< Masalimo 104 >
1 Tamanda Yehova, iwe moyo wanga. Inu Yehova Mulungu wanga, ndinu wamkulu kwambiri; mwavala ulemerero ndi ufumu.
Psalmus David. Benedic anima mea Domino: Domine Deus meus magnificatus es vehementer. Confessionem, et decorem induisti:
2 Iye wadzifunditsa kuwala ngati chovala; watambasula miyamba ngati tenti
amictus lumine sicut vestimento: Extendens caelum sicut pellem:
3 ndipo wayika pa madzi mitanda ya chipinda chake. Iye amasandutsa mitambo kukhala galeta lake, ndi kuwuluka pa mapiko a mphepo.
qui tegis aquis superiora eius. Qui ponis nubem ascensum tuum: qui ambulas super pennas ventorum.
4 Amapanga mphepo kukhala amithenga ake, malawi amoto kukhala atumiki ake.
Qui facis angelos tuos, spiritus: et ministros tuos ignem urentem.
5 Anakhazikitsa dziko lapansi pa maziko ake; silingasunthike.
Qui fundasti terram super stabilitatem suam: non inclinabitur in saeculum saeculi.
6 Munaliphimba ndi nyanja yozama ngati chovala; madzi anayimirira pamwamba pa mapiri.
Abyssus, sicut vestimentum, amictus eius: super montes stabunt aquae.
7 Koma pakudzudzula kwanu madzi anathawa, pa mkokomo wa bingu lanu iwo anamwazika;
Ab increpatione tua fugient: a voce tonitrui tui formidabunt.
8 Inu munamiza mapiri, iwo anatsikira ku zigwa kumalo kumene munawakonzera.
Ascendunt montes: et descendunt campi in locum, quem fundasti eis.
9 Inu munayika malire ndipo sangathe kudutsa, iwo sadzamizanso dziko lapansi.
Terminum posuisti, quem non transgredientur: neque convertentur operire terram.
10 Iye achititsa akasupe kutulutsa madzi kupita ku zigwa; madziwo amayenda pakati pa mapiri.
Qui emittis fontes in convallibus: inter medium montium pertransibunt aquae.
11 Iwo amapereka madzi kwa zirombo zonse zakuthengo; abulu akuthengo amapha ludzu lawo.
Potabunt omnes bestiae agri: expectabunt onagri in siti sua.
12 Mbalame zamlengalenga zimayika zisa mʼmbali mwa madzi; zimayimba pakati pa thambo.
Super ea volucres caeli habitabunt: de medio petrarum dabunt voces.
13 Iye amathirira mapiri kuchokera ku zipinda zake zapamwamba; dziko lapansi limakhutitsidwa ndi chipatso cha ntchito yake.
Rigans montes de superioribus suis: de fructu operum tuorum satiabitur terra:
14 Amameretsa udzu kuti ngʼombe zidye, ndi zomera, kuti munthu azilima kubweretsa chakudya kuchokera mʼdziko lapansi:
Producens foenum iumentis, et herbam servituti hominum: Ut educas panem de terra:
15 vinyo amene amasangalatsa mtima wa munthu, mafuta amene amachititsa nkhope yake kuwala, ndi buledi amene amapereka mphamvu.
et vinum laetificet cor hominis: Ut exhilaret faciem in oleo: et panis cor hominis confirmet.
16 Mitengo ya Yehova ndi yothiriridwa bwino, mikungudza ya ku Lebanoni imene Iye anadzala.
Saturabuntur ligna campi, et cedri Libani, quas plantavit:
17 Mbalame zimamanga zisa zawo; kakowa ali ndi malo ake mʼmikungudzamo.
illic passeres nidificabunt. Herodii domus dux est eorum:
18 Mapiri ataliatali ndi a mbalale; mʼmingʼalu ya miyala ndi mobisalamo mbira.
montes excelsi cervis: petra refugium herinaciis.
