< Masalimo 103 >

1 Salimo la Davide. Tamanda Yehova, iwe moyo wanga; ndi zonse zamʼkati mwanga zitamande dzina lake loyera.
Van David. Loof Jahweh, mijn ziel, Heel mijn binnenste zijn heilige Naam;
2 Tamanda Yehova, iwe moyo wanga, ndipo usayiwale zabwino zake zonse.
Loof Jahweh, mijn ziel, En vergeet zijn talloze weldaden niet!
3 Amene amakhululuka machimo ako onse ndi kuchiritsa nthenda zako zonse,
Hij is het, die al uw zonden vergeeft, En al uw zwakheid geneest;
4 amene awombola moyo wako ku dzenje ndi kukuveka chikondi ndi chifundo chake ngati chipewa chaufumu,
Die uw leven behoedt voor het graf, U kroont met genade en ontferming;
5 amene akwaniritsa zokhumba zako ndi zinthu zabwino, kotero kuti umakhala wamphamvu zatsopano ngati mphungu.
Die al uw verlangens bevredigt, En als een adelaar uw jeugd verjongt!
6 Yehova amachita chilungamo ndipo amaweruza molungama onse opsinjika.
Jahweh oefent gerechtigheid uit, Schaft recht aan alle verdrukten:
7 Iye anadziwitsa Mose njira zake, ntchito zake kwa Aisraeli.
Hij toonde Moses zijn wegen, Aan de kinderen van Israël zijn machtige werken!
8 Yehova ndi wachifundo ndi wokoma mtima, wosakwiya msanga ndi wachikondi chochuluka.
Maar Jahweh is ook barmhartig en genadig, Lankmoedig en rijk aan ontferming:
9 Iye sadzatsutsa nthawi zonse, kapena kusunga mkwiyo wake kwamuyaya;
Hij toornt niet voor immer, En wrokt niet voor eeuwig;
10 satichitira molingana ndi machimo athu, kapena kutibwezera molingana ndi mphulupulu zathu.
Hij vergeldt ons niet naar onze zonden, En straft ons niet naar onze schuld.
11 Pakuti monga kumwamba kuli kutali ndi dziko lapansi, koteronso chikondi chake nʼchachikulu kwa iwo amene amamuopa;
Neen, zo hoog als de hemel Zich boven de aarde verheft, Zo groot is zijn goedheid Voor hen, die Hem vrezen!
12 monga kummawa kutalikirana ndi kumadzulo, koteronso Iye watichotsera mphulupulu zathu kuti zikhale kutali nafe.
Zo ver het oosten staat van het westen, Werpt Hij onze schuld van Zich af;
13 Monga bambo amachitira chifundo ana ake, choncho Yehova ali ndi chifundo ndi iwo amene amamuopa;
Zoals een vader zich over zijn kinderen ontfermt, Ontfermt Zich Jahweh over hen, die Hem vrezen:
14 pakuti Iye amadziwa momwe tinawumbidwira, amakumbukira kuti ndife fumbi.
Want Hij kent onze aard, En bedenkt, dat wij stof zijn.
15 Kunena za munthu, masiku ake ali ngati udzu, amaphuka ngati duwa la mʼmunda;
Als het gras zijn de dagen der mensen, Ze bloeien als een bloem op het veld:
16 koma mphepo imawombapo ndipo silionekanso ndipo malo ake sakumbukirikanso.
Waait er een wind overheen, ze is weg, En men weet niet meer, waar ze stond.
17 Koma kuchokera muyaya mpaka muyaya chikondi cha Yehova chili ndi iwo amene amamuopa, ndi chilungamo chake chili ndi ana a ana awo;
Maar van eeuwigheid is de goedheid van Jahweh, En tot in eeuwigheid blijft zij bestaan; Zijn barmhartigheid is voor hen, die Hem vrezen, En voor de kinderen van hun zonen:
18 iwo amene amasunga pangano lake ndi kukumbukira kumvera malangizo ake.
Voor hen, die zijn Verbond onderhouden, Zijn geboden gedenken en ze volbrengen.
19 Yehova wakhazikitsa mpando wake waufumu mmwamba ndipo ufumu wake umalamulira onse.
In de hemel heeft Jahweh zijn troon opgeslagen, En zijn koningschap beheerst het heelal;
20 Tamandani Yehova, inu angelo ake, amphamvu inu amene mumachita zimene amalamula, amene mumamvera mawu ake.
Jahweh’s engelen zingen Hem glorie, De sterke helden, die zijn geboden volbrengen, Die gehoorzamen aan zijn bevelen!
21 Tamandani Yehova, zolengedwa zonse zakumwamba, inu atumiki ake amene mumachita chifuniro chake.
Looft Jahweh dan, al zijn legerscharen, Zijn dienaars, die zijn wil volbrengt;
22 Tamandani Yehova, ntchito yake yonse kulikonse mu ulamuliro wake. Tamanda Yehova, iwe moyo wanga.
Looft Jahweh, al zijn werken, In iedere plaats van zijn rijk; Loof Jahweh, mijn ziel!

< Masalimo 103 >