خادمان خود را آتش مشتعل.۴
5 Anakhazikitsa dziko lapansi pa maziko ake; silingasunthike.
که زمین را بر اساسش استوار کرده، تا جنبش نخورد تا ابدالاباد.۵
6 Munaliphimba ndi nyanja yozama ngati chovala; madzi anayimirira pamwamba pa mapiri.
آن رابه لجه‌ها مثل ردا پوشانیده‌ای، که آبها بر کوههاایستاده‌اند.۶
7 Koma pakudzudzula kwanu madzi anathawa, pa mkokomo wa bingu lanu iwo anamwazika;
از عتاب تو می‌گریزند. از آواز رعدتو پراکنده می‌شوند.۷
8 Inu munamiza mapiri, iwo anatsikira ku zigwa kumalo kumene munawakonzera.
به فراز کوهها برمی آیند، وبه همواریها فرود می‌آیند، به مکانی که برای آنهامهیا ساخته‌ای.۸
9 Inu munayika malire ndipo sangathe kudutsa, iwo sadzamizanso dziko lapansi.
حدی برای آنها قرار داده‌ای که از آن نگذرند و برنگردند تا زمین را بپوشانند.۹
10 Iye achititsa akasupe kutulutsa madzi kupita ku zigwa; madziwo amayenda pakati pa mapiri.
که چشمه‌ها را در وادیها جاری می‌سازد تا درمیان کوهها روان بشوند.۱۰
11 Iwo amapereka madzi kwa zirombo zonse zakuthengo; abulu akuthengo amapha ludzu lawo.
تمام حیوانات صحرارا سیراب می‌سازند تا گورخران تشنگی خود رافرو نشانند.۱۱
12 Mbalame zamlengalenga zimayika zisa mʼmbali mwa madzi; zimayimba pakati pa thambo.
بر آنها مرغان هوا ساکن می‌شوند واز میان شاخه‌ها آواز خود را می‌دهند.۱۲
13 Iye amathirira mapiri kuchokera ku zipinda zake zapamwamba; dziko lapansi limakhutitsidwa ndi chipatso cha ntchito yake.
او ازغرفات خود کوهها را سیراب می‌کند و از ثمرات اعمال تو زمین سیر می‌شود.۱۳
14 Amameretsa udzu kuti ngʼombe zidye, ndi zomera, kuti munthu azilima kubweretsa chakudya kuchokera mʼdziko lapansi:
نباتات را برای بهایم می‌رویاند و سبزه‌ها رابرای خدمت انسان، و نان را از زمین بیرون می‌آورد.۱۴
15 vinyo amene amasangalatsa mtima wa munthu, mafuta amene amachititsa nkhope yake kuwala, ndi buledi amene amapereka mphamvu.
و شراب را که دل انسان را شادمان می‌کند، و چهره او را به روغن شاداب می‌سازد ودل انسان را به نان قوی می‌گرداند.۱۵
