< Masalimo 103 >

1 Salimo la Davide. Tamanda Yehova, iwe moyo wanga; ndi zonse zamʼkati mwanga zitamande dzina lake loyera.
En Psalm Davids. Lofva Herran, min själ, och allt det uti mig är, hans helga Namn.
2 Tamanda Yehova, iwe moyo wanga, ndipo usayiwale zabwino zake zonse.
Lofva Herran, min själ, och förgät icke, hvad godt han dig gjort hafver;
3 Amene amakhululuka machimo ako onse ndi kuchiritsa nthenda zako zonse,
Den dig alla dina synder förlåter, och helar alla dina brister;
4 amene awombola moyo wako ku dzenje ndi kukuveka chikondi ndi chifundo chake ngati chipewa chaufumu,
Den ditt lif förlöser ifrå förderf, och kröner dig med nåd och barmhertighet;
5 amene akwaniritsa zokhumba zako ndi zinthu zabwino, kotero kuti umakhala wamphamvu zatsopano ngati mphungu.
Den dig uppfyller med tröst, att du dägelig varder, och gör dig ung och frisk såsom en örn.
6 Yehova amachita chilungamo ndipo amaweruza molungama onse opsinjika.
Herren skaffar rättfärdighet och dom, allom dem som orätt lida.
7 Iye anadziwitsa Mose njira zake, ntchito zake kwa Aisraeli.
Han hafver låtit Mose veta sina vägar; Israels barn sin verk.
8 Yehova ndi wachifundo ndi wokoma mtima, wosakwiya msanga ndi wachikondi chochuluka.
Barmhertig och nådelig är Herren, tålig och af stora mildhet.
9 Iye sadzatsutsa nthawi zonse, kapena kusunga mkwiyo wake kwamuyaya;
Han träter icke till evig tid, och vredgas icke evinnerliga.
10 satichitira molingana ndi machimo athu, kapena kutibwezera molingana ndi mphulupulu zathu.
Han handlar icke med oss efter våra synder, och vedergäller oss icke efter våra missgerningar.
11 Pakuti monga kumwamba kuli kutali ndi dziko lapansi, koteronso chikondi chake nʼchachikulu kwa iwo amene amamuopa;
Ty så hög som himmelen öfver jordena är, låter han sina nåd väldig vara öfver dem som frukta honom.
12 monga kummawa kutalikirana ndi kumadzulo, koteronso Iye watichotsera mphulupulu zathu kuti zikhale kutali nafe.
Så långt som öster är ifrå vester, låter han vår öfverträdelse vara ifrån oss.
13 Monga bambo amachitira chifundo ana ake, choncho Yehova ali ndi chifundo ndi iwo amene amamuopa;
Såsom en fader förbarmar sig öfver barnen, så förbarmar sig Herren öfver dem som frukta honom.
14 pakuti Iye amadziwa momwe tinawumbidwira, amakumbukira kuti ndife fumbi.
Ty han vet hvad vi för ett verk äre; han tänker derpå, att vi stoft äre.
15 Kunena za munthu, masiku ake ali ngati udzu, amaphuka ngati duwa la mʼmunda;
En menniska är i sitt lefvande såsom gräs; hon blomstras såsom ett blomster på markene.
16 koma mphepo imawombapo ndipo silionekanso ndipo malo ake sakumbukirikanso.
När vädret deröfver går, så är det intet mer der, och dess rum känner det intet mer.
17 Koma kuchokera muyaya mpaka muyaya chikondi cha Yehova chili ndi iwo amene amamuopa, ndi chilungamo chake chili ndi ana a ana awo;
Men Herrans nåd varar ifrån evighet till evighet, öfver dem som frukta honom; och hans rättfärdighet intill barnabarn,
18 iwo amene amasunga pangano lake ndi kukumbukira kumvera malangizo ake.
När dem som hans förbund hålla, och tänka uppå hans bud, att de derefter göra.
19 Yehova wakhazikitsa mpando wake waufumu mmwamba ndipo ufumu wake umalamulira onse.
Herren hafver beredt sin stol i himmelen, och hans rike skall råda öfver allt.
20 Tamandani Yehova, inu angelo ake, amphamvu inu amene mumachita zimene amalamula, amene mumamvera mawu ake.
Lofver Herran, I hans Änglar, I starke hjeltar, som hans befallning uträtten, att man hans ords röst höra skall.
21 Tamandani Yehova, zolengedwa zonse zakumwamba, inu atumiki ake amene mumachita chifuniro chake.
Lofver Herran, alle hans härar; I hans tjenare, som hans vilja gören.
22 Tamandani Yehova, ntchito yake yonse kulikonse mu ulamuliro wake. Tamanda Yehova, iwe moyo wanga.
Lofver Herran, all hans verk uti all hans herradömes rum; min själ lofve Herran.

< Masalimo 103 >