< Masalimo 102 >

1 Pemphero la munthu wosautsidwa, pamene walefuka, nakhuthulira pamaso pa Yehova kulira kwakeko. Yehova imvani pemphero langa; kulira kwanga kopempha thandizo kufike kwa Inu.
[Gebet eines Elenden, wenn er verschmachtet und seine Klage vor Jehova ausschüttet.] Jehova, höre mein Gebet, und laß zu dir kommen mein Schreien!
2 Musandibisire nkhope yanu pamene ndili pa msautso. Munditcherere khutu; pamene ndiyitana ndiyankheni msanga.
Verbirg dein Angesicht nicht vor mir am Tage meiner Bedrängnis; neige zu mir dein Ohr; an dem Tage, da ich rufe, erhöre mich eilends!
3 Pakuti masiku anga akupita ngati utsi; mafupa anga akunyeka ngati nkhuni zoyaka.
Denn wie Rauch entschwinden meine Tage, und meine Gebeine glühen wie ein Brand.
4 Mtima wanga wakanthidwa ndipo ukufota ngati udzu; ndipo ndimayiwala kudya chakudya changa.
Wie Kraut ist versengt und verdorrt mein Herz, daß ich vergessen habe, [O. denn ich habe vergessen] mein Brot zu essen.
5 Chifukwa cha kubuwula kwanga kofuwula ndatsala chikopa ndi mafupa okhaokha.
Ob der Stimme meines Seufzens klebt mein Gebein an meinem Fleische.
6 Ndili ngati kadzidzi wa ku chipululu, monga kadzidzi pakati pa mabwinja.
Ich gleiche dem Pelikan der Wüste, bin wie die Eule der Einöden. [O. der Trümmer]
7 Ndimagona osapeza tulo; ndakhala ngati mbalame yokhala yokha pa denga.
Ich wache, und bin wie ein einsamer Vogel auf dem Dache.
8 Tsiku lonse adani anga amandichita chipongwe; iwo amene amandinyoza, amagwiritsa ntchito dzina langa ngati temberero.
Den ganzen Tag höhnen mich meine Feinde; die wider mich rasen, schwören bei mir.
9 Pakuti ndimadya phulusa ngati chakudya changa ndi kusakaniza chakumwa changa ndi misozi
Denn Asche esse ich wie Brot, und meinen Trank vermische ich mit Tränen
10 chifukwa cha ukali wanu waukulu, popeza Inu mwandinyamula ndi kunditayira kumbali.
Vor deinem Zorn und deinem Grimm; denn du hast mich emporgehoben und hast mich hingeworfen.
11 Masiku anga ali ngati mthunzi wa kumadzulo; Ine ndikufota ngati udzu.
Meine Tage sind wie ein gestreckter Schatten, und ich verdorre wie Kraut.
12 Koma Inu Yehova, muli pa mpando wanu waufumu kwamuyaya; kudziwika kwanu ndi kokhazikika ku mibado yonse.
Du aber, Jehova, bleibst auf ewig, und dein Gedächtnis [Vergl. 2. Mose 3,15] ist von Geschlecht zu Geschlecht.
13 Inu mudzadzuka ndi kuchitira chifundo Ziyoni pakuti ndi nthawi yoti muonetse kukoma mtima kwanu pa iyeyo; nthawi yoyikika yafika.
Du wirst aufstehen, wirst dich Zions erbarmen; denn es ist Zeit, es zu begnadigen, denn gekommen ist die bestimmte Zeit;
14 Pakuti miyala yake ndi yokondedwa kwa atumiki anu; fumbi lake lokha limawachititsa kuti amve chisoni.
Denn deine Knechte haben Gefallen an seinen Steinen und haben Mitleid mit seinem Schutt.
15 Mitundu ya anthu idzaopa dzina la Yehova, mafumu onse a dziko lapansi adzalemekeza ulemerero wanu.
Und die Nationen werden den Namen Jehovas fürchten, und alle Könige der Erde deine Herrlichkeit.
16 Pakuti Yehova adzamanganso Ziyoni ndi kuonekera mu ulemerero wake.
Denn Jehova wird Zion aufbauen, wird erscheinen in seiner Herrlichkeit;
17 Iye adzayankha pemphero la anthu otayika; sadzanyoza kupempha kwawo.
Er wird sich wenden zum Gebete des Entblößten, und ihr Gebet wird er nicht verachten.
18 Zimenezi zilembedwe chifukwa cha mibado ya mʼtsogolo, kuti anthu amene sanabadwe adzatamande Yehova:
Das wird aufgeschrieben werden für das künftige Geschlecht; und ein Volk, das erschaffen werden soll, wird Jehova [Hebr. Jah] loben.
19 “Yehova anayangʼana pansi kuchokera ku malo ake opatulika mmwamba, kuchokera kumwamba anayangʼana dziko lapansi,
Denn er hat herniedergeblickt von der Höhe seines Heiligtums, Jehova hat herabgeschaut vom Himmel auf die Erde,
20 kuti amve kubuwula kwa anthu a mʼndende, kuti apulumutse amene anayenera kuphedwa.”
Um zu hören das Seufzen des Gefangenen, um zu lösen die Kinder des Todes;
21 Kotero dzina la Yehova lidzalengezedwa mu Ziyoni ndi matamando ake mu Yerusalemu,
Damit man den Namen Jehovas verkündige in Zion, und in Jerusalem sein Lob,
22 pamene mitundu ya anthu ndi maufumu adzasonkhana kuti alambire Yehova.
Wenn die Völker sich versammeln werden allzumal, und die Königreiche, um Jehova zu dienen.
23 Iye anathyola mphamvu zanga pa nthawi ya moyo wanga; Iyeyo anafupikitsa masiku anga.
Er hat meine Kraft gebeugt auf dem Wege, hat verkürzt meine Tage.
24 Choncho Ine ndinati: “Musandichotse, Inu Mulungu wanga, pakati pa masiku a moyo wanga; zaka zanu zimakhalabe pa mibado yonse.
Ich sprach: Mein Gott, [El] nimm mich nicht hinweg in der Hälfte meiner Tage! -Von Geschlecht zu Geschlecht sind deine Jahre.
25 Pachiyambi Inu munakhazikitsa maziko a dziko lapansi ndipo mayiko akumwamba ndi ntchito ya manja anu.
Du hast vormals die Erde gegründet, und die Himmel sind deiner Hände Werk.
26 Izi zidzatha, koma Inu mudzakhalapo; zidzatha ngati chovala. Mudzazisintha ngati chovala ndipo zidzatayidwa.
Sie werden untergehen, du aber bleibst; und sie alle werden veralten wie ein Kleid; wie ein Gewand wirst du sie verwandeln, [O. wechseln] und sie werden verwandelt werden;
27 Koma Inu simusintha, ndipo zaka zanu sizidzatha.
Du aber bist derselbe, [O. er; od.: der da ist, d. h. der unveränderlich in sich selbst ewig besteht; vergl. 5. Mose 32,39; Neh. 9,6] und deine Jahre enden nicht.
28 Ana a atumiki anu adzakhala pamaso panu; zidzukulu zawo zidzakhazikika pamaso panu.”
Die Söhne deiner Knechte werden wohnen, [d. h. im Lande] und ihr Same wird vor dir feststehen.

< Masalimo 102 >