< Masalimo 102 >

1 Pemphero la munthu wosautsidwa, pamene walefuka, nakhuthulira pamaso pa Yehova kulira kwakeko. Yehova imvani pemphero langa; kulira kwanga kopempha thandizo kufike kwa Inu.
Jehová, oye mi oración, y venga mi clamor a ti.
2 Musandibisire nkhope yanu pamene ndili pa msautso. Munditcherere khutu; pamene ndiyitana ndiyankheni msanga.
No escondas de mí tu rostro: en el día de mi angustia inclina a mí tu oreja; el día que te invocare, apresúrate a responderme.
3 Pakuti masiku anga akupita ngati utsi; mafupa anga akunyeka ngati nkhuni zoyaka.
Porque mis días se han consumido como humo; y mis huesos son quemados como en hogar.
4 Mtima wanga wakanthidwa ndipo ukufota ngati udzu; ndipo ndimayiwala kudya chakudya changa.
Mi corazón fue herido, y se secó como la yerba; por lo cual me olvidé de comer mi pan.
5 Chifukwa cha kubuwula kwanga kofuwula ndatsala chikopa ndi mafupa okhaokha.
Por la voz de mi gemido mis huesos se han pegado a mi carne.
6 Ndili ngati kadzidzi wa ku chipululu, monga kadzidzi pakati pa mabwinja.
Soy semejante al pelícano del desierto: soy como el búho de las soledades.
7 Ndimagona osapeza tulo; ndakhala ngati mbalame yokhala yokha pa denga.
Velo, y soy como el pájaro solitario sobre el tejado.
8 Tsiku lonse adani anga amandichita chipongwe; iwo amene amandinyoza, amagwiritsa ntchito dzina langa ngati temberero.
Cada día me afrentan mis enemigos; los que se enfurecen contra mí, conspiran contra mí.
9 Pakuti ndimadya phulusa ngati chakudya changa ndi kusakaniza chakumwa changa ndi misozi
Por lo cual yo como la ceniza a manera de pan; y mi bebida mezclo con lloro,
10 chifukwa cha ukali wanu waukulu, popeza Inu mwandinyamula ndi kunditayira kumbali.
A causa de tu enojo y de tu ira: porque me alzaste, y me arrojaste.
11 Masiku anga ali ngati mthunzi wa kumadzulo; Ine ndikufota ngati udzu.
Mis días son como la sombra que se va: y yo como la yerba me he secado.
12 Koma Inu Yehova, muli pa mpando wanu waufumu kwamuyaya; kudziwika kwanu ndi kokhazikika ku mibado yonse.
Mas tú, Jehová, para siempre permanecerás; y tu memoria para generación y generación.
13 Inu mudzadzuka ndi kuchitira chifundo Ziyoni pakuti ndi nthawi yoti muonetse kukoma mtima kwanu pa iyeyo; nthawi yoyikika yafika.
Tú levantándote habrás misericordia de Sión, porque es tiempo de tener misericordia de ella: porque el plazo es llegado.
14 Pakuti miyala yake ndi yokondedwa kwa atumiki anu; fumbi lake lokha limawachititsa kuti amve chisoni.
Porque tus siervos amaron sus piedras: y del polvo de ella tuvieron compasión.
15 Mitundu ya anthu idzaopa dzina la Yehova, mafumu onse a dziko lapansi adzalemekeza ulemerero wanu.
Y temerán las naciones el nombre de Jehová: y todos los reyes de la tierra tu gloria.
16 Pakuti Yehova adzamanganso Ziyoni ndi kuonekera mu ulemerero wake.
Por cuanto Jehová habrá edificado a Sión; y será visto en su gloria.
17 Iye adzayankha pemphero la anthu otayika; sadzanyoza kupempha kwawo.
Habrá mirado a la oración de los solitarios: y no habrá desechado el ruego de ellos.
18 Zimenezi zilembedwe chifukwa cha mibado ya mʼtsogolo, kuti anthu amene sanabadwe adzatamande Yehova:
Escribirse ha esto para la generación postrera: y el pueblo que se criará, alabará a Jehová.
19 “Yehova anayangʼana pansi kuchokera ku malo ake opatulika mmwamba, kuchokera kumwamba anayangʼana dziko lapansi,
Porque miró de lo alto de su santuario: Jehová miró desde los cielos a la tierra,
20 kuti amve kubuwula kwa anthu a mʼndende, kuti apulumutse amene anayenera kuphedwa.”
Para oír el gemido de los presos: para soltar a los sentenciados a muerte:
21 Kotero dzina la Yehova lidzalengezedwa mu Ziyoni ndi matamando ake mu Yerusalemu,
Porque publiquen en Sión el nombre de Jehová: y su alabanza en Jerusalem,
22 pamene mitundu ya anthu ndi maufumu adzasonkhana kuti alambire Yehova.
Cuando los pueblos se congregaren en uno, y los reinos para servir a Jehová.
23 Iye anathyola mphamvu zanga pa nthawi ya moyo wanga; Iyeyo anafupikitsa masiku anga.
El afligió mi fuerza en el camino, acortó mis días.
24 Choncho Ine ndinati: “Musandichotse, Inu Mulungu wanga, pakati pa masiku a moyo wanga; zaka zanu zimakhalabe pa mibado yonse.
Dije: Dios mío, no me cortes en el medio de mis días; por generación de generaciones son tus años.
25 Pachiyambi Inu munakhazikitsa maziko a dziko lapansi ndipo mayiko akumwamba ndi ntchito ya manja anu.
Tú fundaste la tierra antiguamente, y los cielos son obra de tus manos.
26 Izi zidzatha, koma Inu mudzakhalapo; zidzatha ngati chovala. Mudzazisintha ngati chovala ndipo zidzatayidwa.
Ellos perecerán, y tú permanecerás; y todos ellos como un vestido se envejecerán, como una ropa de vestir los mudarás, y serán mudados:
27 Koma Inu simusintha, ndipo zaka zanu sizidzatha.
Mas tú, el mismo, y tus años no se acabarán.
28 Ana a atumiki anu adzakhala pamaso panu; zidzukulu zawo zidzakhazikika pamaso panu.”
Los hijos de tus siervos habitarán, y su simiente será afirmada delante de ti.

< Masalimo 102 >