< Masalimo 103 >

1 Salimo la Davide. Tamanda Yehova, iwe moyo wanga; ndi zonse zamʼkati mwanga zitamande dzina lake loyera.
“A psalm of David.” Bless the LORD, O my soul! And all that is within me, bless his holy name!
2 Tamanda Yehova, iwe moyo wanga, ndipo usayiwale zabwino zake zonse.
Bless the LORD, O my soul! And forget not all his benefits!
3 Amene amakhululuka machimo ako onse ndi kuchiritsa nthenda zako zonse,
Who forgiveth all thine iniquities; Who healeth all thy diseases;
4 amene awombola moyo wako ku dzenje ndi kukuveka chikondi ndi chifundo chake ngati chipewa chaufumu,
Who redeemeth thy life from the grave; Who crowneth thee with loving-kindness and tender mercies;
5 amene akwaniritsa zokhumba zako ndi zinthu zabwino, kotero kuti umakhala wamphamvu zatsopano ngati mphungu.
Who satisfieth thine old age with good, So that thy youth is renewed like the eagle's.
6 Yehova amachita chilungamo ndipo amaweruza molungama onse opsinjika.
The LORD executeth justice And equity for all the oppressed.
7 Iye anadziwitsa Mose njira zake, ntchito zake kwa Aisraeli.
He made known his ways to Moses, His doings to the children of Israel.
8 Yehova ndi wachifundo ndi wokoma mtima, wosakwiya msanga ndi wachikondi chochuluka.
The LORD is merciful and kind, Slow to anger and rich in mercy.
9 Iye sadzatsutsa nthawi zonse, kapena kusunga mkwiyo wake kwamuyaya;
He doth not always chide, Nor doth he keep his anger for ever.
10 satichitira molingana ndi machimo athu, kapena kutibwezera molingana ndi mphulupulu zathu.
He hath not dealt with us according to our sins, Nor requited us according to our iniquities.
11 Pakuti monga kumwamba kuli kutali ndi dziko lapansi, koteronso chikondi chake nʼchachikulu kwa iwo amene amamuopa;
As high as are the heavens above the earth, So great is his mercy to them that fear him.
12 monga kummawa kutalikirana ndi kumadzulo, koteronso Iye watichotsera mphulupulu zathu kuti zikhale kutali nafe.
As far as the east is from the west, So far hath he removed our transgressions from us.
13 Monga bambo amachitira chifundo ana ake, choncho Yehova ali ndi chifundo ndi iwo amene amamuopa;
Even as a father pitieth his children, So the LORD pitieth them that fear him.
14 pakuti Iye amadziwa momwe tinawumbidwira, amakumbukira kuti ndife fumbi.
For he knoweth our frame, He remembereth that we are dust.
15 Kunena za munthu, masiku ake ali ngati udzu, amaphuka ngati duwa la mʼmunda;
As for man, his days are as grass; As a flower of the field, so he flourisheth.
16 koma mphepo imawombapo ndipo silionekanso ndipo malo ake sakumbukirikanso.
The wind passeth over it, and it is gone; And its place shall know it no more.
17 Koma kuchokera muyaya mpaka muyaya chikondi cha Yehova chili ndi iwo amene amamuopa, ndi chilungamo chake chili ndi ana a ana awo;
But the mercy of the LORD is from everlasting to everlasting to them that fear him, And his righteousness to children's children,
18 iwo amene amasunga pangano lake ndi kukumbukira kumvera malangizo ake.
To such as keep his covenant, And remember his commandments to do them.
19 Yehova wakhazikitsa mpando wake waufumu mmwamba ndipo ufumu wake umalamulira onse.
The LORD hath established his throne in the heavens, And his kingdom ruleth over all.
20 Tamandani Yehova, inu angelo ake, amphamvu inu amene mumachita zimene amalamula, amene mumamvera mawu ake.
Bless the LORD, ye his angels, Ye mighty ones who do his commands, Hearkening to the voice of his word!
21 Tamandani Yehova, zolengedwa zonse zakumwamba, inu atumiki ake amene mumachita chifuniro chake.
Bless the LORD, all ye his hosts; Ye, his ministers, who do his pleasure!
22 Tamandani Yehova, ntchito yake yonse kulikonse mu ulamuliro wake. Tamanda Yehova, iwe moyo wanga.
Bless the LORD, all his works, In all places of his dominion! Bless the LORD, O my soul!

< Masalimo 103 >