< Masalimo 102 >

1 Pemphero la munthu wosautsidwa, pamene walefuka, nakhuthulira pamaso pa Yehova kulira kwakeko. Yehova imvani pemphero langa; kulira kwanga kopempha thandizo kufike kwa Inu.
Prière d’un malheureux, lorsqu’il est abattu et qu’il répand sa plainte devant l’Éternel. Éternel, écoute ma prière, Et que mon cri parvienne jusqu’à toi!
2 Musandibisire nkhope yanu pamene ndili pa msautso. Munditcherere khutu; pamene ndiyitana ndiyankheni msanga.
Ne me cache pas ta face au jour de ma détresse! Incline vers moi ton oreille quand je crie! Hâte-toi de m’exaucer!
3 Pakuti masiku anga akupita ngati utsi; mafupa anga akunyeka ngati nkhuni zoyaka.
Car mes jours s’évanouissent en fumée, Et mes os sont enflammés comme un tison.
4 Mtima wanga wakanthidwa ndipo ukufota ngati udzu; ndipo ndimayiwala kudya chakudya changa.
Mon cœur est frappé et se dessèche comme l’herbe; J’oublie même de manger mon pain.
5 Chifukwa cha kubuwula kwanga kofuwula ndatsala chikopa ndi mafupa okhaokha.
Mes gémissements sont tels Que mes os s’attachent à ma chair.
6 Ndili ngati kadzidzi wa ku chipululu, monga kadzidzi pakati pa mabwinja.
Je ressemble au pélican du désert, Je suis comme le chat-huant des ruines;
7 Ndimagona osapeza tulo; ndakhala ngati mbalame yokhala yokha pa denga.
Je n’ai plus de sommeil, et je suis Comme l’oiseau solitaire sur un toit.
8 Tsiku lonse adani anga amandichita chipongwe; iwo amene amandinyoza, amagwiritsa ntchito dzina langa ngati temberero.
Chaque jour mes ennemis m’outragent, Et c’est par moi que jurent mes adversaires en fureur.
9 Pakuti ndimadya phulusa ngati chakudya changa ndi kusakaniza chakumwa changa ndi misozi
Je mange la poussière au lieu de pain, Et je mêle des larmes à ma boisson,
10 chifukwa cha ukali wanu waukulu, popeza Inu mwandinyamula ndi kunditayira kumbali.
A cause de ta colère et de ta fureur; Car tu m’as soulevé et jeté au loin.
11 Masiku anga ali ngati mthunzi wa kumadzulo; Ine ndikufota ngati udzu.
Mes jours sont comme l’ombre à son déclin, Et je me dessèche comme l’herbe.
12 Koma Inu Yehova, muli pa mpando wanu waufumu kwamuyaya; kudziwika kwanu ndi kokhazikika ku mibado yonse.
Mais toi, Éternel! Tu règnes à perpétuité, Et ta mémoire dure de génération en génération.
13 Inu mudzadzuka ndi kuchitira chifundo Ziyoni pakuti ndi nthawi yoti muonetse kukoma mtima kwanu pa iyeyo; nthawi yoyikika yafika.
Tu te lèveras, tu auras pitié de Sion; Car le temps d’avoir pitié d’elle, Le temps fixé est à son terme;
14 Pakuti miyala yake ndi yokondedwa kwa atumiki anu; fumbi lake lokha limawachititsa kuti amve chisoni.
Car tes serviteurs en aiment les pierres, Ils en chérissent la poussière.
15 Mitundu ya anthu idzaopa dzina la Yehova, mafumu onse a dziko lapansi adzalemekeza ulemerero wanu.
Alors les nations craindront le nom de l’Éternel, Et tous les rois de la terre ta gloire.
16 Pakuti Yehova adzamanganso Ziyoni ndi kuonekera mu ulemerero wake.
Oui, l’Éternel rebâtira Sion, Il se montrera dans sa gloire.
17 Iye adzayankha pemphero la anthu otayika; sadzanyoza kupempha kwawo.
Il est attentif à la prière du misérable, Il ne dédaigne pas sa prière.
18 Zimenezi zilembedwe chifukwa cha mibado ya mʼtsogolo, kuti anthu amene sanabadwe adzatamande Yehova:
Que cela soit écrit pour la génération future, Et que le peuple qui sera créé célèbre l’Éternel!
19 “Yehova anayangʼana pansi kuchokera ku malo ake opatulika mmwamba, kuchokera kumwamba anayangʼana dziko lapansi,
Car il regarde du lieu élevé de sa sainteté; Du haut des cieux l’Éternel regarde sur la terre,
20 kuti amve kubuwula kwa anthu a mʼndende, kuti apulumutse amene anayenera kuphedwa.”
Pour écouter les gémissements des captifs, Pour délivrer ceux qui vont périr,
21 Kotero dzina la Yehova lidzalengezedwa mu Ziyoni ndi matamando ake mu Yerusalemu,
Afin qu’ils publient dans Sion le nom de l’Éternel, Et ses louanges dans Jérusalem,
22 pamene mitundu ya anthu ndi maufumu adzasonkhana kuti alambire Yehova.
Quand tous les peuples s’assembleront, Et tous les royaumes, pour servir l’Éternel.
23 Iye anathyola mphamvu zanga pa nthawi ya moyo wanga; Iyeyo anafupikitsa masiku anga.
Il a brisé ma force dans la route, Il a abrégé mes jours.
24 Choncho Ine ndinati: “Musandichotse, Inu Mulungu wanga, pakati pa masiku a moyo wanga; zaka zanu zimakhalabe pa mibado yonse.
Je dis: Mon Dieu, ne m’enlève pas au milieu de mes jours, Toi, dont les années durent éternellement!
25 Pachiyambi Inu munakhazikitsa maziko a dziko lapansi ndipo mayiko akumwamba ndi ntchito ya manja anu.
Tu as anciennement fondé la terre, Et les cieux sont l’ouvrage de tes mains.
26 Izi zidzatha, koma Inu mudzakhalapo; zidzatha ngati chovala. Mudzazisintha ngati chovala ndipo zidzatayidwa.
Ils périront, mais tu subsisteras; Ils s’useront tous comme un vêtement; Tu les changeras comme un habit, et ils seront changés.
27 Koma Inu simusintha, ndipo zaka zanu sizidzatha.
Mais toi, tu restes le même, Et tes années ne finiront point.
28 Ana a atumiki anu adzakhala pamaso panu; zidzukulu zawo zidzakhazikika pamaso panu.”
Les fils de tes serviteurs habiteront leur pays, Et leur postérité s’affermira devant toi.

< Masalimo 102 >