< Masalimo 104 >

1 Tamanda Yehova, iwe moyo wanga. Inu Yehova Mulungu wanga, ndinu wamkulu kwambiri; mwavala ulemerero ndi ufumu.
Bless Jehovah, O my soul! Jehovah my God, thou art very great; thou art clothed with majesty and splendour;
2 Iye wadzifunditsa kuwala ngati chovala; watambasula miyamba ngati tenti
Covering thyself with light as with a garment, stretching out the heavens like a tent-curtain; —
3 ndipo wayika pa madzi mitanda ya chipinda chake. Iye amasandutsa mitambo kukhala galeta lake, ndi kuwuluka pa mapiko a mphepo.
Who layeth the beams of his upper chambers in the waters, who maketh clouds his chariot, who walketh upon the wings of the wind;
4 Amapanga mphepo kukhala amithenga ake, malawi amoto kukhala atumiki ake.
Who maketh his angels spirits; his ministers a flame of fire.
5 Anakhazikitsa dziko lapansi pa maziko ake; silingasunthike.
He laid the earth upon its foundations: it shall not be removed for ever.
6 Munaliphimba ndi nyanja yozama ngati chovala; madzi anayimirira pamwamba pa mapiri.
Thou hadst covered it with the deep, as with a vesture; the waters stood above the mountains:
7 Koma pakudzudzula kwanu madzi anathawa, pa mkokomo wa bingu lanu iwo anamwazika;
At thy rebuke they fled, at the voice of thy thunder they hasted away; —
8 Inu munamiza mapiri, iwo anatsikira ku zigwa kumalo kumene munawakonzera.
The mountains rose, the valleys sank, unto the place which thou hadst founded for them; —
9 Inu munayika malire ndipo sangathe kudutsa, iwo sadzamizanso dziko lapansi.
Thou hast set a bound which they may not pass over, that they turn not again to cover the earth.
10 Iye achititsa akasupe kutulutsa madzi kupita ku zigwa; madziwo amayenda pakati pa mapiri.
He sendeth the springs into the valleys: they run among the mountains;
11 Iwo amapereka madzi kwa zirombo zonse zakuthengo; abulu akuthengo amapha ludzu lawo.
They give drink to every beast of the field; the wild asses quench their thirst.
12 Mbalame zamlengalenga zimayika zisa mʼmbali mwa madzi; zimayimba pakati pa thambo.
The birds of heaven dwell by them; they give forth their voice from among the branches.
13 Iye amathirira mapiri kuchokera ku zipinda zake zapamwamba; dziko lapansi limakhutitsidwa ndi chipatso cha ntchito yake.
He watereth the mountains from his upper-chambers: the earth is satisfied with the fruit of thy works.
14 Amameretsa udzu kuti ngʼombe zidye, ndi zomera, kuti munthu azilima kubweretsa chakudya kuchokera mʼdziko lapansi:
He maketh the grass to grow for the cattle, and herb for the service of man; bringing forth bread out of the earth,
15 vinyo amene amasangalatsa mtima wa munthu, mafuta amene amachititsa nkhope yake kuwala, ndi buledi amene amapereka mphamvu.
And wine which gladdeneth the heart of man; making [his] face shine with oil; and with bread he strengtheneth man's heart.
16 Mitengo ya Yehova ndi yothiriridwa bwino, mikungudza ya ku Lebanoni imene Iye anadzala.
The trees of Jehovah are satisfied, the cedars of Lebanon, which he hath planted,
17 Mbalame zimamanga zisa zawo; kakowa ali ndi malo ake mʼmikungudzamo.
Where the birds make their nests; [as for] the stork, the fir trees are her house.
18 Mapiri ataliatali ndi a mbalale; mʼmingʼalu ya miyala ndi mobisalamo mbira.
The high mountains are for the wild goats; the cliffs, a refuge for the rock-badgers.
19 Mwezi umasiyanitsa nyengo ndipo dzuwa limadziwa nthawi yake yolowera.
He made the moon for seasons: the sun knoweth its going down.
20 Inu mumabweretsa mdima nukhala usiku, ndipo zirombo zonse za ku nkhalango zimatuluka.
Thou makest darkness, and it is night, wherein all the beasts of the forest creep forth:
21 Mikango imabangula kufuna nyama, ndi kufunafuna chakudya chawo kuchokera kwa Mulungu.
The young lions roar after the prey, and to seek their food from God.
22 Dzuwa limatuluka ndipo iyo imapita kukabisala; imabwerera kukagona pansi mʼmapanga awo.
The sun ariseth, they retreat, and lay them down in their dens.
23 Pamenepo munthu amapita ku ntchito yake, kukagwira ntchito yake mpaka madzulo.
Man goeth forth unto his work, and to his labour until the evening.
24 Ntchito zanu ndi zochulukadi Inu Yehova! Munazipanga zonse mwanzeru, dziko lapansi ladzaza ndi zolengedwa zanu.
How manifold are thy works, O Jehovah! in wisdom hast thou made them all: the earth is full of thy riches.
25 Kuli nyanja yayikulu ndi yotambalala, yodzaza ndi zolengedwa zosawerengeka, zamoyo zanu zazikulu ndi zazingʼono zomwe.
Yonder is the great and wide sea: therein are moving things innumerable, living creatures small and great.
26 Kumeneko sitima zapamadzi zimayenda uku ndi uku, ndiponso Leviyatani amene munamulenga kuti asewere kumeneko.
There go the ships; [there] that leviathan, which thou hast formed to play therein.
27 Zonsezi zimayangʼana kwa Inu kuti muzipatse chakudya chawo pa nthawi yake yoyenera.
These all look unto thee, that thou mayest give their food in its season:
28 Mukazipatsa, zimachisonkhanitsa pamodzi; mukatsekula dzanja lanu, izo zimakhutitsidwa ndi zinthu zabwino.
That thou givest unto them, they gather; thou openest thy hand, they are filled with good.
29 Mukabisa nkhope yanu, izo zimachita mantha aakulu; mukachotsa mpweya wawo, zimafa ndi kubwerera ku fumbi.
Thou hidest thy face, they are troubled; thou takest away their breath, they expire and return to their dust.
30 Mukatumiza mzimu wanu, izo zimalengedwa ndipo mumakozanso maonekedwe a dziko lapansi.
Thou sendest forth thy spirit, they are created, and thou renewest the face of the earth.
31 Ulemerero wa Yehova ukhalebe mpaka muyaya; Yehova akondwere ndi ntchito ya manja ake;
The glory of Jehovah will endure for ever; Jehovah will rejoice in his works.
32 Iye amene amayangʼana dziko lapansi ndipo limanjenjemera, amene amakhudza mapiri ndipo amatuluka utsi.
He looketh on the earth, and it trembleth; he toucheth the mountains, and they smoke.
33 Ine ndidzayimbira Yehova moyo wanga wonse; ndidzayimbira matamando Mulungu wanga nthawi yonse imene ndili ndi moyo.
I will sing unto Jehovah as long as I live; I will sing psalms to my God while I have my being.
34 Zolingalira zanga zikhale zomukomera Iye, pamene ndikusangalala mwa Yehova.
My meditation shall be pleasant unto him; I will rejoice in Jehovah.
35 Koma anthu ochimwa awonongeke pa dziko lapansi ndipo anthu oyipa asapezekenso. Tamanda Yehova, Iwe moyo wanga. Tamandani Yehova.
Sinners shall be consumed out of the earth, and the wicked shall be no more. Bless Jehovah, O my soul. Hallelujah!

< Masalimo 104 >