< Masalimo 103 >

1 Salimo la Davide. Tamanda Yehova, iwe moyo wanga; ndi zonse zamʼkati mwanga zitamande dzina lake loyera.
Par David. Loue Yahvé, mon âme! Tout ce qui est en moi, loue son saint nom!
2 Tamanda Yehova, iwe moyo wanga, ndipo usayiwale zabwino zake zonse.
Louez Yahvé, mon âme! et n'oubliez pas tous ses avantages,
3 Amene amakhululuka machimo ako onse ndi kuchiritsa nthenda zako zonse,
qui pardonne tous vos péchés, qui guérit toutes vos maladies,
4 amene awombola moyo wako ku dzenje ndi kukuveka chikondi ndi chifundo chake ngati chipewa chaufumu,
qui rachète votre vie de la destruction, qui vous couronne de bonté et de tendresse,
5 amene akwaniritsa zokhumba zako ndi zinthu zabwino, kotero kuti umakhala wamphamvu zatsopano ngati mphungu.
qui satisfait ton désir par de bonnes choses, afin que ta jeunesse se renouvelle comme celle de l'aigle.
6 Yehova amachita chilungamo ndipo amaweruza molungama onse opsinjika.
Yahvé exécute des actes justes, et la justice pour tous ceux qui sont opprimés.
7 Iye anadziwitsa Mose njira zake, ntchito zake kwa Aisraeli.
Il a fait connaître ses voies à Moïse, ses actes aux enfants d'Israël.
8 Yehova ndi wachifundo ndi wokoma mtima, wosakwiya msanga ndi wachikondi chochuluka.
Yahvé est miséricordieux et compatissant, lent à la colère, et abondant en bonté.
9 Iye sadzatsutsa nthawi zonse, kapena kusunga mkwiyo wake kwamuyaya;
Il n'accusera pas toujours; il ne restera pas non plus en colère pour toujours.
10 satichitira molingana ndi machimo athu, kapena kutibwezera molingana ndi mphulupulu zathu.
Il ne nous a pas traités selon nos péchés, et ne nous a pas remboursé pour nos iniquités.
11 Pakuti monga kumwamba kuli kutali ndi dziko lapansi, koteronso chikondi chake nʼchachikulu kwa iwo amene amamuopa;
Car comme les cieux sont élevés au-dessus de la terre, tant est grande sa bonté envers ceux qui le craignent.
12 monga kummawa kutalikirana ndi kumadzulo, koteronso Iye watichotsera mphulupulu zathu kuti zikhale kutali nafe.
Aussi loin que l'est est de l'ouest, jusqu'à ce qu'il ait éloigné de nous nos transgressions.
13 Monga bambo amachitira chifundo ana ake, choncho Yehova ali ndi chifundo ndi iwo amene amamuopa;
Comme un père a de la compassion pour ses enfants, Yahvé a donc de la compassion pour ceux qui le craignent.
14 pakuti Iye amadziwa momwe tinawumbidwira, amakumbukira kuti ndife fumbi.
Car il sait comment nous sommes faits. Il se souvient que nous sommes de la poussière.
15 Kunena za munthu, masiku ake ali ngati udzu, amaphuka ngati duwa la mʼmunda;
Quant à l'homme, ses jours sont comme l'herbe. Comme une fleur des champs, il s'épanouit.
16 koma mphepo imawombapo ndipo silionekanso ndipo malo ake sakumbukirikanso.
Car le vent passe sur elle, et elle disparaît. Sa place ne s'en souvient plus.
17 Koma kuchokera muyaya mpaka muyaya chikondi cha Yehova chili ndi iwo amene amamuopa, ndi chilungamo chake chili ndi ana a ana awo;
Mais la bonté de Yahvé est d'éternité en éternité avec ceux qui le craignent, sa justice aux enfants des enfants,
18 iwo amene amasunga pangano lake ndi kukumbukira kumvera malangizo ake.
à ceux qui gardent son alliance, à ceux qui se souviennent d'obéir à ses préceptes.
19 Yehova wakhazikitsa mpando wake waufumu mmwamba ndipo ufumu wake umalamulira onse.
Yahvé a établi son trône dans les cieux. Son royaume règne sur tout.
20 Tamandani Yehova, inu angelo ake, amphamvu inu amene mumachita zimene amalamula, amene mumamvera mawu ake.
Louez Yahvé, vous, ses anges, qui sont puissants en force, qui accomplissent sa parole, en obéissant à la voix de sa parole.
21 Tamandani Yehova, zolengedwa zonse zakumwamba, inu atumiki ake amene mumachita chifuniro chake.
Louez Yahvé, vous toutes ses armées, vous êtes ses serviteurs, qui faites sa volonté.
22 Tamandani Yehova, ntchito yake yonse kulikonse mu ulamuliro wake. Tamanda Yehova, iwe moyo wanga.
Louez Yahvé, vous toutes ses œuvres, dans tous les lieux de sa domination. Loue Yahvé, mon âme!

< Masalimo 103 >