< Masalimo 103 >

1 Salimo la Davide. Tamanda Yehova, iwe moyo wanga; ndi zonse zamʼkati mwanga zitamande dzina lake loyera.
By David. Praise the LORD, my soul! All that is within me, praise his holy name!
2 Tamanda Yehova, iwe moyo wanga, ndipo usayiwale zabwino zake zonse.
Praise the LORD, my soul, and don’t forget all his benefits,
3 Amene amakhululuka machimo ako onse ndi kuchiritsa nthenda zako zonse,
who forgives all your sins, who heals all your diseases,
4 amene awombola moyo wako ku dzenje ndi kukuveka chikondi ndi chifundo chake ngati chipewa chaufumu,
who redeems your life from destruction, who crowns you with loving kindness and tender mercies,
5 amene akwaniritsa zokhumba zako ndi zinthu zabwino, kotero kuti umakhala wamphamvu zatsopano ngati mphungu.
who satisfies your desire with good things, so that your youth is renewed like the eagle’s.
6 Yehova amachita chilungamo ndipo amaweruza molungama onse opsinjika.
The LORD executes righteous acts, and justice for all who are oppressed.
7 Iye anadziwitsa Mose njira zake, ntchito zake kwa Aisraeli.
He made known his ways to Moses, his deeds to the children of Israel.
8 Yehova ndi wachifundo ndi wokoma mtima, wosakwiya msanga ndi wachikondi chochuluka.
The LORD is merciful and gracious, slow to anger, and abundant in loving kindness.
9 Iye sadzatsutsa nthawi zonse, kapena kusunga mkwiyo wake kwamuyaya;
He will not always accuse; neither will he stay angry forever.
10 satichitira molingana ndi machimo athu, kapena kutibwezera molingana ndi mphulupulu zathu.
He has not dealt with us according to our sins, nor repaid us for our iniquities.
11 Pakuti monga kumwamba kuli kutali ndi dziko lapansi, koteronso chikondi chake nʼchachikulu kwa iwo amene amamuopa;
For as the heavens are high above the earth, so great is his loving kindness towards those who fear him.
12 monga kummawa kutalikirana ndi kumadzulo, koteronso Iye watichotsera mphulupulu zathu kuti zikhale kutali nafe.
As far as the east is from the west, so far has he removed our transgressions from us.
13 Monga bambo amachitira chifundo ana ake, choncho Yehova ali ndi chifundo ndi iwo amene amamuopa;
Like a father has compassion on his children, so the LORD has compassion on those who fear him.
14 pakuti Iye amadziwa momwe tinawumbidwira, amakumbukira kuti ndife fumbi.
For he knows how we are made. He remembers that we are dust.
15 Kunena za munthu, masiku ake ali ngati udzu, amaphuka ngati duwa la mʼmunda;
As for man, his days are like grass. As a flower of the field, so he flourishes.
16 koma mphepo imawombapo ndipo silionekanso ndipo malo ake sakumbukirikanso.
For the wind passes over it, and it is gone. Its place remembers it no more.
17 Koma kuchokera muyaya mpaka muyaya chikondi cha Yehova chili ndi iwo amene amamuopa, ndi chilungamo chake chili ndi ana a ana awo;
But the LORD’s loving kindness is from everlasting to everlasting with those who fear him, his righteousness to children’s children,
18 iwo amene amasunga pangano lake ndi kukumbukira kumvera malangizo ake.
to those who keep his covenant, to those who remember to obey his precepts.
19 Yehova wakhazikitsa mpando wake waufumu mmwamba ndipo ufumu wake umalamulira onse.
The LORD has established his throne in the heavens. His kingdom rules over all.
20 Tamandani Yehova, inu angelo ake, amphamvu inu amene mumachita zimene amalamula, amene mumamvera mawu ake.
Praise the LORD, you angels of his, who are mighty in strength, who fulfil his word, obeying the voice of his word.
21 Tamandani Yehova, zolengedwa zonse zakumwamba, inu atumiki ake amene mumachita chifuniro chake.
Praise the LORD, all you armies of his, you servants of his, who do his pleasure.
22 Tamandani Yehova, ntchito yake yonse kulikonse mu ulamuliro wake. Tamanda Yehova, iwe moyo wanga.
Praise the LORD, all you works of his, in all places of his dominion. Praise the LORD, my soul!

< Masalimo 103 >