< Masalimo 102 >

1 Pemphero la munthu wosautsidwa, pamene walefuka, nakhuthulira pamaso pa Yehova kulira kwakeko. Yehova imvani pemphero langa; kulira kwanga kopempha thandizo kufike kwa Inu.
Molitev za ubozega, ko je v stiski in pred Gospoda izliva premišljevanje svoje. Gospod, čuj molitev mojo, in vpitje moje pridi do tebe.
2 Musandibisire nkhope yanu pamene ndili pa msautso. Munditcherere khutu; pamene ndiyitana ndiyankheni msanga.
Ne skrivaj mi obličja svojega, ko sem v stiski; nagni mi uho svoje, ko kličem; naglo me usliši.
3 Pakuti masiku anga akupita ngati utsi; mafupa anga akunyeka ngati nkhuni zoyaka.
Ker ginejo kakor dim dnevi moji; in kosti moje se sušé kakor pogorišče.
4 Mtima wanga wakanthidwa ndipo ukufota ngati udzu; ndipo ndimayiwala kudya chakudya changa.
Zadeto vene kakor trava srce moje, ker pozabljam použivati svojo jed.
5 Chifukwa cha kubuwula kwanga kofuwula ndatsala chikopa ndi mafupa okhaokha.
Od glasú zdihovanja mojega drži se kost moja mojega mesa.
6 Ndili ngati kadzidzi wa ku chipululu, monga kadzidzi pakati pa mabwinja.
Podoben sem pelikanu v puščavi; kakor sova sem v podrtinah.
7 Ndimagona osapeza tulo; ndakhala ngati mbalame yokhala yokha pa denga.
Vedno sem podoben samotnemu vrabcu na strehi.
8 Tsiku lonse adani anga amandichita chipongwe; iwo amene amandinyoza, amagwiritsa ntchito dzina langa ngati temberero.
Ves dan me sramoté sovražniki moji; zoper mene divjajoč prisezajo pri meni.
9 Pakuti ndimadya phulusa ngati chakudya changa ndi kusakaniza chakumwa changa ndi misozi
Ker pepel jem kakor kruh; in pijače svoje mešam z jokom.
10 chifukwa cha ukali wanu waukulu, popeza Inu mwandinyamula ndi kunditayira kumbali.
Zaradi nevolje tvoje in srdite jeze tvoje; ker vzdignil si me in vrgel me na tla.
11 Masiku anga ali ngati mthunzi wa kumadzulo; Ine ndikufota ngati udzu.
Dnevi moji so podobni senci, ki se je nagnila; in jaz sem se posušil kakor trava.
12 Koma Inu Yehova, muli pa mpando wanu waufumu kwamuyaya; kudziwika kwanu ndi kokhazikika ku mibado yonse.
Ti pa, Gospod, ostajaš vekomaj, in spomin tvoj od roda do roda.
13 Inu mudzadzuka ndi kuchitira chifundo Ziyoni pakuti ndi nthawi yoti muonetse kukoma mtima kwanu pa iyeyo; nthawi yoyikika yafika.
Ti bodeš vstal in usmilil se Sijona, ker čas je storiti mu milost, ker prišel je čas določeni,
14 Pakuti miyala yake ndi yokondedwa kwa atumiki anu; fumbi lake lokha limawachititsa kuti amve chisoni.
Ko se naj hlapci tvoji veselé njegovega kamenja, in milost storé njegovemu prahu;
15 Mitundu ya anthu idzaopa dzina la Yehova, mafumu onse a dziko lapansi adzalemekeza ulemerero wanu.
Da česté narodi ime Gospodovo, in vsi kralji zemlje čast tvojo.
16 Pakuti Yehova adzamanganso Ziyoni ndi kuonekera mu ulemerero wake.
Ko bode Gospod zidal Sijon in prikazal se v časti svoji,
17 Iye adzayankha pemphero la anthu otayika; sadzanyoza kupempha kwawo.
Ozrl se bode v nazega molitev, in ne bode zametal njih molitve.
18 Zimenezi zilembedwe chifukwa cha mibado ya mʼtsogolo, kuti anthu amene sanabadwe adzatamande Yehova:
Zapiše se naj to naslednjemu rodu, da ljudstvo poživljeno hvali Gospoda.
19 “Yehova anayangʼana pansi kuchokera ku malo ake opatulika mmwamba, kuchokera kumwamba anayangʼana dziko lapansi,
Ker pogledal bode z višave svetosti svoje Gospod, ozrl se z nebés na zemljo.
20 kuti amve kubuwula kwa anthu a mʼndende, kuti apulumutse amene anayenera kuphedwa.”
Da usliši jetnika zdihovanje, da oprosti njé, ki se že izdajajo smrti;
21 Kotero dzina la Yehova lidzalengezedwa mu Ziyoni ndi matamando ake mu Yerusalemu,
Da oznanjajo na Sijonu ime Gospodovo, in hvalo njegovo v Jeruzalemu,
22 pamene mitundu ya anthu ndi maufumu adzasonkhana kuti alambire Yehova.
Ko se zbirajo ljudstva in kralji čestit Gospoda.
23 Iye anathyola mphamvu zanga pa nthawi ya moyo wanga; Iyeyo anafupikitsa masiku anga.
Pobija sicer na tem poti moči moje, dnî moje krajša,
24 Choncho Ine ndinati: “Musandichotse, Inu Mulungu wanga, pakati pa masiku a moyo wanga; zaka zanu zimakhalabe pa mibado yonse.
Ali govorim: Bog moj mogočni, ne vzemi me v sredi mojih dnî; skozi vse rodove so dnevi tvoji,
25 Pachiyambi Inu munakhazikitsa maziko a dziko lapansi ndipo mayiko akumwamba ndi ntchito ya manja anu.
Predno si ustanovil zemljo, in so bila nebesa delo tvojih rok;
26 Izi zidzatha, koma Inu mudzakhalapo; zidzatha ngati chovala. Mudzazisintha ngati chovala ndipo zidzatayidwa.
Tisto bode prešlo, ti pa ostaneš; tisto, pravim, vse postara se kakor oblačilo; kakor obleko jih izpremeniš in izpremené se.
27 Koma Inu simusintha, ndipo zaka zanu sizidzatha.
Ti pa si isti, in let tvojih ni konca.
28 Ana a atumiki anu adzakhala pamaso panu; zidzukulu zawo zidzakhazikika pamaso panu.”
Sinovi hlapcev tvojih bodo prebivali, in njih seme se utrdi pred teboj.

< Masalimo 102 >