< Masalimo 103 >

1 Salimo la Davide. Tamanda Yehova, iwe moyo wanga; ndi zonse zamʼkati mwanga zitamande dzina lake loyera.
David kah Aw ka hinglu, BOEIPA te uem lamtah, ka kotak boeih loh a ming cim te uem lah.
2 Tamanda Yehova, iwe moyo wanga, ndipo usayiwale zabwino zake zonse.
Aw ka hinglu, BOEIPA te uem lamtah amah kah a thaphu paek boeih te hnilh boeh.
3 Amene amakhululuka machimo ako onse ndi kuchiritsa nthenda zako zonse,
Nang kathaesainah boeih te khodawk han ngai tih, na tlohtat boeih aka hoeih sak,
4 amene awombola moyo wako ku dzenje ndi kukuveka chikondi ndi chifundo chake ngati chipewa chaufumu,
Na hingnah vaam khui lamkah aka tlan tih sitlohnah neh haidamnah te nang aka khuem sak loh,
5 amene akwaniritsa zokhumba zako ndi zinthu zabwino, kotero kuti umakhala wamphamvu zatsopano ngati mphungu.
Na kamrhui te hnothen neh a kum sak tih na camoe tue te atha bangla a thahuel sak.
6 Yehova amachita chilungamo ndipo amaweruza molungama onse opsinjika.
Hlang kah hnaemtaek aka yok rhoek boeih ham BOEIPA loh duengnah neh tiktamnah a saii pah.
7 Iye anadziwitsa Mose njira zake, ntchito zake kwa Aisraeli.
Moses taengah amah khosing, Israel ca rhoek taengah a khoboe te a tueng.
8 Yehova ndi wachifundo ndi wokoma mtima, wosakwiya msanga ndi wachikondi chochuluka.
Thinphoei neh lungvatnah BOEIPA loh thintoek a ueh tih sitlohnah neh baetawt.
9 Iye sadzatsutsa nthawi zonse, kapena kusunga mkwiyo wake kwamuyaya;
A yoeyah la ho pawt vetih, kumhal duela lunguen mahpawh.
10 satichitira molingana ndi machimo athu, kapena kutibwezera molingana ndi mphulupulu zathu.
Mamih kah tholhnah bangla mamih taengah saii pawt tih mamih kathaesainah bangla mamih taengah han suk moenih.
11 Pakuti monga kumwamba kuli kutali ndi dziko lapansi, koteronso chikondi chake nʼchachikulu kwa iwo amene amamuopa;
Diklai soah vaan a sang bangla amah aka rhih rhoek ham a sitlohnah khaw len.
12 monga kummawa kutalikirana ndi kumadzulo, koteronso Iye watichotsera mphulupulu zathu kuti zikhale kutali nafe.
Khocuk lamkah khotlak a lakhla bangla mamih kah boekoeknah te mamih taeng lamkah a lakhla sak coeng.
13 Monga bambo amachitira chifundo ana ake, choncho Yehova ali ndi chifundo ndi iwo amene amamuopa;
A nap a loh camoe rhoek te a haidam bangla amah aka rhih rhoek te BOEIPA loh a haidam.
14 pakuti Iye amadziwa momwe tinawumbidwira, amakumbukira kuti ndife fumbi.
Amah loh mamih kah benbonah he a ming tih mamih he laipi ni tila a poek.
15 Kunena za munthu, masiku ake ali ngati udzu, amaphuka ngati duwa la mʼmunda;
Hlanghing kah a tue sulrham bangla om tih khohmuen tamlaep bangla khooi van mai.
16 koma mphepo imawombapo ndipo silionekanso ndipo malo ake sakumbukirikanso.
Khohli loh anih a pah tih a hmata atah amah hmuen hmat voel pawh.
17 Koma kuchokera muyaya mpaka muyaya chikondi cha Yehova chili ndi iwo amene amamuopa, ndi chilungamo chake chili ndi ana a ana awo;
Tedae BOEIPA kah sitlohnah tah amah aka rhih rhoek taengah khosuen lamkah kumhal duela om tih a duengnah a ca rhoek kah a ca rhoek patoeng taengah,
18 iwo amene amasunga pangano lake ndi kukumbukira kumvera malangizo ake.
a paipi aka tuem tih a olrhi vai ham aka thoelh rhoek taengah om.
19 Yehova wakhazikitsa mpando wake waufumu mmwamba ndipo ufumu wake umalamulira onse.
BOEIPA loh vaan ah a ngolkhoel a hol tih a ram a cungkuem te a taemrhai.
20 Tamandani Yehova, inu angelo ake, amphamvu inu amene mumachita zimene amalamula, amene mumamvera mawu ake.
A olthui ol ngai ham amah kah olka bangla aka saii, thadueng puencawn, hlangrhalh rhoek loh BOEIPA te uem uh lah.
21 Tamandani Yehova, zolengedwa zonse zakumwamba, inu atumiki ake amene mumachita chifuniro chake.
Amah kah caempuei boeih loh BOEIPA te uem uh lamtah amah kah bibi boeih loh a kolonah te saii uh lah.
22 Tamandani Yehova, ntchito yake yonse kulikonse mu ulamuliro wake. Tamanda Yehova, iwe moyo wanga.
A khohung hmuen boeih kah a kutngo boeih BOEIPA te uem uh lah. Aw ka hinglu, BOEIPA te uem lah.

< Masalimo 103 >