< Masalimo 104 >

1 Tamanda Yehova, iwe moyo wanga. Inu Yehova Mulungu wanga, ndinu wamkulu kwambiri; mwavala ulemerero ndi ufumu.
E Iehova, e kuu Akua e, ua nui loa no oe; Ua kahikoia no oe i ka nani a me ka hanohano.
2 Iye wadzifunditsa kuwala ngati chovala; watambasula miyamba ngati tenti
Ua uhiia no oe i ka malamalama me he kapa la; Ua hohola no oe i na lani me he paku la.
3 ndipo wayika pa madzi mitanda ya chipinda chake. Iye amasandutsa mitambo kukhala galeta lake, ndi kuwuluka pa mapiko a mphepo.
Ua haua no oia i kona mau keena kiekie ma na wai; Ua kau aku no hoi i na ao maluna i kaa mau nona: A ua holoholo me na eheu o ka makani.
4 Amapanga mphepo kukhala amithenga ake, malawi amoto kukhala atumiki ake.
Ua hana oia i kona poe elele, he makani; A i kona poe kahuns hoi, he lapalapa ahi;
5 Anakhazikitsa dziko lapansi pa maziko ake; silingasunthike.
Ua hoopaa oia i ka honua maluna o kona kumu, I ole ia e nauweuwe, a mau loa aku.
6 Munaliphimba ndi nyanja yozama ngati chovala; madzi anayimirira pamwamba pa mapiri.
A ua uhi no oe ia i ka hohonu, me he kapa la: Ku mai la na wai, maluna o na mauna.
7 Koma pakudzudzula kwanu madzi anathawa, pa mkokomo wa bingu lanu iwo anamwazika;
I kou papa ana, holo no lakou; I ka leo o kou hekili, auhee aku la lakou.
8 Inu munamiza mapiri, iwo anatsikira ku zigwa kumalo kumene munawakonzera.
Ea mai la no maluna o na mauna; A emi iho la ma na awawa ilalo, A i kahi au i hookumu ai no lakou.
9 Inu munayika malire ndipo sangathe kudutsa, iwo sadzamizanso dziko lapansi.
Ua kau pale oe i mokuna no lakou. I ole lakou e hala'e; I ole hoi e hoi hou mai, a uhi i ka honua.
10 Iye achititsa akasupe kutulutsa madzi kupita ku zigwa; madziwo amayenda pakati pa mapiri.
Kuu mai la oia i na waipuna ma na awawa, I kahe mai lakou, mawaena o na mauna.
11 Iwo amapereka madzi kwa zirombo zonse zakuthengo; abulu akuthengo amapha ludzu lawo.
Hoohainu no lakou i na holoholona a pau o ke kula; A hooana no hoi na hoki hihiu i ko lakou makewai.
12 Mbalame zamlengalenga zimayika zisa mʼmbali mwa madzi; zimayimba pakati pa thambo.
Maluna olaila na manu o ka lewa e hoopunana'i, A kani hoi ko lakou leo iwaena o na lala.
13 Iye amathirira mapiri kuchokera ku zipinda zake zapamwamba; dziko lapansi limakhutitsidwa ndi chipatso cha ntchito yake.
Ua hoomauu mai no oia i ua mauna, mailoko mai o kona waihonawai; Ua maona hoi ka aina i ka hua o kau hana ana.
14 Amameretsa udzu kuti ngʼombe zidye, ndi zomera, kuti munthu azilima kubweretsa chakudya kuchokera mʼdziko lapansi:
Nana no i hooulu mai ka mauu no na holoholona, A me ka mea uli hoi i pono ai na kanaka: I hoopuka mai ai oia i ka ai mailoko mai o ka honua,
15 vinyo amene amasangalatsa mtima wa munthu, mafuta amene amachititsa nkhope yake kuwala, ndi buledi amene amapereka mphamvu.
A me ka waina hoi i mea e olioli ai ko na kanaka naau, A me ka aila hoi, i mea e hinuhinu ai kana maka, A me ka berena, ka mea e hooikaika ai ka naau o na kanaka.
16 Mitengo ya Yehova ndi yothiriridwa bwino, mikungudza ya ku Lebanoni imene Iye anadzala.
Ua kena no na laau o Iehova, Na kedera hoi o Lebanona, na mea ana i kanu ai;
17 Mbalame zimamanga zisa zawo; kakowa ali ndi malo ake mʼmikungudzamo.
Malaila no e hoopunana'i na manu; O ke kikonia, o na laau kaa kona hale.
18 Mapiri ataliatali ndi a mbalale; mʼmingʼalu ya miyala ndi mobisalamo mbira.
O na mauna kiekie ka puuhonua o na kao hihiu; A o na pohaku hoi ko na rabita.
