< Masalimo 104 >

1 Tamanda Yehova, iwe moyo wanga. Inu Yehova Mulungu wanga, ndinu wamkulu kwambiri; mwavala ulemerero ndi ufumu.
Bénis, mon âme, l’Eternel! Eternel, mon Dieu, tu es infiniment grand; tu es vêtu de splendeur et de majesté.
2 Iye wadzifunditsa kuwala ngati chovala; watambasula miyamba ngati tenti
Tu t’enveloppes de lumière comme d’un manteau, tu déploies les cieux comme une tenture.
3 ndipo wayika pa madzi mitanda ya chipinda chake. Iye amasandutsa mitambo kukhala galeta lake, ndi kuwuluka pa mapiko a mphepo.
Sur les eaux tu as posé les voûtes de ta demeure sublime, les nuages te servent de char, tu t’avances sur les ailes du vent.
4 Amapanga mphepo kukhala amithenga ake, malawi amoto kukhala atumiki ake.
Des vents tu fais tes messagers; des flammes ardentes, tes ministres.
5 Anakhazikitsa dziko lapansi pa maziko ake; silingasunthike.
Tu as fondé la terre sur ses colonnes d’appui, pour qu’elle ne chancelle jamais.
6 Munaliphimba ndi nyanja yozama ngati chovala; madzi anayimirira pamwamba pa mapiri.
Tu l’as couverte de flots comme d’un vêtement; sur les montagnes les eaux s’étaient arrêtées.
7 Koma pakudzudzula kwanu madzi anathawa, pa mkokomo wa bingu lanu iwo anamwazika;
A ton injonction elles s’enfuirent; au bruit de ton tonnerre, elles s’élancèrent éperdues.
8 Inu munamiza mapiri, iwo anatsikira ku zigwa kumalo kumene munawakonzera.
Des montagnes s’élevèrent, des vallées s’abaissèrent, occupant la place que tu leur avais assignée.
9 Inu munayika malire ndipo sangathe kudutsa, iwo sadzamizanso dziko lapansi.
Tu leur as fixé des barrières infranchissables, pour les empêcher de submerger à nouveau la terre.
10 Iye achititsa akasupe kutulutsa madzi kupita ku zigwa; madziwo amayenda pakati pa mapiri.
Tu fais jaillir des sources dans les vallées, elles poursuivent leur course entre les montagnes.
11 Iwo amapereka madzi kwa zirombo zonse zakuthengo; abulu akuthengo amapha ludzu lawo.
Elles abreuvent toutes les bêtes des champs, les onagres y étanchent leur soif.
12 Mbalame zamlengalenga zimayika zisa mʼmbali mwa madzi; zimayimba pakati pa thambo.
Sur leurs bords, les oiseaux du ciel font leur demeure; d’entre la feuillée, ils élèvent leur ramage.
13 Iye amathirira mapiri kuchokera ku zipinda zake zapamwamba; dziko lapansi limakhutitsidwa ndi chipatso cha ntchito yake.
Du haut de ta résidence tu arroses les montagnes, la terre est nourrie du fruit de tes œuvres.
14 Amameretsa udzu kuti ngʼombe zidye, ndi zomera, kuti munthu azilima kubweretsa chakudya kuchokera mʼdziko lapansi:
Tu fais croître l’herbe pour les animaux domestiques, des plantes pour l’usage de l’homme, en tirant sa nourriture du sein de la terre:
15 vinyo amene amasangalatsa mtima wa munthu, mafuta amene amachititsa nkhope yake kuwala, ndi buledi amene amapereka mphamvu.
le vin qui réjouit le cœur des mortels, l’huile qui fait resplendir les visages, le pain enfin qui fortifie le cœur de l’homme.
16 Mitengo ya Yehova ndi yothiriridwa bwino, mikungudza ya ku Lebanoni imene Iye anadzala.
Les arbres de l’Eternel sont abondamment pourvus, les cèdres du Liban que sa main a plantés.
17 Mbalame zimamanga zisa zawo; kakowa ali ndi malo ake mʼmikungudzamo.
Là les oiseaux bâtissent leurs nids, la cigogne fait des cyprès sa demeure.
18 Mapiri ataliatali ndi a mbalale; mʼmingʼalu ya miyala ndi mobisalamo mbira.
Les montagnes escarpées servent de retraite aux chamois, les rochers de refuge aux gerboises.
