< Masalimo 102 >

1 Pemphero la munthu wosautsidwa, pamene walefuka, nakhuthulira pamaso pa Yehova kulira kwakeko. Yehova imvani pemphero langa; kulira kwanga kopempha thandizo kufike kwa Inu.
Aberante mmɔborɔni mpaebɔ. Osu kyerɛ Awurade bere a ɔwɔ ahohia mu. Awurade, tie me mpaebɔ; na ma me mmoa ho sufrɛ nnu wʼanim.
2 Musandibisire nkhope yanu pamene ndili pa msautso. Munditcherere khutu; pamene ndiyitana ndiyankheni msanga.
Mmfa wʼanim nhintaw me bere a mewɔ ahohia mu. Brɛ wʼaso ase ma me; na sɛ misu frɛ wo a, gye me so ntɛm.
3 Pakuti masiku anga akupita ngati utsi; mafupa anga akunyeka ngati nkhuni zoyaka.
Me nkwanna reyera te sɛ wusiw; me nnompe adɔ sɛ nyansramma.
4 Mtima wanga wakanthidwa ndipo ukufota ngati udzu; ndipo ndimayiwala kudya chakudya changa.
Me koma abotow na akisa sɛ sare; na me kɔn nnɔ aduan.
5 Chifukwa cha kubuwula kwanga kofuwula ndatsala chikopa ndi mafupa okhaokha.
Mʼapinisi dennen nti maka ɔhonam ne nnompe.
6 Ndili ngati kadzidzi wa ku chipululu, monga kadzidzi pakati pa mabwinja.
Mete sɛ sare so patu, te sɛ patu a ɔte nnwiriwii mu.
7 Ndimagona osapeza tulo; ndakhala ngati mbalame yokhala yokha pa denga.
Meda hɔ a, mʼani gu so; mayɛ sɛ anomaa bi a ɔno nko ara si ɔdan atifi.
8 Tsiku lonse adani anga amandichita chipongwe; iwo amene amandinyoza, amagwiritsa ntchito dzina langa ngati temberero.
Da mu nyinaa mʼatamfo bɔ me akutia. Wɔn a wodi me ho fɛw no bɔ me din de dome.
9 Pakuti ndimadya phulusa ngati chakudya changa ndi kusakaniza chakumwa changa ndi misozi
Mede nsõ ayɛ mʼaduan na mede nusu fra me nsu mu
10 chifukwa cha ukali wanu waukulu, popeza Inu mwandinyamula ndi kunditayira kumbali.
esiane wʼabufuwhyew dennen no nti, woama me so, ayi me asi nkyɛn.
11 Masiku anga ali ngati mthunzi wa kumadzulo; Ine ndikufota ngati udzu.
Me nkwa nna te sɛ anwummere sunsuma; na mehyew sɛ sare.
12 Koma Inu Yehova, muli pa mpando wanu waufumu kwamuyaya; kudziwika kwanu ndi kokhazikika ku mibado yonse.
Nanso wo Awurade, woyɛ ɔhene daa daa; na wo din a ahyeta no te hɔ daa awo ntoatoaso nyinaa mu.
13 Inu mudzadzuka ndi kuchitira chifundo Ziyoni pakuti ndi nthawi yoti muonetse kukoma mtima kwanu pa iyeyo; nthawi yoyikika yafika.
Wobɛsɔre na woahu Sion mmɔbɔ; bere adu sɛ wuhu no mmɔbɔ; bere a wohyɛe no aso.
14 Pakuti miyala yake ndi yokondedwa kwa atumiki anu; fumbi lake lokha limawachititsa kuti amve chisoni.
Nʼabo som bo ma wʼasomfo; ne mfutuma hyɛ wɔn awerɛhow.
15 Mitundu ya anthu idzaopa dzina la Yehova, mafumu onse a dziko lapansi adzalemekeza ulemerero wanu.
Amanaman no besuro Awurade din; asase so ahemfo nyinaa bedi wʼanuonyam ni.
16 Pakuti Yehova adzamanganso Ziyoni ndi kuonekera mu ulemerero wake.
Awurade bɛkyekyere Sion bio, na wapue wɔ nʼanuonyam mu.
17 Iye adzayankha pemphero la anthu otayika; sadzanyoza kupempha kwawo.
Obetie mmɔborɔfo mpaebɔ; na ɔremmu nʼani ngu wɔn sufrɛ so.
18 Zimenezi zilembedwe chifukwa cha mibado ya mʼtsogolo, kuti anthu amene sanabadwe adzatamande Yehova:
Monkyerɛw eyi mma nkyirimma, sɛnea ɛbɛyɛ a wɔn a wonnya nwoo wɔn no bɛkamfo Awurade;
19 “Yehova anayangʼana pansi kuchokera ku malo ake opatulika mmwamba, kuchokera kumwamba anayangʼana dziko lapansi,
“Awurade hwɛɛ fam fi ne kronkronbea wɔ ɔsoro hɔ; ofi ɔsoro hwɛɛ asase,
20 kuti amve kubuwula kwa anthu a mʼndende, kuti apulumutse amene anayenera kuphedwa.”
sɛnea ɔbɛte nneduafo apinisi, na wɔagyaa wɔn a wɔabu wɔn kumfɔ no.”
21 Kotero dzina la Yehova lidzalengezedwa mu Ziyoni ndi matamando ake mu Yerusalemu,
Enti wɔbɛpae mu abɔ Awurade din wɔ Sion na wɔakamfo no wɔ Yerusalem,
22 pamene mitundu ya anthu ndi maufumu adzasonkhana kuti alambire Yehova.
bere a amanaman ne ahenni ahorow behyia mu na wɔasom Awurade.
23 Iye anathyola mphamvu zanga pa nthawi ya moyo wanga; Iyeyo anafupikitsa masiku anga.
Ɔmaa me yɛɛ mmerɛw wɔ bere a merenyin. Otwaa me nkwa nna so.
24 Choncho Ine ndinati: “Musandichotse, Inu Mulungu wanga, pakati pa masiku a moyo wanga; zaka zanu zimakhalabe pa mibado yonse.
Enti mekae se, “Me Onyankopɔn, mfa me nkɔ, wɔ me nkwa nna mfimfini; wo mfe wɔ hɔ daa kodu awo ntoatoaso nyinaa mu.
25 Pachiyambi Inu munakhazikitsa maziko a dziko lapansi ndipo mayiko akumwamba ndi ntchito ya manja anu.
Mfiase no wotoo asase fapem, na ɔsoro yɛ wo nsa ano adwuma.
26 Izi zidzatha, koma Inu mudzakhalapo; zidzatha ngati chovala. Mudzazisintha ngati chovala ndipo zidzatayidwa.
Ne nyinaa betwa mu na wo de, wobɛtena hɔ daa; wɔbɛtetew te sɛ atade. Wobɛsesa wɔn te sɛ ntama, na wɔbɛtow wɔn agu.
27 Koma Inu simusintha, ndipo zaka zanu sizidzatha.
Nanso wote sɛnea wote, na wo mfe to rentwa da.
28 Ana a atumiki anu adzakhala pamaso panu; zidzukulu zawo zidzakhazikika pamaso panu.”
Wʼasomfo mma bɛtena nkwa mu wɔ wʼanim; na wɔn asefo ase betim wɔ wʼanim.”

< Masalimo 102 >