19 Mwezi umasiyanitsa nyengo ndipo dzuwa limadziwa nthawi yake yolowera.
Fecit lunam in tempora: sol cognovit occasum suum.
20 Inu mumabweretsa mdima nukhala usiku, ndipo zirombo zonse za ku nkhalango zimatuluka.
Posuisti tenebras, et facta est nox: in ipsa pertransibunt omnes bestiae silvae.
21 Mikango imabangula kufuna nyama, ndi kufunafuna chakudya chawo kuchokera kwa Mulungu.
Catuli leonum rugientes, ut rapiant, et quaerant a Deo escam sibi.
22 Dzuwa limatuluka ndipo iyo imapita kukabisala; imabwerera kukagona pansi mʼmapanga awo.
Ortus est sol, et congregati sunt: et in cubilibus suis collocabuntur.
23 Pamenepo munthu amapita ku ntchito yake, kukagwira ntchito yake mpaka madzulo.
Exibit homo ad opus suum: et ad operationem suam usque ad vesperum.
24 Ntchito zanu ndi zochulukadi Inu Yehova! Munazipanga zonse mwanzeru, dziko lapansi ladzaza ndi zolengedwa zanu.
Quam magnificata sunt opera tua Domine! omnia in sapientia fecisti: impleta est terra possessione tua.
25 Kuli nyanja yayikulu ndi yotambalala, yodzaza ndi zolengedwa zosawerengeka, zamoyo zanu zazikulu ndi zazingʼono zomwe.
Hoc mare magnum, et spatiosum manibus: illic reptilia, quorum non est numerus. Animalia pusilla cum magnis:
26 Kumeneko sitima zapamadzi zimayenda uku ndi uku, ndiponso Leviyatani amene munamulenga kuti asewere kumeneko.
illic naves pertransibunt. Draco iste, quem formasti ad illudendum ei:
27 Zonsezi zimayangʼana kwa Inu kuti muzipatse chakudya chawo pa nthawi yake yoyenera.
omnia a te expectant ut des illis escam in tempore.
28 Mukazipatsa, zimachisonkhanitsa pamodzi; mukatsekula dzanja lanu, izo zimakhutitsidwa ndi zinthu zabwino.
Dante te illis, colligent: aperiente te manum tuam, omnia implebuntur bonitate.
29 Mukabisa nkhope yanu, izo zimachita mantha aakulu; mukachotsa mpweya wawo, zimafa ndi kubwerera ku fumbi.
Avertente autem te faciem, turbabuntur: auferes spiritum eorum, et deficient, et in pulverem suum revertentur.
30 Mukatumiza mzimu wanu, izo zimalengedwa ndipo mumakozanso maonekedwe a dziko lapansi.
Emittes spiritum tuum, et creabuntur: et renovabis faciem terrae.
31 Ulemerero wa Yehova ukhalebe mpaka muyaya; Yehova akondwere ndi ntchito ya manja ake;
Sit gloria Domini in saeculum: laetabitur Dominus in operibus suis:
32 Iye amene amayangʼana dziko lapansi ndipo limanjenjemera, amene amakhudza mapiri ndipo amatuluka utsi.
Qui respicit terram, et facit eam tremere: qui tangit montes, et fumigant.
33 Ine ndidzayimbira Yehova moyo wanga wonse; ndidzayimbira matamando Mulungu wanga nthawi yonse imene ndili ndi moyo.
Cantabo Domino in vita mea: psallam Deo meo quamdiu sum.
34 Zolingalira zanga zikhale zomukomera Iye, pamene ndikusangalala mwa Yehova.
Iucundum sit ei eloquium meum: ego vero delectabor in Domino.
35 Koma anthu ochimwa awonongeke pa dziko lapansi ndipo anthu oyipa asapezekenso. Tamanda Yehova, Iwe moyo wanga. Tamandani Yehova.
Deficiant peccatores a terra, et iniqui ita ut non sint: benedic anima mea Domino.