< Masalimo 103 >
1 Salimo la Davide. Tamanda Yehova, iwe moyo wanga; ndi zonse zamʼkati mwanga zitamande dzina lake loyera.
Von David. Preise, meine Seele, Jahwe, und alles, was in mir ist, seinen heiligen Namen!
2 Tamanda Yehova, iwe moyo wanga, ndipo usayiwale zabwino zake zonse.
Preise, meine Seele, Jahwe, und vergiß nicht, was er dir alles gethan hat!
3 Amene amakhululuka machimo ako onse ndi kuchiritsa nthenda zako zonse,
Der dir alle deine Schuld vergab, alle deine Gebrechen heilte,
4 amene awombola moyo wako ku dzenje ndi kukuveka chikondi ndi chifundo chake ngati chipewa chaufumu,
der dein Leben aus der Grube erlöste, mit Gnade und Barmherzigkeit dich krönte,
5 amene akwaniritsa zokhumba zako ndi zinthu zabwino, kotero kuti umakhala wamphamvu zatsopano ngati mphungu.
der dein Verlangen mit Gutem sättigte; dem Adler gleich erneuert sich deine Jugend!
6 Yehova amachita chilungamo ndipo amaweruza molungama onse opsinjika.
Gerechtigkeit schafft Jahwe und Recht für alle Unterdrückten.
7 Iye anadziwitsa Mose njira zake, ntchito zake kwa Aisraeli.
Er ließ seine Wege Mose kund werden, den Söhnen Israels seine großen Thaten.
8 Yehova ndi wachifundo ndi wokoma mtima, wosakwiya msanga ndi wachikondi chochuluka.
Barmherzig und gnädig ist Jahwe, langsam zum Zorn und reich an Huld.
9 Iye sadzatsutsa nthawi zonse, kapena kusunga mkwiyo wake kwamuyaya;
Nicht für immer hadert er, noch trägt er ewig nach.
10 satichitira molingana ndi machimo athu, kapena kutibwezera molingana ndi mphulupulu zathu.
Er verfuhr mit uns nicht nach unseren Sünden und vergalt uns nicht nach unseren Verschuldungen,
11 Pakuti monga kumwamba kuli kutali ndi dziko lapansi, koteronso chikondi chake nʼchachikulu kwa iwo amene amamuopa;
sondern so hoch der Himmel über der Erde ist, ist seine Gnade mächtig über denen, die ihn fürchten.
12 monga kummawa kutalikirana ndi kumadzulo, koteronso Iye watichotsera mphulupulu zathu kuti zikhale kutali nafe.
So fern der Sonnenaufgang vom Untergang, hat er unsere Vergehungen von uns entfernt.
13 Monga bambo amachitira chifundo ana ake, choncho Yehova ali ndi chifundo ndi iwo amene amamuopa;
Wie sich ein Vater über Kinder erbarmt, hat sich Jahwe erbarmt über die, die ihn fürchten.
14 pakuti Iye amadziwa momwe tinawumbidwira, amakumbukira kuti ndife fumbi.
Denn er weiß, woraus wir geformt sind, ist eingedenk, daß wir Staub sind.
15 Kunena za munthu, masiku ake ali ngati udzu, amaphuka ngati duwa la mʼmunda;
Des Menschen Lebenstage sind wie das Gras; wie eine Blume auf dem Felde, also blüht er.
16 koma mphepo imawombapo ndipo silionekanso ndipo malo ake sakumbukirikanso.
Wenn ein Windhauch über ihn dahingefahren, ist er dahin, und seine Stätte kennt ihn nicht mehr.
17 Koma kuchokera muyaya mpaka muyaya chikondi cha Yehova chili ndi iwo amene amamuopa, ndi chilungamo chake chili ndi ana a ana awo;
Die Gnade Jahwes aber währt von Ewigkeit zu Ewigkeit über denen, die ihn fürchten, und seine Gerechtigkeit auf Kindeskinder
18 iwo amene amasunga pangano lake ndi kukumbukira kumvera malangizo ake.
derer, die seinen Bund halten und seiner Gebote eingedenk sind, daß sie danach thun.
19 Yehova wakhazikitsa mpando wake waufumu mmwamba ndipo ufumu wake umalamulira onse.
Jahwe hat seinen Thron im Himmel aufgerichtet, und sein Königtum herrscht über das All.
20 Tamandani Yehova, inu angelo ake, amphamvu inu amene mumachita zimene amalamula, amene mumamvera mawu ake.
Preist Jahwe, ihr, seine Engel, ihr starken Helden, die ihr seinen Befehl ausrichtet, indem sie auf den Schall seines Wortes hören.
21 Tamandani Yehova, zolengedwa zonse zakumwamba, inu atumiki ake amene mumachita chifuniro chake.
Preist Jahwe, ihr, all sein Heer, seine Diener, die ihr seinen Willen vollzieht.
22 Tamandani Yehova, ntchito yake yonse kulikonse mu ulamuliro wake. Tamanda Yehova, iwe moyo wanga.
Preist Jahwe, alle seine Werke an allen Orten seiner Herrschaft. Preise, meine Seele, Jahwe!