< Masalimo 102 >

1 Pemphero la munthu wosautsidwa, pamene walefuka, nakhuthulira pamaso pa Yehova kulira kwakeko. Yehova imvani pemphero langa; kulira kwanga kopempha thandizo kufike kwa Inu.
prayer to/for afflicted for to enfeeble and to/for face: before LORD to pour: pour complaint his LORD to hear: hear [emph?] prayer my and cry my to(wards) you to come (in): come
2 Musandibisire nkhope yanu pamene ndili pa msautso. Munditcherere khutu; pamene ndiyitana ndiyankheni msanga.
not to hide face your from me in/on/with day to distress to/for me to stretch to(wards) me ear your in/on/with day to call: call to to hasten to answer me
3 Pakuti masiku anga akupita ngati utsi; mafupa anga akunyeka ngati nkhuni zoyaka.
for to end: expend in/on/with smoke day my and bone my like burning to scorch
4 Mtima wanga wakanthidwa ndipo ukufota ngati udzu; ndipo ndimayiwala kudya chakudya changa.
to smite like/as vegetation and to wither heart my for to forget from to eat food: bread my
5 Chifukwa cha kubuwula kwanga kofuwula ndatsala chikopa ndi mafupa okhaokha.
from voice: sound sighing my to cleave bone my to/for flesh my
6 Ndili ngati kadzidzi wa ku chipululu, monga kadzidzi pakati pa mabwinja.
to resemble to/for pelican wilderness to be like/as owl desolation
7 Ndimagona osapeza tulo; ndakhala ngati mbalame yokhala yokha pa denga.
to watch and to be like/as bird be alone upon roof
8 Tsiku lonse adani anga amandichita chipongwe; iwo amene amandinyoza, amagwiritsa ntchito dzina langa ngati temberero.
all [the] day to taunt me enemy my to boast: rave madly me in/on/with me to swear
9 Pakuti ndimadya phulusa ngati chakudya changa ndi kusakaniza chakumwa changa ndi misozi
for ashes like/as food: bread to eat and drink my in/on/with weeping to mix
10 chifukwa cha ukali wanu waukulu, popeza Inu mwandinyamula ndi kunditayira kumbali.
from face: because indignation your and wrath your for to lift: raise me and to throw me
11 Masiku anga ali ngati mthunzi wa kumadzulo; Ine ndikufota ngati udzu.
day my like/as shadow to stretch and I like/as vegetation to wither
12 Koma Inu Yehova, muli pa mpando wanu waufumu kwamuyaya; kudziwika kwanu ndi kokhazikika ku mibado yonse.
and you(m. s.) LORD to/for forever: enduring to dwell and memorial your to/for generation and generation
13 Inu mudzadzuka ndi kuchitira chifundo Ziyoni pakuti ndi nthawi yoti muonetse kukoma mtima kwanu pa iyeyo; nthawi yoyikika yafika.
you(m. s.) to arise: rise to have compassion Zion for time to/for be gracious her for to come (in): come meeting: time appointed
14 Pakuti miyala yake ndi yokondedwa kwa atumiki anu; fumbi lake lokha limawachititsa kuti amve chisoni.
for to accept servant/slave your [obj] stone her and [obj] dust her be gracious
15 Mitundu ya anthu idzaopa dzina la Yehova, mafumu onse a dziko lapansi adzalemekeza ulemerero wanu.
and to fear: revere nation [obj] name LORD and all king [the] land: country/planet [obj] glory your
16 Pakuti Yehova adzamanganso Ziyoni ndi kuonekera mu ulemerero wake.
for to build LORD Zion to see: see in/on/with glory his
17 Iye adzayankha pemphero la anthu otayika; sadzanyoza kupempha kwawo.
to turn to(wards) prayer [the] destitute and not to despise [obj] prayer their
18 Zimenezi zilembedwe chifukwa cha mibado ya mʼtsogolo, kuti anthu amene sanabadwe adzatamande Yehova:
to write this to/for generation last and people to create to boast: praise LORD
19 “Yehova anayangʼana pansi kuchokera ku malo ake opatulika mmwamba, kuchokera kumwamba anayangʼana dziko lapansi,
for to look from height holiness his LORD from heaven to(wards) land: country/planet to look
20 kuti amve kubuwula kwa anthu a mʼndende, kuti apulumutse amene anayenera kuphedwa.”
to/for to hear: hear groaning prisoner to/for to open son: descendant/people death
21 Kotero dzina la Yehova lidzalengezedwa mu Ziyoni ndi matamando ake mu Yerusalemu,
to/for to recount in/on/with Zion name LORD and praise his in/on/with Jerusalem
22 pamene mitundu ya anthu ndi maufumu adzasonkhana kuti alambire Yehova.
in/on/with to gather people together and kingdom to/for to serve: minister [obj] LORD
23 Iye anathyola mphamvu zanga pa nthawi ya moyo wanga; Iyeyo anafupikitsa masiku anga.
to afflict in/on/with way: journey (strength my *Q(K)*) be short day my
24 Choncho Ine ndinati: “Musandichotse, Inu Mulungu wanga, pakati pa masiku a moyo wanga; zaka zanu zimakhalabe pa mibado yonse.
to say God my not to ascend: establish me in/on/with half day my in/on/with generation generation year your
25 Pachiyambi Inu munakhazikitsa maziko a dziko lapansi ndipo mayiko akumwamba ndi ntchito ya manja anu.
to/for face: before [the] land: country/planet to found and deed: work hand your heaven
26 Izi zidzatha, koma Inu mudzakhalapo; zidzatha ngati chovala. Mudzazisintha ngati chovala ndipo zidzatayidwa.
they(masc.) to perish and you(m. s.) to stand: stand and all their like/as garment to become old like/as clothing to pass them and to pass
27 Koma Inu simusintha, ndipo zaka zanu sizidzatha.
and you(m. s.) he/she/it and year your not to finish
28 Ana a atumiki anu adzakhala pamaso panu; zidzukulu zawo zidzakhazikika pamaso panu.”
son: child servant/slave your to dwell and seed: children their to/for face: before your to establish: establish

< Masalimo 102 >