< Masalimo 102 >

1 Pemphero la munthu wosautsidwa, pamene walefuka, nakhuthulira pamaso pa Yehova kulira kwakeko. Yehova imvani pemphero langa; kulira kwanga kopempha thandizo kufike kwa Inu.
Modlitwa strapionego, gdy uciśniony wylewa przed PANEM swoją skargę. PANIE, wysłuchaj mojej modlitwy i niech przyjdzie do ciebie moje wołanie.
2 Musandibisire nkhope yanu pamene ndili pa msautso. Munditcherere khutu; pamene ndiyitana ndiyankheni msanga.
Nie ukrywaj przede mną swego oblicza, w dniu mego ucisku nakłoń ku mnie swego ucha; w dniu, w którym cię wzywam, szybko mnie wysłuchaj.
3 Pakuti masiku anga akupita ngati utsi; mafupa anga akunyeka ngati nkhuni zoyaka.
Moje dni bowiem nikną jak dym, a moje kości są rozpalone jak ognisko.
4 Mtima wanga wakanthidwa ndipo ukufota ngati udzu; ndipo ndimayiwala kudya chakudya changa.
Moje serce jest porażone i usycha jak trawa, [tak] że zapomniałem jeść chleb.
5 Chifukwa cha kubuwula kwanga kofuwula ndatsala chikopa ndi mafupa okhaokha.
Od głosu mego wołania moje kości przylgnęły mi do ciała.
6 Ndili ngati kadzidzi wa ku chipululu, monga kadzidzi pakati pa mabwinja.
Jestem podobny do pelikana na pustyni, jestem jak sowa na pustkowiu.
7 Ndimagona osapeza tulo; ndakhala ngati mbalame yokhala yokha pa denga.
Czuwam i jestem jak samotny wróbel na dachu.
8 Tsiku lonse adani anga amandichita chipongwe; iwo amene amandinyoza, amagwiritsa ntchito dzina langa ngati temberero.
Przez cały dzień znieważają mnie moi wrogowie i przeklinają mnie ci, którzy szaleją przeciwko mnie.
9 Pakuti ndimadya phulusa ngati chakudya changa ndi kusakaniza chakumwa changa ndi misozi
Jadam bowiem popiół jak chleb, a mój napój mieszam ze łzami;
10 chifukwa cha ukali wanu waukulu, popeza Inu mwandinyamula ndi kunditayira kumbali.
Z powodu twego gniewu i zapalczywości, bo podniosłeś mnie i strąciłeś.
11 Masiku anga ali ngati mthunzi wa kumadzulo; Ine ndikufota ngati udzu.
Moje dni są jak chylący się cień, a ja usycham jak trawa.
12 Koma Inu Yehova, muli pa mpando wanu waufumu kwamuyaya; kudziwika kwanu ndi kokhazikika ku mibado yonse.
Ale ty, PANIE, trwasz na wieki, a twoja pamięć z pokolenia na pokolenie.
13 Inu mudzadzuka ndi kuchitira chifundo Ziyoni pakuti ndi nthawi yoti muonetse kukoma mtima kwanu pa iyeyo; nthawi yoyikika yafika.
Powstaniesz i zmiłujesz się nad Syjonem, bo czas, byś się nad nim zlitował, gdyż nadszedł czas wyznaczony.
14 Pakuti miyala yake ndi yokondedwa kwa atumiki anu; fumbi lake lokha limawachititsa kuti amve chisoni.
Twoi słudzy bowiem miłują jego kamienie i litują się nad jego prochem;
15 Mitundu ya anthu idzaopa dzina la Yehova, mafumu onse a dziko lapansi adzalemekeza ulemerero wanu.
A poganie będą się bać imienia PANA i wszyscy królowie ziemi – twojej chwały;
16 Pakuti Yehova adzamanganso Ziyoni ndi kuonekera mu ulemerero wake.
Gdy PAN odbuduje Syjon i ukaże się w swojej chwale;
17 Iye adzayankha pemphero la anthu otayika; sadzanyoza kupempha kwawo.
Przychyli się do modlitwy opuszczonych i nie pogardzi ich modlitwą.
18 Zimenezi zilembedwe chifukwa cha mibado ya mʼtsogolo, kuti anthu amene sanabadwe adzatamande Yehova:
Zapiszą to dla przyszłego pokolenia, a lud, który ma być stworzony, będzie chwalić PANA.
19 “Yehova anayangʼana pansi kuchokera ku malo ake opatulika mmwamba, kuchokera kumwamba anayangʼana dziko lapansi,
Spojrzał bowiem z wysokości swojej świątyni; PAN popatrzył z nieba na ziemię;
20 kuti amve kubuwula kwa anthu a mʼndende, kuti apulumutse amene anayenera kuphedwa.”
Aby wysłuchać jęku więźniów i uwolnić skazanych na śmierć;
21 Kotero dzina la Yehova lidzalengezedwa mu Ziyoni ndi matamando ake mu Yerusalemu,
Aby głosili na Syjonie imię PANA i jego chwałę w Jeruzalem;
22 pamene mitundu ya anthu ndi maufumu adzasonkhana kuti alambire Yehova.
Gdy się zgromadzą razem narody i królestwa, aby służyć PANU.
23 Iye anathyola mphamvu zanga pa nthawi ya moyo wanga; Iyeyo anafupikitsa masiku anga.
Osłabił w drodze moją siłę, skrócił moje dni.
24 Choncho Ine ndinati: “Musandichotse, Inu Mulungu wanga, pakati pa masiku a moyo wanga; zaka zanu zimakhalabe pa mibado yonse.
Powiedziałem: Mój Boże, nie zabieraj mnie w połowie moich dni; twoje lata bowiem [trwają] z pokolenia na pokolenie.
25 Pachiyambi Inu munakhazikitsa maziko a dziko lapansi ndipo mayiko akumwamba ndi ntchito ya manja anu.
Ty dawno założyłeś [fundamenty] ziemi i niebiosa są dziełem twoich rąk.
26 Izi zidzatha, koma Inu mudzakhalapo; zidzatha ngati chovala. Mudzazisintha ngati chovala ndipo zidzatayidwa.
One przeminą, ale ty pozostajesz; wszystkie jak szata się zestarzeją, zmienisz je jak płaszcz i będą odmienione.
27 Koma Inu simusintha, ndipo zaka zanu sizidzatha.
Ale ty [zawsze jesteś] ten sam, a twoje lata nigdy się nie skończą.
28 Ana a atumiki anu adzakhala pamaso panu; zidzukulu zawo zidzakhazikika pamaso panu.”
Synowie twoich sług będą trwać [u ciebie], a ich potomstwo zostanie przed tobą utwierdzone.

< Masalimo 102 >