< Masalimo 104 >

1 Tamanda Yehova, iwe moyo wanga. Inu Yehova Mulungu wanga, ndinu wamkulu kwambiri; mwavala ulemerero ndi ufumu.
Bénis Yahvé, mon âme. Yahvé, mon Dieu, tu es très grand. Tu es vêtu d'honneur et de majesté.
2 Iye wadzifunditsa kuwala ngati chovala; watambasula miyamba ngati tenti
Il se couvre de lumière comme d'un vêtement. Il étend les cieux comme un rideau.
3 ndipo wayika pa madzi mitanda ya chipinda chake. Iye amasandutsa mitambo kukhala galeta lake, ndi kuwuluka pa mapiko a mphepo.
Il pose les poutres de ses chambres dans les eaux. Il fait des nuages son char. Il marche sur les ailes du vent.
4 Amapanga mphepo kukhala amithenga ake, malawi amoto kukhala atumiki ake.
Il fait de ses messagers des vents, et ses serviteurs des flammes de feu.
5 Anakhazikitsa dziko lapansi pa maziko ake; silingasunthike.
Il a posé les fondations de la terre, qu'il ne devrait pas être déplacé pour toujours.
6 Munaliphimba ndi nyanja yozama ngati chovala; madzi anayimirira pamwamba pa mapiri.
Tu l'as couvert de l'abîme comme d'un manteau. Les eaux s'élevaient au-dessus des montagnes.
7 Koma pakudzudzula kwanu madzi anathawa, pa mkokomo wa bingu lanu iwo anamwazika;
A ta réprimande, ils se sont enfuis. À la voix de votre tonnerre, ils se sont précipités.
8 Inu munamiza mapiri, iwo anatsikira ku zigwa kumalo kumene munawakonzera.
Les montagnes se sont élevées, les vallées se sont effondrées, à la place que vous leur aviez assignée.
9 Inu munayika malire ndipo sangathe kudutsa, iwo sadzamizanso dziko lapansi.
Tu as fixé une frontière qu'ils ne pourront pas franchir, qu'ils ne se retournent pas pour recouvrir la terre.
10 Iye achititsa akasupe kutulutsa madzi kupita ku zigwa; madziwo amayenda pakati pa mapiri.
Il fait jaillir des sources dans les vallées. Ils courent entre les montagnes.
11 Iwo amapereka madzi kwa zirombo zonse zakuthengo; abulu akuthengo amapha ludzu lawo.
Ils donnent à boire à tous les animaux des champs. Les ânes sauvages étanchent leur soif.
12 Mbalame zamlengalenga zimayika zisa mʼmbali mwa madzi; zimayimba pakati pa thambo.
Les oiseaux du ciel font leur nid près d'eux. Ils chantent parmi les branches.
13 Iye amathirira mapiri kuchokera ku zipinda zake zapamwamba; dziko lapansi limakhutitsidwa ndi chipatso cha ntchito yake.
Il arrose les montagnes depuis ses chambres. La terre est remplie du fruit de tes œuvres.
14 Amameretsa udzu kuti ngʼombe zidye, ndi zomera, kuti munthu azilima kubweretsa chakudya kuchokera mʼdziko lapansi:
Il fait pousser l'herbe pour le bétail, et des plantes que l'homme peut cultiver, pour qu'il produise de la nourriture à partir de la terre:
15 vinyo amene amasangalatsa mtima wa munthu, mafuta amene amachititsa nkhope yake kuwala, ndi buledi amene amapereka mphamvu.
le vin qui réjouit le cœur de l'homme, de l'huile pour faire briller son visage, et le pain qui fortifie le cœur de l'homme.
16 Mitengo ya Yehova ndi yothiriridwa bwino, mikungudza ya ku Lebanoni imene Iye anadzala.
Les arbres de Yahvé sont bien arrosés, les cèdres du Liban, qu'il a plantés,
17 Mbalame zimamanga zisa zawo; kakowa ali ndi malo ake mʼmikungudzamo.
où les oiseaux font leurs nids. La cigogne a élu domicile dans les cyprès.
18 Mapiri ataliatali ndi a mbalale; mʼmingʼalu ya miyala ndi mobisalamo mbira.
Les hautes montagnes sont pour les boucs sauvages. Les rochers sont un refuge pour les blaireaux des rochers.
