< Masalimo 103 >
1 Salimo la Davide. Tamanda Yehova, iwe moyo wanga; ndi zonse zamʼkati mwanga zitamande dzina lake loyera.
[Psalm lal David] Kaksakin LEUM GOD, O ngunik! Ma nukewa in nga, in kaksakin Ine mutal lal!
2 Tamanda Yehova, iwe moyo wanga, ndipo usayiwale zabwino zake zonse.
Kaksakin LEUM GOD, O ngunik, Ac tia mulkunla lupan kulang lal.
3 Amene amakhululuka machimo ako onse ndi kuchiritsa nthenda zako zonse,
El nunak munas ke ma koluk luk nukewa Ac akkeyala mas luk nukewa.
4 amene awombola moyo wako ku dzenje ndi kukuveka chikondi ndi chifundo chake ngati chipewa chaufumu,
El moliyula liki misa Ac akinsewowoyeyu ke lungse ac pakoten.
5 amene akwaniritsa zokhumba zako ndi zinthu zabwino, kotero kuti umakhala wamphamvu zatsopano ngati mphungu.
El akkihpye moul luk ke ma wo Tuh nga in fusr na ac ku oana sie won eagle.
6 Yehova amachita chilungamo ndipo amaweruza molungama onse opsinjika.
LEUM GOD El oru nununku lal in wi layen lun mwet akkeokyeyuk, El oru tuh nununku suwohs in orek nu selos.
7 Iye anadziwitsa Mose njira zake, ntchito zake kwa Aisraeli.
El akkalemye inkanek lal nu sel Moses Ac lela tuh mwet Israel in liye orekma kulana lal.
8 Yehova ndi wachifundo ndi wokoma mtima, wosakwiya msanga ndi wachikondi chochuluka.
LEUM GOD El kulang ac pakoten, El tia sa in mulat, ac yoklana lungkulang lal.
9 Iye sadzatsutsa nthawi zonse, kapena kusunga mkwiyo wake kwamuyaya;
El ac tia kaiyuk pacl nukewa, El tia kolla mulat lal nwe tok.
10 satichitira molingana ndi machimo athu, kapena kutibwezera molingana ndi mphulupulu zathu.
El tia kai kut fal nu ke ma koluk lasr, Ku ase nu sesr ma fal nu ke orekma koluk lasr.
11 Pakuti monga kumwamba kuli kutali ndi dziko lapansi, koteronso chikondi chake nʼchachikulu kwa iwo amene amamuopa;
Tuh lungse lun God nu selos su sunakunul Oana fulatan kusrao nu faclu.
12 monga kummawa kutalikirana ndi kumadzulo, koteronso Iye watichotsera mphulupulu zathu kuti zikhale kutali nafe.
El usla ma koluk lasr loes liki kut, Oana lusen kutulap lac nwe roto.
13 Monga bambo amachitira chifundo ana ake, choncho Yehova ali ndi chifundo ndi iwo amene amamuopa;
LEUM GOD El pakomutalos su akfulatyal, Oana ke sie papa el pakomuta tulik natul.
14 pakuti Iye amadziwa momwe tinawumbidwira, amakumbukira kuti ndife fumbi.
God El etu lah mea kut orekla kac, El esam lah kut orekla ke kutkut.
15 Kunena za munthu, masiku ake ali ngati udzu, amaphuka ngati duwa la mʼmunda;
A funu mwet uh, moul lasr uh oana mah. Kut kapak ac farngelik oana ros inimae,
16 koma mphepo imawombapo ndipo silionekanso ndipo malo ake sakumbukirikanso.
Na eng tuhyak nu faclos ac elos wanginla Ac tia sifil liyeyuk.
17 Koma kuchokera muyaya mpaka muyaya chikondi cha Yehova chili ndi iwo amene amamuopa, ndi chilungamo chake chili ndi ana a ana awo;
A nu selos su sangeng sin LEUM GOD, lungse lal oan nu tok ma pahtpat, Ac suwoswos lal nu sin fwil nu ke fwil —
18 iwo amene amasunga pangano lake ndi kukumbukira kumvera malangizo ake.
Nu selos su karinganang wuleang lal Ac oaru in akos ma sap lal.
19 Yehova wakhazikitsa mpando wake waufumu mmwamba ndipo ufumu wake umalamulira onse.
LEUM GOD El oakiya tron lal inkusrao; El tokosra fin ma nukewa.
20 Tamandani Yehova, inu angelo ake, amphamvu inu amene mumachita zimene amalamula, amene mumamvera mawu ake.
Kaksakin LEUM GOD, kowos lipufan kulana lal, Su akos sap ku lal, Ac porongo kas lal.
21 Tamandani Yehova, zolengedwa zonse zakumwamba, inu atumiki ake amene mumachita chifuniro chake.
Kaksakin LEUM GOD, kowos un mwet ku lal inkusrao, Kowos mwet kulansap lal, su oru lungse lal.
22 Tamandani Yehova, ntchito yake yonse kulikonse mu ulamuliro wake. Tamanda Yehova, iwe moyo wanga.
Kaksakin LEUM GOD, kowos su ma orekla lal In acn nukewa el leumi. Kaksakin LEUM GOD, O ngunik!