< Masalimo 103 >
1 Salimo la Davide. Tamanda Yehova, iwe moyo wanga; ndi zonse zamʼkati mwanga zitamande dzina lake loyera.
[A Psalm] of David. Bless the LORD, O my soul: and all that is within me, [bless] his holy name.
2 Tamanda Yehova, iwe moyo wanga, ndipo usayiwale zabwino zake zonse.
Bless the LORD, O my soul, and forget not all his benefits:
3 Amene amakhululuka machimo ako onse ndi kuchiritsa nthenda zako zonse,
Who forgiveth all thine iniquities; who healeth all thy diseases;
4 amene awombola moyo wako ku dzenje ndi kukuveka chikondi ndi chifundo chake ngati chipewa chaufumu,
Who redeemeth thy life from destruction; who crowneth thee with lovingkindness and tender mercies;
5 amene akwaniritsa zokhumba zako ndi zinthu zabwino, kotero kuti umakhala wamphamvu zatsopano ngati mphungu.
Who satisfieth thy mouth with good [things; so that] thy youth is renewed like the eagle’s.
6 Yehova amachita chilungamo ndipo amaweruza molungama onse opsinjika.
The LORD executeth righteousness and judgment for all that are oppressed.
7 Iye anadziwitsa Mose njira zake, ntchito zake kwa Aisraeli.
He made known his ways unto Moses, his acts unto the children of Israel.
8 Yehova ndi wachifundo ndi wokoma mtima, wosakwiya msanga ndi wachikondi chochuluka.
The LORD [is] merciful and gracious, slow to anger, and plenteous in mercy.
9 Iye sadzatsutsa nthawi zonse, kapena kusunga mkwiyo wake kwamuyaya;
He will not always chide: neither will he keep [his anger] for ever.
10 satichitira molingana ndi machimo athu, kapena kutibwezera molingana ndi mphulupulu zathu.
He hath not dealt with us after our sins; nor rewarded us according to our iniquities.
11 Pakuti monga kumwamba kuli kutali ndi dziko lapansi, koteronso chikondi chake nʼchachikulu kwa iwo amene amamuopa;
For as the heaven is high above the earth, [so] great is his mercy toward them that fear him.
12 monga kummawa kutalikirana ndi kumadzulo, koteronso Iye watichotsera mphulupulu zathu kuti zikhale kutali nafe.
As far as the east is from the west, [so] far hath he removed our transgressions from us.
13 Monga bambo amachitira chifundo ana ake, choncho Yehova ali ndi chifundo ndi iwo amene amamuopa;
Like as a father pitieth [his] children, [so] the LORD pitieth them that fear him.
14 pakuti Iye amadziwa momwe tinawumbidwira, amakumbukira kuti ndife fumbi.
For he knoweth our frame; he remembereth that we [are] dust.
15 Kunena za munthu, masiku ake ali ngati udzu, amaphuka ngati duwa la mʼmunda;
[As for] man, his days [are] as grass: as a flower of the field, so he flourisheth.
16 koma mphepo imawombapo ndipo silionekanso ndipo malo ake sakumbukirikanso.
For the wind passeth over it, and it is gone; and the place thereof shall know it no more.
17 Koma kuchokera muyaya mpaka muyaya chikondi cha Yehova chili ndi iwo amene amamuopa, ndi chilungamo chake chili ndi ana a ana awo;
But the mercy of the LORD [is] from everlasting to everlasting upon them that fear him, and his righteousness unto children’s children;
18 iwo amene amasunga pangano lake ndi kukumbukira kumvera malangizo ake.
To such as keep his covenant, and to those that remember his commandments to do them.
19 Yehova wakhazikitsa mpando wake waufumu mmwamba ndipo ufumu wake umalamulira onse.
The LORD hath prepared his throne in the heavens; and his kingdom ruleth over all.
20 Tamandani Yehova, inu angelo ake, amphamvu inu amene mumachita zimene amalamula, amene mumamvera mawu ake.
Bless the LORD, ye his angels, that excel in strength, that do his commandments, hearkening unto the voice of his word.
21 Tamandani Yehova, zolengedwa zonse zakumwamba, inu atumiki ake amene mumachita chifuniro chake.
Bless ye the LORD, all [ye] his hosts; [ye] ministers of his, that do his pleasure.
22 Tamandani Yehova, ntchito yake yonse kulikonse mu ulamuliro wake. Tamanda Yehova, iwe moyo wanga.
Bless the LORD, all his works in all places of his dominion: bless the LORD, O my soul.