< Masalimo 102 >

1 Pemphero la munthu wosautsidwa, pamene walefuka, nakhuthulira pamaso pa Yehova kulira kwakeko. Yehova imvani pemphero langa; kulira kwanga kopempha thandizo kufike kwa Inu.
Prière de l'affligé, lorsqu'il est abattu et qu'il exhale sa plainte devant l'Éternel. Éternel, écoute ma prière, Et que mon cri parvienne jusqu'à toi!,
2 Musandibisire nkhope yanu pamene ndili pa msautso. Munditcherere khutu; pamene ndiyitana ndiyankheni msanga.
Ne me cache pas ta face, au jour de ma détresse; Incline vers moi ton oreille! Au jour où je t'invoque, hâte-toi de me répondre!
3 Pakuti masiku anga akupita ngati utsi; mafupa anga akunyeka ngati nkhuni zoyaka.
Car mes jours s'évanouissent comme une fumée, Et mes os se consument comme un brasier.
4 Mtima wanga wakanthidwa ndipo ukufota ngati udzu; ndipo ndimayiwala kudya chakudya changa.
Mon coeur a été frappé, et il se dessèche comme l'herbe; J'oublie même de manger mon pain.
5 Chifukwa cha kubuwula kwanga kofuwula ndatsala chikopa ndi mafupa okhaokha.
Je pousse de tels gémissements. Que mes os s'attachent à ma chair.
6 Ndili ngati kadzidzi wa ku chipululu, monga kadzidzi pakati pa mabwinja.
Je ressemble au pélican du désert; Je suis comme le hibou des ruines.
7 Ndimagona osapeza tulo; ndakhala ngati mbalame yokhala yokha pa denga.
Je n'ai plus de sommeil, Et je suis comme le passereau solitaire sur un toit.
8 Tsiku lonse adani anga amandichita chipongwe; iwo amene amandinyoza, amagwiritsa ntchito dzina langa ngati temberero.
Tous les jours, mes ennemis m'outragent. Et mes adversaires en fureur prononcent mon nom Comme un nom maudit.
9 Pakuti ndimadya phulusa ngati chakudya changa ndi kusakaniza chakumwa changa ndi misozi
Je fais de la cendre ma nourriture. Et je mêle des larmes à mon breuvage,
10 chifukwa cha ukali wanu waukulu, popeza Inu mwandinyamula ndi kunditayira kumbali.
A cause de ton indignation et de ton courroux; Car tu m'as saisi et rejeté au loin.
11 Masiku anga ali ngati mthunzi wa kumadzulo; Ine ndikufota ngati udzu.
Mes jours s'inclinent comme l'ombre du soir Et je me dessèche comme l'herbe.
12 Koma Inu Yehova, muli pa mpando wanu waufumu kwamuyaya; kudziwika kwanu ndi kokhazikika ku mibado yonse.
Mais toi, ô Éternel, tu règnes à perpétuité. Et ta mémoire subsiste d'âge en âge.
13 Inu mudzadzuka ndi kuchitira chifundo Ziyoni pakuti ndi nthawi yoti muonetse kukoma mtima kwanu pa iyeyo; nthawi yoyikika yafika.
Tu te lèveras, tu auras pitié de Sion. Il est temps de lui faire grâce: L'heure est venue!
14 Pakuti miyala yake ndi yokondedwa kwa atumiki anu; fumbi lake lokha limawachititsa kuti amve chisoni.
Car tes serviteurs en chérissent les pierres; Ils aiment jusqu'à sa poussière.
15 Mitundu ya anthu idzaopa dzina la Yehova, mafumu onse a dziko lapansi adzalemekeza ulemerero wanu.
Alors les peuples craindront le nom de l'Éternel. Tous les rois de la terre, ô Dieu, verront ta gloire,
16 Pakuti Yehova adzamanganso Ziyoni ndi kuonekera mu ulemerero wake.
Parce que l'Éternel aura rebâti Sion, Qu'il aura paru dans sa gloire,
17 Iye adzayankha pemphero la anthu otayika; sadzanyoza kupempha kwawo.
Qu'il aura écouté la requête des misérables, Et n'aura pas méprisé leur supplication.
18 Zimenezi zilembedwe chifukwa cha mibado ya mʼtsogolo, kuti anthu amene sanabadwe adzatamande Yehova:
Cela sera écrit pour la génération future. Et le peuple qui sera créé, louera l'Éternel.
19 “Yehova anayangʼana pansi kuchokera ku malo ake opatulika mmwamba, kuchokera kumwamba anayangʼana dziko lapansi,
Car l'Éternel abaissera ses regards, Du haut de sa demeure sainte. Et, du haut des cieux, l'Éternel jettera les yeux sur la terre,
20 kuti amve kubuwula kwa anthu a mʼndende, kuti apulumutse amene anayenera kuphedwa.”
Pour écouter les gémissements du captif, Pour délivrer ceux qui sont voués à la mort.
21 Kotero dzina la Yehova lidzalengezedwa mu Ziyoni ndi matamando ake mu Yerusalemu,
Alors on célébrera le nom de l'Éternel dans Sion, Et ses louanges dans Jérusalem,
22 pamene mitundu ya anthu ndi maufumu adzasonkhana kuti alambire Yehova.
Quand tous les peuples, ainsi que les royaumes, Se rassembleront pour servir l'Eternel.
23 Iye anathyola mphamvu zanga pa nthawi ya moyo wanga; Iyeyo anafupikitsa masiku anga.
Dieu a brisé ma force au milieu de ma course; Il a abrégé mes jours.
24 Choncho Ine ndinati: “Musandichotse, Inu Mulungu wanga, pakati pa masiku a moyo wanga; zaka zanu zimakhalabe pa mibado yonse.
J'ai dit: mon Dieu, ne m'enlève pas à la fleur de l'âge, Toi dont les années subsistent de siècle en siècle!
25 Pachiyambi Inu munakhazikitsa maziko a dziko lapansi ndipo mayiko akumwamba ndi ntchito ya manja anu.
Tu as jadis fondé la terre, Et les cieux sont l'oeuvre de tes mains.
26 Izi zidzatha, koma Inu mudzakhalapo; zidzatha ngati chovala. Mudzazisintha ngati chovala ndipo zidzatayidwa.
Ils périront; mais toi, tu subsisteras. Ils s'useront tous comme un vêtement; Tu les changeras comme un habit, et ils passeront.
27 Koma Inu simusintha, ndipo zaka zanu sizidzatha.
Mais toi, tu es toujours le même. Et tes années ne finiront point.
28 Ana a atumiki anu adzakhala pamaso panu; zidzukulu zawo zidzakhazikika pamaso panu.”
Les enfants de tes serviteurs auront une demeure assurée, Et leur postérité se perpétuera sous tes yeux.

< Masalimo 102 >