19 Mwezi umasiyanitsa nyengo ndipo dzuwa limadziwa nthawi yake yolowera.
Nana no i hana i na mahina no na kau; Ua ike no ka la i kona napoo ana.
20 Inu mumabweretsa mdima nukhala usiku, ndipo zirombo zonse za ku nkhalango zimatuluka.
Lawe mai no oe i ka pouli, a ua po; Ia manawa, kolo mai na mea kolo a pau o ka nahelehele.
21 Mikango imabangula kufuna nyama, ndi kufunafuna chakudya chawo kuchokera kwa Mulungu.
Uwo mai la hoi na liona opiopio i ko lakou wahi, A imi hoi i ka ai, mai ke Akua mai.
22 Dzuwa limatuluka ndipo iyo imapita kukabisala; imabwerera kukagona pansi mʼmapanga awo.
Puka mai la ka la, alaila, akoakoa lakou, A moe no lakou, ma ko lakou ana.
23 Pamenepo munthu amapita ku ntchito yake, kukagwira ntchito yake mpaka madzulo.
Hele aku no ke kanaka i kana hana, A i kona hooikaika hoi, a ahiahi.
24 Ntchito zanu ndi zochulukadi Inu Yehova! Munazipanga zonse mwanzeru, dziko lapansi ladzaza ndi zolengedwa zanu.
Nani ka nui o kau mau hana, e Iehova! Ma ke akamai i hana mai ai oe ia mau mea a pau: Ua piha hoi ka honua i kau waiwai.
25 Kuli nyanja yayikulu ndi yotambalala, yodzaza ndi zolengedwa zosawerengeka, zamoyo zanu zazikulu ndi zazingʼono zomwe.
A me keia moana nui hoi, a palahalaha, Malaila no na mea kolo, pau ole i ka heluia, A me na mea ola, he liilii, a he nui no hoi.
26 Kumeneko sitima zapamadzi zimayenda uku ndi uku, ndiponso Leviyatani amene munamulenga kuti asewere kumeneko.
Malaila no na moku e holo ae; Aia hoi kela leviatana au i hana'i, e paani ilaila.
27 Zonsezi zimayangʼana kwa Inu kuti muzipatse chakudya chawo pa nthawi yake yoyenera.
Kakali no keia poe a pau ia oe, I haawi mai ai oe i ka lakou ai i ka wa pono.
28 Mukazipatsa, zimachisonkhanitsa pamodzi; mukatsekula dzanja lanu, izo zimakhutitsidwa ndi zinthu zabwino.
O ka mea au e haawi mai ai na lakou, oia ka lakou e hooiliili iho; Wehe no oe i kou lima, a lako iho la lakou i ka maikai.
29 Mukabisa nkhope yanu, izo zimachita mantha aakulu; mukachotsa mpweya wawo, zimafa ndi kubwerera ku fumbi.
I huna oe i kou maka, make koke iho la lakou; Lawe oe i ko lakou ea, make no lakou, a hoi hou i ka lepo.
30 Mukatumiza mzimu wanu, izo zimalengedwa ndipo mumakozanso maonekedwe a dziko lapansi.
Hoouna mai oe i kou ea, ua hanaia iho la lakou; A nau no hoi i hoano hou i ka mnka o ka honua.
31 Ulemerero wa Yehova ukhalebe mpaka muyaya; Yehova akondwere ndi ntchito ya manja ake;
E mau loa ana no ka nani o Iehova; E lealea mai no o Iehova i kana mau hana.
32 Iye amene amayangʼana dziko lapansi ndipo limanjenjemera, amene amakhudza mapiri ndipo amatuluka utsi.
Nana mai no oia i ka honua, a haalulu iho la ia; Hoopa mai oia i na mauna, uwahi ae la lakou.
33 Ine ndidzayimbira Yehova moyo wanga wonse; ndidzayimbira matamando Mulungu wanga nthawi yonse imene ndili ndi moyo.
E oli aku au ia Iehova i ka manawa o ko'u ola ana; E hoolea no hoi au i ke Akua, a i ko'u hopena,
34 Zolingalira zanga zikhale zomukomera Iye, pamene ndikusangalala mwa Yehova.
He mea ono ko'u noonoo ana ia ia; A ma Iehova no wau e lealea ai.
35 Koma anthu ochimwa awonongeke pa dziko lapansi ndipo anthu oyipa asapezekenso. Tamanda Yehova, Iwe moyo wanga. Tamandani Yehova.
E hookiia'e ka poe hewa mai ka honua aku, O ka poe lawehala hoi, aole e koe lakou. E hoomaikai aku ia Iehova, e kuu uhane: E halelu aku oukou ia Iehova.

< Masalimo 104 >