19 Mwezi umasiyanitsa nyengo ndipo dzuwa limadziwa nthawi yake yolowera.
Il a fait la lune pour marquer les temps, le soleil connaît le terme de sa course.
20 Inu mumabweretsa mdima nukhala usiku, ndipo zirombo zonse za ku nkhalango zimatuluka.
Tu amènes les ténèbres, et c’est la nuit, la nuit, où circulent tous les hôtes de la forêt.
21 Mikango imabangula kufuna nyama, ndi kufunafuna chakudya chawo kuchokera kwa Mulungu.
Les lionceaux rugissent après la proie, demandant à Dieu leur pâture.
22 Dzuwa limatuluka ndipo iyo imapita kukabisala; imabwerera kukagona pansi mʼmapanga awo.
Le soleil commence à poindre, ils se retirent, et vont se blottir dans leurs tanières;
23 Pamenepo munthu amapita ku ntchito yake, kukagwira ntchito yake mpaka madzulo.
l’homme se rend à son labeur, accomplit sa besogne jusqu’au soir.
24 Ntchito zanu ndi zochulukadi Inu Yehova! Munazipanga zonse mwanzeru, dziko lapansi ladzaza ndi zolengedwa zanu.
Que tes œuvres sont grandes, ô Seigneur! Toutes, tu les as faites avec sagesse; la terre est remplie de tes créations.
25 Kuli nyanja yayikulu ndi yotambalala, yodzaza ndi zolengedwa zosawerengeka, zamoyo zanu zazikulu ndi zazingʼono zomwe.
Voici le grand océan, aux étendues immenses! Là fourmillent des êtres sans nombre, des bêtes petites et grandes.
26 Kumeneko sitima zapamadzi zimayenda uku ndi uku, ndiponso Leviyatani amene munamulenga kuti asewere kumeneko.
Là cheminent des navires, ce Léviathan que tu as formé pour s’y ébattre.
27 Zonsezi zimayangʼana kwa Inu kuti muzipatse chakudya chawo pa nthawi yake yoyenera.
Tous mettent en toi leur attente, assurés que tu leur donneras leur nourriture en temps voulu.
28 Mukazipatsa, zimachisonkhanitsa pamodzi; mukatsekula dzanja lanu, izo zimakhutitsidwa ndi zinthu zabwino.
Tu la leur donnes, ils la recueillent; tu ouvres la main, ils sont comblés de biens.
29 Mukabisa nkhope yanu, izo zimachita mantha aakulu; mukachotsa mpweya wawo, zimafa ndi kubwerera ku fumbi.
Tu dérobes ta face, ils sont dans l’épouvante; tu leur retires le souffle, ils expirent et retombent dans leur poussière.
30 Mukatumiza mzimu wanu, izo zimalengedwa ndipo mumakozanso maonekedwe a dziko lapansi.
Tu renvoies ton souffle, ils renaissent, et tu renouvelles la face de la terre!
31 Ulemerero wa Yehova ukhalebe mpaka muyaya; Yehova akondwere ndi ntchito ya manja ake;
Que la gloire de l’Eternel dure à jamais! Que le Seigneur se réjouisse de ses œuvres!
32 Iye amene amayangʼana dziko lapansi ndipo limanjenjemera, amene amakhudza mapiri ndipo amatuluka utsi.
Il regarde la terre, et elle vacille, il effleure les montagnes, et elles fument.
33 Ine ndidzayimbira Yehova moyo wanga wonse; ndidzayimbira matamando Mulungu wanga nthawi yonse imene ndili ndi moyo.
Je veux chanter l’Eternel ma vie durant, célébrer mon Dieu tant que j’existerai.
34 Zolingalira zanga zikhale zomukomera Iye, pamene ndikusangalala mwa Yehova.
Puisse mon cantique lui être agréable! Moi, je me délecte en l’Eternel.
35 Koma anthu ochimwa awonongeke pa dziko lapansi ndipo anthu oyipa asapezekenso. Tamanda Yehova, Iwe moyo wanga. Tamandani Yehova.
Que les pécheurs disparaissent de la terre, que les méchants ne soient plus! Mon âme, bénis l’Eternel, Alléluia!

< Masalimo 104 >