19 Mwezi umasiyanitsa nyengo ndipo dzuwa limadziwa nthawi yake yolowera.
Il a établi la lune pour les saisons. Le soleil sait quand se coucher.
20 Inu mumabweretsa mdima nukhala usiku, ndipo zirombo zonse za ku nkhalango zimatuluka.
Tu fais des ténèbres, et c'est la nuit, dans lequel tous les animaux de la forêt rôdent.
21 Mikango imabangula kufuna nyama, ndi kufunafuna chakudya chawo kuchokera kwa Mulungu.
Les jeunes lions rugissent après leur proie, et cherchent leur nourriture auprès de Dieu.
22 Dzuwa limatuluka ndipo iyo imapita kukabisala; imabwerera kukagona pansi mʼmapanga awo.
Le soleil se lève, et ils s'enfuient, et se couchent dans leurs tanières.
23 Pamenepo munthu amapita ku ntchito yake, kukagwira ntchito yake mpaka madzulo.
L'homme se rend à son travail, à son travail jusqu'au soir.
24 Ntchito zanu ndi zochulukadi Inu Yehova! Munazipanga zonse mwanzeru, dziko lapansi ladzaza ndi zolengedwa zanu.
Yahvé, que tes œuvres sont nombreuses! Dans la sagesse, vous les avez tous créés. La terre est pleine de vos richesses.
25 Kuli nyanja yayikulu ndi yotambalala, yodzaza ndi zolengedwa zosawerengeka, zamoyo zanu zazikulu ndi zazingʼono zomwe.
Voilà la mer, grande et large, dans laquelle se trouvent d'innombrables êtres vivants, les petits et les grands animaux.
26 Kumeneko sitima zapamadzi zimayenda uku ndi uku, ndiponso Leviyatani amene munamulenga kuti asewere kumeneko.
C'est là que vont les navires, et leviathan, que vous avez formé pour y jouer.
27 Zonsezi zimayangʼana kwa Inu kuti muzipatse chakudya chawo pa nthawi yake yoyenera.
Ils t'attendent tous, afin que vous leur donniez leur nourriture en temps voulu.
28 Mukazipatsa, zimachisonkhanitsa pamodzi; mukatsekula dzanja lanu, izo zimakhutitsidwa ndi zinthu zabwino.
Tu leur donnes, ils recueillent. Vous ouvrez votre main; ils sont satisfaits du bien.
29 Mukabisa nkhope yanu, izo zimachita mantha aakulu; mukachotsa mpweya wawo, zimafa ndi kubwerera ku fumbi.
Vous cachez votre visage, ils sont troublés. Vous leur coupez le souffle, ils meurent et retournent à la poussière.
30 Mukatumiza mzimu wanu, izo zimalengedwa ndipo mumakozanso maonekedwe a dziko lapansi.
Tu envoies ton Esprit et ils sont créés. Vous renouvelez la surface du sol.
31 Ulemerero wa Yehova ukhalebe mpaka muyaya; Yehova akondwere ndi ntchito ya manja ake;
Que la gloire de Yahvé dure à jamais. Que Yahvé se réjouisse de ses œuvres.
32 Iye amene amayangʼana dziko lapansi ndipo limanjenjemera, amene amakhudza mapiri ndipo amatuluka utsi.
Il regarde la terre, et elle tremble. Il touche les montagnes, et elles fument.
33 Ine ndidzayimbira Yehova moyo wanga wonse; ndidzayimbira matamando Mulungu wanga nthawi yonse imene ndili ndi moyo.
Je chanterai à Yahvé aussi longtemps que je vivrai. Je chanterai les louanges de mon Dieu tant que j'ai un être.
34 Zolingalira zanga zikhale zomukomera Iye, pamene ndikusangalala mwa Yehova.
Que ma méditation lui soit douce. Je me réjouirai en Yahvé.
35 Koma anthu ochimwa awonongeke pa dziko lapansi ndipo anthu oyipa asapezekenso. Tamanda Yehova, Iwe moyo wanga. Tamandani Yehova.
Que les pécheurs disparaissent de la terre! Que les méchants ne soient plus. Bénis Yahvé, mon âme. Louez Yah!

< Masalimo 104 >