< Masalimo 103 >

1 Salimo la Davide. Tamanda Yehova, iwe moyo wanga; ndi zonse zamʼkati mwanga zitamande dzina lake loyera.
ダビデの歌 わがたましいよ、主をほめよ。わがうちなるすべてのものよ、その聖なるみ名をほめよ。
2 Tamanda Yehova, iwe moyo wanga, ndipo usayiwale zabwino zake zonse.
わがたましいよ、主をほめよ。そのすべてのめぐみを心にとめよ。
3 Amene amakhululuka machimo ako onse ndi kuchiritsa nthenda zako zonse,
主はあなたのすべての不義をゆるし、あなたのすべての病をいやし、
4 amene awombola moyo wako ku dzenje ndi kukuveka chikondi ndi chifundo chake ngati chipewa chaufumu,
あなたのいのちを墓からあがないいだし、いつくしみと、あわれみとをあなたにこうむらせ、
5 amene akwaniritsa zokhumba zako ndi zinthu zabwino, kotero kuti umakhala wamphamvu zatsopano ngati mphungu.
あなたの生きながらえるかぎり、良き物をもってあなたを飽き足らせられる。こうしてあなたは若返って、わしのように新たになる。
6 Yehova amachita chilungamo ndipo amaweruza molungama onse opsinjika.
主はすべてしえたげられる者のために正義と公正とを行われる。
7 Iye anadziwitsa Mose njira zake, ntchito zake kwa Aisraeli.
主はおのれの道をモーセに知らせ、おのれのしわざをイスラエルの人々に知らせられた。
8 Yehova ndi wachifundo ndi wokoma mtima, wosakwiya msanga ndi wachikondi chochuluka.
主はあわれみに富み、めぐみふかく、怒ること遅く、いつくしみ豊かでいらせられる。
9 Iye sadzatsutsa nthawi zonse, kapena kusunga mkwiyo wake kwamuyaya;
主は常に責めることをせず、また、とこしえに怒りをいだかれない。
10 satichitira molingana ndi machimo athu, kapena kutibwezera molingana ndi mphulupulu zathu.
主はわれらの罪にしたがってわれらをあしらわず、われらの不義にしたがって報いられない。
11 Pakuti monga kumwamba kuli kutali ndi dziko lapansi, koteronso chikondi chake nʼchachikulu kwa iwo amene amamuopa;
天が地よりも高いように、主がおのれを恐れる者に賜わるいつくしみは大きい、
12 monga kummawa kutalikirana ndi kumadzulo, koteronso Iye watichotsera mphulupulu zathu kuti zikhale kutali nafe.
東が西から遠いように、主はわれらのとがをわれらから遠ざけられる。
13 Monga bambo amachitira chifundo ana ake, choncho Yehova ali ndi chifundo ndi iwo amene amamuopa;
父がその子供をあわれむように、主はおのれを恐れる者をあわれまれる。
14 pakuti Iye amadziwa momwe tinawumbidwira, amakumbukira kuti ndife fumbi.
主はわれらの造られたさまを知り、われらのちりであることを覚えていられるからである。
15 Kunena za munthu, masiku ake ali ngati udzu, amaphuka ngati duwa la mʼmunda;
人は、そのよわいは草のごとく、その栄えは野の花にひとしい。
16 koma mphepo imawombapo ndipo silionekanso ndipo malo ake sakumbukirikanso.
風がその上を過ぎると、うせて跡なく、その場所にきいても、もはやそれを知らない。
17 Koma kuchokera muyaya mpaka muyaya chikondi cha Yehova chili ndi iwo amene amamuopa, ndi chilungamo chake chili ndi ana a ana awo;
しかし主のいつくしみは、とこしえからとこしえまで、主を恐れる者の上にあり、その義は子らの子に及び、
18 iwo amene amasunga pangano lake ndi kukumbukira kumvera malangizo ake.
その契約を守り、その命令を心にとめて行う者にまで及ぶ。
19 Yehova wakhazikitsa mpando wake waufumu mmwamba ndipo ufumu wake umalamulira onse.
主はその玉座を天に堅くすえられ、そのまつりごとはすべての物を統べ治める。
20 Tamandani Yehova, inu angelo ake, amphamvu inu amene mumachita zimene amalamula, amene mumamvera mawu ake.
主の使たちよ、そのみ言葉の声を聞いて、これを行う勇士たちよ、主をほめまつれ。
21 Tamandani Yehova, zolengedwa zonse zakumwamba, inu atumiki ake amene mumachita chifuniro chake.
そのすべての万軍よ、そのみこころを行うしもべたちよ、主をほめよ。
22 Tamandani Yehova, ntchito yake yonse kulikonse mu ulamuliro wake. Tamanda Yehova, iwe moyo wanga.
主が造られたすべての物よ、そのまつりごとの下にあるすべての所で、主をほめよ。わがたましいよ、主をほめよ。

< Masalimo 103 >