< Masalimo 103 >
1 Salimo la Davide. Tamanda Yehova, iwe moyo wanga; ndi zonse zamʼkati mwanga zitamande dzina lake loyera.
For David himself. Bless the Lord, O my soul: and let all that is within me bless his holy name.
2 Tamanda Yehova, iwe moyo wanga, ndipo usayiwale zabwino zake zonse.
Bless the Lord, O my soul, and never forget all he hath done for thee.
3 Amene amakhululuka machimo ako onse ndi kuchiritsa nthenda zako zonse,
Who forgiveth all thy iniquities: who healeth all thy diseases.
4 amene awombola moyo wako ku dzenje ndi kukuveka chikondi ndi chifundo chake ngati chipewa chaufumu,
Who redeemeth thy life from destruction: who crowneth thee with mercy and compassion.
5 amene akwaniritsa zokhumba zako ndi zinthu zabwino, kotero kuti umakhala wamphamvu zatsopano ngati mphungu.
Who satisfieth thy desire with good things: thy youth shall be renewed like the eagle’s.
6 Yehova amachita chilungamo ndipo amaweruza molungama onse opsinjika.
The Lord doth mercies, and judgment for all that suffer wrong.
7 Iye anadziwitsa Mose njira zake, ntchito zake kwa Aisraeli.
He hath made his ways known to Moses: his wills to the children of Israel.
8 Yehova ndi wachifundo ndi wokoma mtima, wosakwiya msanga ndi wachikondi chochuluka.
The ford is compassionate and merciful: longsuffering and plenteous in mercy.
9 Iye sadzatsutsa nthawi zonse, kapena kusunga mkwiyo wake kwamuyaya;
He will not always be angry: nor will he threaten for ever.
10 satichitira molingana ndi machimo athu, kapena kutibwezera molingana ndi mphulupulu zathu.
He hath not dealt with us according to our sins: nor rewarded us according to our iniquities.
11 Pakuti monga kumwamba kuli kutali ndi dziko lapansi, koteronso chikondi chake nʼchachikulu kwa iwo amene amamuopa;
For according to the height of the heaven above the earth: he hath strengthened his mercy towards them that fear him.
12 monga kummawa kutalikirana ndi kumadzulo, koteronso Iye watichotsera mphulupulu zathu kuti zikhale kutali nafe.
As far as the east is from the west, so far hath he removed our iniquities from us.
13 Monga bambo amachitira chifundo ana ake, choncho Yehova ali ndi chifundo ndi iwo amene amamuopa;
As a father hath compassion on his children, so hath the Lord compassion on them that fear him:
14 pakuti Iye amadziwa momwe tinawumbidwira, amakumbukira kuti ndife fumbi.
For he knoweth our frame. He remembereth that we are dust:
15 Kunena za munthu, masiku ake ali ngati udzu, amaphuka ngati duwa la mʼmunda;
Man’s days are as grass, as the flower of the field so shall he flourish.
16 koma mphepo imawombapo ndipo silionekanso ndipo malo ake sakumbukirikanso.
For the spirit shall pass in him, and he shall not be: and he shall know his place no more.
17 Koma kuchokera muyaya mpaka muyaya chikondi cha Yehova chili ndi iwo amene amamuopa, ndi chilungamo chake chili ndi ana a ana awo;
But the mercy of the Lord is from eternity and unto eternity upon them that fear him: And his justice unto children’s children,
18 iwo amene amasunga pangano lake ndi kukumbukira kumvera malangizo ake.
To such as keep his covenant, And are mindful of his commandments to do them.
19 Yehova wakhazikitsa mpando wake waufumu mmwamba ndipo ufumu wake umalamulira onse.
The Lord hath prepared his throne in heaven: and his kingdom shall rule over all.
20 Tamandani Yehova, inu angelo ake, amphamvu inu amene mumachita zimene amalamula, amene mumamvera mawu ake.
Bless the Lord, all ye his angels: you that are mighty in strength, and execute his word, hearkening to the voice of his orders.
21 Tamandani Yehova, zolengedwa zonse zakumwamba, inu atumiki ake amene mumachita chifuniro chake.
Bless the Lord, all ye his hosts: you ministers of his that do his will.
22 Tamandani Yehova, ntchito yake yonse kulikonse mu ulamuliro wake. Tamanda Yehova, iwe moyo wanga.
Bless the Lord, all his works: in every place of his dominion, O my soul, bless thou the Lord.