< Masalimo 102 >
1 Pemphero la munthu wosautsidwa, pamene walefuka, nakhuthulira pamaso pa Yehova kulira kwakeko. Yehova imvani pemphero langa; kulira kwanga kopempha thandizo kufike kwa Inu.
(곤고한 자가 마음이 상하여 그 근심을 여호와 앞에 토하는 기도) 여호와여, 내 기도를 들으시고 나의 부르짖음을 주께 상달케 하소서
2 Musandibisire nkhope yanu pamene ndili pa msautso. Munditcherere khutu; pamene ndiyitana ndiyankheni msanga.
나의 괴로운 날에 주의 얼굴을 내게 숨기지 마소서 주의 귀를 기울이사 내가 부르짖는 날에 속히 내게 응답하소서
3 Pakuti masiku anga akupita ngati utsi; mafupa anga akunyeka ngati nkhuni zoyaka.
대저 내 날이 연기 같이 소멸하며 내 뼈가 냉과리 같이 탔나이다
4 Mtima wanga wakanthidwa ndipo ukufota ngati udzu; ndipo ndimayiwala kudya chakudya changa.
내가 음식 먹기도 잊었음으로 내 마음이 풀 같이 쇠잔하였사오며
5 Chifukwa cha kubuwula kwanga kofuwula ndatsala chikopa ndi mafupa okhaokha.
나의 탄식 소리를 인하여 나의 살이 뼈에 붙었나이다
6 Ndili ngati kadzidzi wa ku chipululu, monga kadzidzi pakati pa mabwinja.
나는 광야의 당아새 같고 황폐한 곳의 부엉이 같이 되었사오며
7 Ndimagona osapeza tulo; ndakhala ngati mbalame yokhala yokha pa denga.
내가 밤을 새우니 지붕 위에 외로운 참새 같으니이다
8 Tsiku lonse adani anga amandichita chipongwe; iwo amene amandinyoza, amagwiritsa ntchito dzina langa ngati temberero.
내 원수들이 종일 나를 훼방하며 나를 대하여 미칠듯이 날치는 자들이 나를 가리켜 맹세하나이다
9 Pakuti ndimadya phulusa ngati chakudya changa ndi kusakaniza chakumwa changa ndi misozi
나는 재를 양식 같이 먹으며 나의 마심에는 눈물을 섞었사오니
10 chifukwa cha ukali wanu waukulu, popeza Inu mwandinyamula ndi kunditayira kumbali.
이는 주의 분과 노를 인함이라 주께서 나를 드셨다가 던지셨나이다
11 Masiku anga ali ngati mthunzi wa kumadzulo; Ine ndikufota ngati udzu.
내 날이 기울어지는 그림자 같고 내가 풀의 쇠잔함 같으니이다
12 Koma Inu Yehova, muli pa mpando wanu waufumu kwamuyaya; kudziwika kwanu ndi kokhazikika ku mibado yonse.
여호와여, 주는 영원히 계시고 주의 기념 명칭은 대대에 이르리이다
13 Inu mudzadzuka ndi kuchitira chifundo Ziyoni pakuti ndi nthawi yoti muonetse kukoma mtima kwanu pa iyeyo; nthawi yoyikika yafika.
주께서 일어나사 시온을 긍휼히 여기시리니 지금은 그를 긍휼히 여기실 때라 정한 기한이 옴이니이다
14 Pakuti miyala yake ndi yokondedwa kwa atumiki anu; fumbi lake lokha limawachititsa kuti amve chisoni.
주의 종들이 시온의 돌들을 즐거워하며 그 티끌도 연휼히 여기나이다
15 Mitundu ya anthu idzaopa dzina la Yehova, mafumu onse a dziko lapansi adzalemekeza ulemerero wanu.
이에 열방이 여호와의 이름을 경외하며 세계 열왕이 주의 영광을 경외하리니
16 Pakuti Yehova adzamanganso Ziyoni ndi kuonekera mu ulemerero wake.
대저 여호와께서 시온을 건설하시고 그 영광 중에 나타나셨음이라
17 Iye adzayankha pemphero la anthu otayika; sadzanyoza kupempha kwawo.
여호와께서 빈궁한 자의 기도를 돌아보시며 저희 기도를 멸시치 아니하셨도다
18 Zimenezi zilembedwe chifukwa cha mibado ya mʼtsogolo, kuti anthu amene sanabadwe adzatamande Yehova:
이 일이 장래 세대를 위하여 기록되리니 창조함을 받을 백성이 여호와를 찬송하리로다
19 “Yehova anayangʼana pansi kuchokera ku malo ake opatulika mmwamba, kuchokera kumwamba anayangʼana dziko lapansi,
여호와께서 그 높은 성소에서 하감하시며 하늘에서 땅을 감찰하셨으니
20 kuti amve kubuwula kwa anthu a mʼndende, kuti apulumutse amene anayenera kuphedwa.”
이는 갇힌자의 탄식을 들으시며 죽이기로 정한 자를 해방하사
21 Kotero dzina la Yehova lidzalengezedwa mu Ziyoni ndi matamando ake mu Yerusalemu,
여호와의 이름을 시온에서 그 영예를 예루살렘에서 선포케 하려 하심이라
22 pamene mitundu ya anthu ndi maufumu adzasonkhana kuti alambire Yehova.
때에 민족들과 나라들이 모여 여호와를 섬기리로다
23 Iye anathyola mphamvu zanga pa nthawi ya moyo wanga; Iyeyo anafupikitsa masiku anga.
저가 내 힘을 중도에 쇠약케 하시며 내 날을 단촉케 하셨도다
24 Choncho Ine ndinati: “Musandichotse, Inu Mulungu wanga, pakati pa masiku a moyo wanga; zaka zanu zimakhalabe pa mibado yonse.
나의 말이 나의 하나님이여, 나의 중년에 나를 데려가지 마옵소서 주의 연대는 대대에 무궁하니이다
25 Pachiyambi Inu munakhazikitsa maziko a dziko lapansi ndipo mayiko akumwamba ndi ntchito ya manja anu.
주께서 옛적에 땅의 기초를 두셨사오며 하늘도 주의 손으로 지으신 바니이다
26 Izi zidzatha, koma Inu mudzakhalapo; zidzatha ngati chovala. Mudzazisintha ngati chovala ndipo zidzatayidwa.
천지는 없어지려니와 주는 영존하시겠고 그것들은 다 옷 같이 낡으리니 의복같이 바꾸시면 바뀌려니와
27 Koma Inu simusintha, ndipo zaka zanu sizidzatha.
주는 여상하시고 주의 년대는 무궁하리이다
28 Ana a atumiki anu adzakhala pamaso panu; zidzukulu zawo zidzakhazikika pamaso panu.”
주의 종들의 자손이 항상 있고 그 후손이 주의 앞에 굳게 서리이다 하였도다