< Masalimo 103 >

1 Salimo la Davide. Tamanda Yehova, iwe moyo wanga; ndi zonse zamʼkati mwanga zitamande dzina lake loyera.
Min Sjæl! lov Herren, og alt det, som i mig er, love hans hellige Navn.
2 Tamanda Yehova, iwe moyo wanga, ndipo usayiwale zabwino zake zonse.
Min Sjæl! lov Herren og glem ikke alle hans Velgerninger,
3 Amene amakhululuka machimo ako onse ndi kuchiritsa nthenda zako zonse,
ham, som forlader dig alle dine Misgerninger; ham, som læger alle dine Sygdomme;
4 amene awombola moyo wako ku dzenje ndi kukuveka chikondi ndi chifundo chake ngati chipewa chaufumu,
ham, som genløser dit Liv fra Graven; ham, som kroner dig med Miskundhed og Barmhjertighed;
5 amene akwaniritsa zokhumba zako ndi zinthu zabwino, kotero kuti umakhala wamphamvu zatsopano ngati mphungu.
ham, som mætter din Sjæl med det gode, at du bliver ung igen som Ørnen.
6 Yehova amachita chilungamo ndipo amaweruza molungama onse opsinjika.
Herren øver Retfærdighed og Ret for alle fortrykte.
7 Iye anadziwitsa Mose njira zake, ntchito zake kwa Aisraeli.
Han lod Mose vide sine Veje, Israels Børn sine Gerninger.
8 Yehova ndi wachifundo ndi wokoma mtima, wosakwiya msanga ndi wachikondi chochuluka.
Herren er barmhjertig og naadig, langmodig og af megen Miskundhed.
9 Iye sadzatsutsa nthawi zonse, kapena kusunga mkwiyo wake kwamuyaya;
Han skal ikke bestandig gaa i Rette, ej heller beholde Vrede evindelig.
10 satichitira molingana ndi machimo athu, kapena kutibwezera molingana ndi mphulupulu zathu.
Han har ikke gjort imod os efter vore Synder og ikke betalt os efter vore Misgerninger.
11 Pakuti monga kumwamba kuli kutali ndi dziko lapansi, koteronso chikondi chake nʼchachikulu kwa iwo amene amamuopa;
Thi saa høj Himmelen er over Jorden, har hans Miskundhed været mægtig over dem, som frygte ham.
12 monga kummawa kutalikirana ndi kumadzulo, koteronso Iye watichotsera mphulupulu zathu kuti zikhale kutali nafe.
Saa langt som Østen er fra Vesten, har han ladet vore Overtrædelser være langt fra os.
13 Monga bambo amachitira chifundo ana ake, choncho Yehova ali ndi chifundo ndi iwo amene amamuopa;
Ligesom en Fader forbarmer sig over Børn, saa forbarmer Herren sig over dem, som frygte ham.
14 pakuti Iye amadziwa momwe tinawumbidwira, amakumbukira kuti ndife fumbi.
Thi han kender vor Skabning, han kommer i Hu, at vi ere Støv.
15 Kunena za munthu, masiku ake ali ngati udzu, amaphuka ngati duwa la mʼmunda;
Et Menneskes Dage ere som Græs; som et Blomster paa Marken, saa blomstrer han.
16 koma mphepo imawombapo ndipo silionekanso ndipo malo ake sakumbukirikanso.
Naar et Vejr farer over det, da er det ikke mere, og dets Sted kender det ikke længere.
17 Koma kuchokera muyaya mpaka muyaya chikondi cha Yehova chili ndi iwo amene amamuopa, ndi chilungamo chake chili ndi ana a ana awo;
Men Herrens Miskundhed er fra Evighed og indtil Evighed over dem, som frygte ham, og hans Retfærdighed med Børnebørn,
18 iwo amene amasunga pangano lake ndi kukumbukira kumvera malangizo ake.
med dem, som holde hans Pagt, og med dem, som komme hans Befalinger i Hu for at gøre derefter.
19 Yehova wakhazikitsa mpando wake waufumu mmwamba ndipo ufumu wake umalamulira onse.
Herren har befæstet sin Trone i Himmelen, og hans Rige behersker alt.
20 Tamandani Yehova, inu angelo ake, amphamvu inu amene mumachita zimene amalamula, amene mumamvera mawu ake.
Lover Herren, I hans Engle! I vældige i Magt, som udrette hans Ord, idet I høre paa hans Ords Røst!
21 Tamandani Yehova, zolengedwa zonse zakumwamba, inu atumiki ake amene mumachita chifuniro chake.
Lover Herren, alle hans Hærskarer! I hans Tjenere, som gøre hans Villie!
22 Tamandani Yehova, ntchito yake yonse kulikonse mu ulamuliro wake. Tamanda Yehova, iwe moyo wanga.
Lover Herren, I hans Gerninger alle til Hobe! i alle hans Herredømmes Steder: Min Sjæl, lov Herren!

< Masalimo 103 >