< Masalimo 104 >
1 Tamanda Yehova, iwe moyo wanga. Inu Yehova Mulungu wanga, ndinu wamkulu kwambiri; mwavala ulemerero ndi ufumu.
Bless, O my soul, the Lord. O Lord my God, thou art very great; with glory and majesty art thou clothed.
2 Iye wadzifunditsa kuwala ngati chovala; watambasula miyamba ngati tenti
[Thou art he] who wrappeth himself in light as with a garment; who stretcheth out the heavens like a curtain;
3 ndipo wayika pa madzi mitanda ya chipinda chake. Iye amasandutsa mitambo kukhala galeta lake, ndi kuwuluka pa mapiko a mphepo.
Who frameth of the waters the beams of his upper-chambers; who maketh the clouds his chariot; who walketh along upon the wings of the wind:
4 Amapanga mphepo kukhala amithenga ake, malawi amoto kukhala atumiki ake.
Who maketh the winds his messengers; the flaming fire his ministers;
5 Anakhazikitsa dziko lapansi pa maziko ake; silingasunthike.
Who hath founded the earth upon her bases, that she should not be moved to all eternity.
6 Munaliphimba ndi nyanja yozama ngati chovala; madzi anayimirira pamwamba pa mapiri.
Thou hadst covered the deep as with a garment: above the mountains stood the waters.
7 Koma pakudzudzula kwanu madzi anathawa, pa mkokomo wa bingu lanu iwo anamwazika;
At thy rebuke they fled, at the voice of thy thunder they hastened away.
8 Inu munamiza mapiri, iwo anatsikira ku zigwa kumalo kumene munawakonzera.
They ascended mountains; they went down valleys, unto the place which thou hadst founded for them.
9 Inu munayika malire ndipo sangathe kudutsa, iwo sadzamizanso dziko lapansi.
Bounds hast thou set which they cannot pass over, that they return not again to cover the earth.
10 Iye achititsa akasupe kutulutsa madzi kupita ku zigwa; madziwo amayenda pakati pa mapiri.
[Thou art he] who sendeth springs into the valleys, between mountains they run along.
11 Iwo amapereka madzi kwa zirombo zonse zakuthengo; abulu akuthengo amapha ludzu lawo.
They give drink to all the beasts of the field: the wild asses quench [thereon] their thirst.
12 Mbalame zamlengalenga zimayika zisa mʼmbali mwa madzi; zimayimba pakati pa thambo.
By them have the fowls of the heaven ever their habitation, from between the branches they send forth their voice.
13 Iye amathirira mapiri kuchokera ku zipinda zake zapamwamba; dziko lapansi limakhutitsidwa ndi chipatso cha ntchito yake.
Who watereth the mountains from his upper-chambers: from the fruit of thy works is the earth satisfied.
14 Amameretsa udzu kuti ngʼombe zidye, ndi zomera, kuti munthu azilima kubweretsa chakudya kuchokera mʼdziko lapansi:
[Thou art he] who causeth grass to grow for the cattle, and herbs by the service of man, that he may bring forth bread out of the earth;
15 vinyo amene amasangalatsa mtima wa munthu, mafuta amene amachititsa nkhope yake kuwala, ndi buledi amene amapereka mphamvu.
And wine that maketh joyful the heart of man, [and] oil to brighten his face, and bread which strengtheneth the heart of man.
16 Mitengo ya Yehova ndi yothiriridwa bwino, mikungudza ya ku Lebanoni imene Iye anadzala.
Full of sap are the trees of the Lord, the cedars of Lebanon which he hath planted;
17 Mbalame zimamanga zisa zawo; kakowa ali ndi malo ake mʼmikungudzamo.
Where the birds make their nests: the stork—fir-trees are her house.
18 Mapiri ataliatali ndi a mbalale; mʼmingʼalu ya miyala ndi mobisalamo mbira.
The high mountains are for the wild goats: the rocks are a shelter for the conies.
19 Mwezi umasiyanitsa nyengo ndipo dzuwa limadziwa nthawi yake yolowera.
He hath made the moon for seasons: the sun knoweth his going down.
20 Inu mumabweretsa mdima nukhala usiku, ndipo zirombo zonse za ku nkhalango zimatuluka.
Thou causest darkness, and it becometh night, wherein creep forth all the beasts of the forest.
21 Mikango imabangula kufuna nyama, ndi kufunafuna chakudya chawo kuchokera kwa Mulungu.
The young lions roar after their prey, and ask from God their food.
22 Dzuwa limatuluka ndipo iyo imapita kukabisala; imabwerera kukagona pansi mʼmapanga awo.
The sun ariseth, they withdraw [to their lairs], and lie down in their dens.
23 Pamenepo munthu amapita ku ntchito yake, kukagwira ntchito yake mpaka madzulo.
Man goeth [then] forth unto his work, and to his labor until the evening.
24 Ntchito zanu ndi zochulukadi Inu Yehova! Munazipanga zonse mwanzeru, dziko lapansi ladzaza ndi zolengedwa zanu.
How manifold are thy works, O Lord! in wisdom hast thou made them all: the earth is full of thy riches.
25 Kuli nyanja yayikulu ndi yotambalala, yodzaza ndi zolengedwa zosawerengeka, zamoyo zanu zazikulu ndi zazingʼono zomwe.
Here is this great and wide-extended sea; therein are moving things without number, living creatures both small and great.
26 Kumeneko sitima zapamadzi zimayenda uku ndi uku, ndiponso Leviyatani amene munamulenga kuti asewere kumeneko.
There the ships make their way: [there also] is the leviathan, whom thou hast made to sport therein.
27 Zonsezi zimayangʼana kwa Inu kuti muzipatse chakudya chawo pa nthawi yake yoyenera.
All of these wait upon thee, to give them their food in its due season.
28 Mukazipatsa, zimachisonkhanitsa pamodzi; mukatsekula dzanja lanu, izo zimakhutitsidwa ndi zinthu zabwino.
What thou givest them they gather: thou openest thy hand, they are satisfied with good.
29 Mukabisa nkhope yanu, izo zimachita mantha aakulu; mukachotsa mpweya wawo, zimafa ndi kubwerera ku fumbi.
Thou hidest thy face, they suddenly vanish: thou takest away their spirit, they perish, and to their dust they return.
30 Mukatumiza mzimu wanu, izo zimalengedwa ndipo mumakozanso maonekedwe a dziko lapansi.
Thou sendest forth thy spirit, they are created; and thou renewest the face of the earth.
31 Ulemerero wa Yehova ukhalebe mpaka muyaya; Yehova akondwere ndi ntchito ya manja ake;
The glory of the Lord will endure for ever; the Lord will rejoice in his works:
32 Iye amene amayangʼana dziko lapansi ndipo limanjenjemera, amene amakhudza mapiri ndipo amatuluka utsi.
He who looketh down on the earth, and she trembleth; who toucheth the mountains, and they smoke.
33 Ine ndidzayimbira Yehova moyo wanga wonse; ndidzayimbira matamando Mulungu wanga nthawi yonse imene ndili ndi moyo.
I will sing unto the Lord while I live: I will sing praises to my God while I exist.
34 Zolingalira zanga zikhale zomukomera Iye, pamene ndikusangalala mwa Yehova.
May my speech be agreeable to him: I will indeed rejoice in the Lord.
35 Koma anthu ochimwa awonongeke pa dziko lapansi ndipo anthu oyipa asapezekenso. Tamanda Yehova, Iwe moyo wanga. Tamandani Yehova.
May the sinners cease from off the earth, and the wicked be no more. Bless, O my soul, the Lord. Hallelujah.