< Masalimo 103 >

1 Salimo la Davide. Tamanda Yehova, iwe moyo wanga; ndi zonse zamʼkati mwanga zitamande dzina lake loyera.
[Salmo] di Davide BENEDICI, anima mia, il Signore; E tutte le mie interiora [benedite] il Nome suo santo.
2 Tamanda Yehova, iwe moyo wanga, ndipo usayiwale zabwino zake zonse.
Benedici, anima mia, il Signore, E non dimenticare alcuno dei suoi beneficii.
3 Amene amakhululuka machimo ako onse ndi kuchiritsa nthenda zako zonse,
[Egli è quel] che [ti] perdona tutte le tue iniquità; Che sana tutte le tue infermità;
4 amene awombola moyo wako ku dzenje ndi kukuveka chikondi ndi chifundo chake ngati chipewa chaufumu,
Che riscuote dalla fossa la tua vita; Che ti corona di benignità e di compassioni;
5 amene akwaniritsa zokhumba zako ndi zinthu zabwino, kotero kuti umakhala wamphamvu zatsopano ngati mphungu.
Che sazia di beni la tua bocca; Che ti fa ringiovanire come l'aquila.
6 Yehova amachita chilungamo ndipo amaweruza molungama onse opsinjika.
Il Signore fa giustizia E ragione a tutti quelli che sono oppressati.
7 Iye anadziwitsa Mose njira zake, ntchito zake kwa Aisraeli.
Egli ha fatte assapere a Mosè le sue vie, [Ed] a' figliuoli d'Israele le sue opere.
8 Yehova ndi wachifundo ndi wokoma mtima, wosakwiya msanga ndi wachikondi chochuluka.
Il Signore [è] pietoso e clemente; Lento all'ira, e di gran benignità.
9 Iye sadzatsutsa nthawi zonse, kapena kusunga mkwiyo wake kwamuyaya;
Egli non contende in eterno; E non serba [l'ira] in perpetuo.
10 satichitira molingana ndi machimo athu, kapena kutibwezera molingana ndi mphulupulu zathu.
Egli non ci ha fatto secondo i nostri peccati; E non ci ha reso la retribuzione secondo le nostre iniquità.
11 Pakuti monga kumwamba kuli kutali ndi dziko lapansi, koteronso chikondi chake nʼchachikulu kwa iwo amene amamuopa;
Perciocchè, quanto sono alti i cieli sopra la terra, [Tanto] è grande la sua benignità inverso quelli che lo temono.
12 monga kummawa kutalikirana ndi kumadzulo, koteronso Iye watichotsera mphulupulu zathu kuti zikhale kutali nafe.
Quant'è lontano il Levante dal Ponente, [Tanto] ha egli allontanati da noi i nostri misfatti.
13 Monga bambo amachitira chifundo ana ake, choncho Yehova ali ndi chifundo ndi iwo amene amamuopa;
Come un padre è pietoso inverso i figliuoli, [Così] è il Signore pietoso inverso quelli che lo temono.
14 pakuti Iye amadziwa momwe tinawumbidwira, amakumbukira kuti ndife fumbi.
Perciocchè egli conosce la nostra natura; Egli si ricorda che noi [siamo] polvere.
15 Kunena za munthu, masiku ake ali ngati udzu, amaphuka ngati duwa la mʼmunda;
I giorni dell'uomo [son] come l'erba; Egli fiorisce come il fiore del campo.
16 koma mphepo imawombapo ndipo silionekanso ndipo malo ake sakumbukirikanso.
[Il quale], se un vento gli passa sopra, non [è] più; E il suo luogo non lo riconosce più.
17 Koma kuchokera muyaya mpaka muyaya chikondi cha Yehova chili ndi iwo amene amamuopa, ndi chilungamo chake chili ndi ana a ana awo;
Ma la benignità del Signore [è] di secolo in secolo Sopra quelli che lo temono; E la sua giustizia sopra i figliuoli de' figliuoli,
18 iwo amene amasunga pangano lake ndi kukumbukira kumvera malangizo ake.
Di quelli che osservano il suo patto, E che si ricordano de' suoi comandamenti, per metterli in opera.
19 Yehova wakhazikitsa mpando wake waufumu mmwamba ndipo ufumu wake umalamulira onse.
Il Signore ha stabilito il suo trono ne' cieli; E il suo regno signoreggia per tutto.
20 Tamandani Yehova, inu angelo ake, amphamvu inu amene mumachita zimene amalamula, amene mumamvera mawu ake.
Benedite il Signore, [voi] suoi Angeli, Possenti di forza, che fate ciò ch'egli dice, Ubbidendo alla voce della sua parola.
21 Tamandani Yehova, zolengedwa zonse zakumwamba, inu atumiki ake amene mumachita chifuniro chake.
Benedite il Signore, [voi] tutti gli eserciti suoi; [Voi] suoi ministri, che fate ciò che gli piace.
22 Tamandani Yehova, ntchito yake yonse kulikonse mu ulamuliro wake. Tamanda Yehova, iwe moyo wanga.
Benedite il Signore, [voi] tutte l'opere sue, In tutti i luoghi della sua signoria. Anima mia, benedici il Signore.

< Masalimo 103 >