16 Mitengo ya Yehova ndi yothiriridwa bwino, mikungudza ya ku Lebanoni imene Iye anadzala.
درختان خداوند شادابند، یعنی سروهای آزاد لبنان که غرس کرده است،۱۶
17 Mbalame zimamanga zisa zawo; kakowa ali ndi malo ake mʼmikungudzamo.
که در آنها مرغان آشیانهای خود را می‌گیرند و اما صنوبر خانه لق لق می‌باشد.۱۷
18 Mapiri ataliatali ndi a mbalale; mʼmingʼalu ya miyala ndi mobisalamo mbira.
کوههای بلند برای بزهای کوهی و صخره هابرای یربوع ملجاء است.۱۸
19 Mwezi umasiyanitsa nyengo ndipo dzuwa limadziwa nthawi yake yolowera.
ماه را برای موسمهاساخت و آفتاب مغرب خود را می‌داند.۱۹
20 Inu mumabweretsa mdima nukhala usiku, ndipo zirombo zonse za ku nkhalango zimatuluka.
تاریکی می‌سازی و شب می‌شود که در آن همه حیوانات جنگلی راه می‌روند.۲۰
21 Mikango imabangula kufuna nyama, ndi kufunafuna chakudya chawo kuchokera kwa Mulungu.
شیربچگان برای شکار خود غرش می‌کنند و خوراک خویش را از خدا می‌جویند.۲۱
22 Dzuwa limatuluka ndipo iyo imapita kukabisala; imabwerera kukagona pansi mʼmapanga awo.
چون آفتاب طلوع می‌کند جمع می‌شوند و در بیشه های خودمی خوابند.۲۲
23 Pamenepo munthu amapita ku ntchito yake, kukagwira ntchito yake mpaka madzulo.
انسان برای عمل خود بیرون می‌آید و به جهت شغل خویش تا شامگاه.۲۳
24 Ntchito zanu ndi zochulukadi Inu Yehova! Munazipanga zonse mwanzeru, dziko lapansi ladzaza ndi zolengedwa zanu.
‌ای خداوند اعمال تو چه بسیار است. جمیع آنها را به حکمت کرده‌ای. زمین از دولت تو پر است.۲۴
25 Kuli nyanja yayikulu ndi yotambalala, yodzaza ndi zolengedwa zosawerengeka, zamoyo zanu zazikulu ndi zazingʼono zomwe.
و آن دریای بزرگ و وسیع الاطراف نیز که در آن حشرات از حد شماره زیاده‌اند و حیوانات خرد و بزرگ.۲۵
26 Kumeneko sitima zapamadzi zimayenda uku ndi uku, ndiponso Leviyatani amene munamulenga kuti asewere kumeneko.
و در آن کشتیها راه می‌روند و آن لویاتان که به جهت بازی کردن در آن آفریده‌ای.۲۶
27 Zonsezi zimayangʼana kwa Inu kuti muzipatse chakudya chawo pa nthawi yake yoyenera.
جمیع اینها از تو انتظارمی کشند تا خوراک آنها را در وقتش برسانی.۲۷
28 Mukazipatsa, zimachisonkhanitsa pamodzi; mukatsekula dzanja lanu, izo zimakhutitsidwa ndi zinthu zabwino.
آنچه را که به آنها می‌دهی، فرا می‌گیرند. دست خود را باز می‌کنی، پس از چیزهای نیکو سیرمی شوند.۲۸
29 Mukabisa nkhope yanu, izo zimachita mantha aakulu; mukachotsa mpweya wawo, zimafa ndi kubwerera ku fumbi.
روی خود را می‌پوشانی پس مضطرب می‌گردند. روح آنها را قبض می‌کنی، پس می‌میرند و به خاک خود برمی گردند.۲۹
30 Mukatumiza mzimu wanu, izo zimalengedwa ndipo mumakozanso maonekedwe a dziko lapansi.
چون روح خود را می‌فرستی، آفریده می‌شوند و روی زمین را تازه می‌گردانی.۳۰
31 Ulemerero wa Yehova ukhalebe mpaka muyaya; Yehova akondwere ndi ntchito ya manja ake;
جلال خداوند تا ابدالاباد است. خداوند ازاعمال خود راضی خواهد بود.۳۱
32 Iye amene amayangʼana dziko lapansi ndipo limanjenjemera, amene amakhudza mapiri ndipo amatuluka utsi.
که به زمین نگاه می‌کند و آن می‌لرزد. کوهها را لمس می‌کند، پس آتش فشان می‌شوند.۳۲
33 Ine ndidzayimbira Yehova moyo wanga wonse; ndidzayimbira matamando Mulungu wanga nthawi yonse imene ndili ndi moyo.
خداوند را خواهم سرایید تا زنده می‌باشم. برای خدای خود تسبیح خواهم خواند تا وجود دارم.۳۳
34 Zolingalira zanga zikhale zomukomera Iye, pamene ndikusangalala mwa Yehova.
تفکر من او رالذیذ بشود و من در خداوند شادمان خواهم بود.۳۴
35 Koma anthu ochimwa awonongeke pa dziko lapansi ndipo anthu oyipa asapezekenso. Tamanda Yehova, Iwe moyo wanga. Tamandani Yehova.
گناهکاران از زمین نابود گردند و شریران دیگر یافت نشوند. ای جان من، خداوند را متبارک بخوان! هللویاه!۳۵

< Masalimo 104 >