< Masalimo 103 >
1 Salimo la Davide. Tamanda Yehova, iwe moyo wanga; ndi zonse zamʼkati mwanga zitamande dzina lake loyera.
Of David. O my soul, bless the Lord; and all that is in me, his holy name.
2 Tamanda Yehova, iwe moyo wanga, ndipo usayiwale zabwino zake zonse.
O my soul, bless the Lord; and forget not one of his benefits.
3 Amene amakhululuka machimo ako onse ndi kuchiritsa nthenda zako zonse,
He pardons all your sins, he heals all your diseases.
4 amene awombola moyo wako ku dzenje ndi kukuveka chikondi ndi chifundo chake ngati chipewa chaufumu,
He ransoms your life from the pit, he crowns you with kindness and pity.
5 amene akwaniritsa zokhumba zako ndi zinthu zabwino, kotero kuti umakhala wamphamvu zatsopano ngati mphungu.
He gives you your heart’s desire, renewing your youth like the eagle’s.
6 Yehova amachita chilungamo ndipo amaweruza molungama onse opsinjika.
The Lord executes justice – and right for all who are wronged.
7 Iye anadziwitsa Mose njira zake, ntchito zake kwa Aisraeli.
He revealed his ways to Moses, his acts to the children of Israel.
8 Yehova ndi wachifundo ndi wokoma mtima, wosakwiya msanga ndi wachikondi chochuluka.
Full of pity and grace is the Lord, patient, and rich in kindness:
9 Iye sadzatsutsa nthawi zonse, kapena kusunga mkwiyo wake kwamuyaya;
he will not always chide, nor cherish his anger forever.
10 satichitira molingana ndi machimo athu, kapena kutibwezera molingana ndi mphulupulu zathu.
Not after our sins has he dealt with us, nor requited us after our wickedness.
11 Pakuti monga kumwamba kuli kutali ndi dziko lapansi, koteronso chikondi chake nʼchachikulu kwa iwo amene amamuopa;
For high as the heavens o’er the earth is his love over those who fear him.
12 monga kummawa kutalikirana ndi kumadzulo, koteronso Iye watichotsera mphulupulu zathu kuti zikhale kutali nafe.
Far as is east from the west has he put our transgressions from us.
13 Monga bambo amachitira chifundo ana ake, choncho Yehova ali ndi chifundo ndi iwo amene amamuopa;
As a father pities his children, so the Lord pities those who fear him;
14 pakuti Iye amadziwa momwe tinawumbidwira, amakumbukira kuti ndife fumbi.
for well he knows our frame, he remembers that we are dust.
15 Kunena za munthu, masiku ake ali ngati udzu, amaphuka ngati duwa la mʼmunda;
A person’s days are as grass; blossoms like a flower of the meadow.
16 koma mphepo imawombapo ndipo silionekanso ndipo malo ake sakumbukirikanso.
At the breath of the wind it is gone, and the place thereof knows it no more.
17 Koma kuchokera muyaya mpaka muyaya chikondi cha Yehova chili ndi iwo amene amamuopa, ndi chilungamo chake chili ndi ana a ana awo;
But the love of the Lord is eternal, and his kindness to children’s children,
18 iwo amene amasunga pangano lake ndi kukumbukira kumvera malangizo ake.
to those who keep his covenant and mindfully do his behests.
19 Yehova wakhazikitsa mpando wake waufumu mmwamba ndipo ufumu wake umalamulira onse.
The Lord has set his throne in the heavens; the whole world is under his sway.
20 Tamandani Yehova, inu angelo ake, amphamvu inu amene mumachita zimene amalamula, amene mumamvera mawu ake.
Bless the Lord, you angels of his, mighty heroes performing his word.
21 Tamandani Yehova, zolengedwa zonse zakumwamba, inu atumiki ake amene mumachita chifuniro chake.
Bless the Lord, all you his hosts, you servants who do his will.
22 Tamandani Yehova, ntchito yake yonse kulikonse mu ulamuliro wake. Tamanda Yehova, iwe moyo wanga.
Bless the Lord, all you his works, far as his sway extends. O my soul, bless the Lord.