< Masalimo 101 >

1 Salimo la Davide. Ndidzayimba za chikondi ndi chiweruzo chanu cholungama; kwa Inu Yehova ndidzayimba matamando.
[A Psalm by David.] I will sing of loving kindness and justice. To you, LORD, I will sing praises.
2 Ndidzatsata njira yolungama; nanga mudzabwera liti kwa ine? Ndidzayenda mʼnyumba mwanga ndi mtima wosalakwa.
I will be careful to live a blameless life. When will you come to me? I will walk within my house with a blameless heart.
3 Sindidzayika chinthu chilichonse choyipa pamaso panga. Ine ndimadana ndi zochita za anthu opanda chikhulupiriro; iwo sadzadziphatika kwa ine.
I will set no vile thing before my eyes. I hate the deeds of faithless men. They will not cling to me.
4 Anthu a mtima wokhota adzakhala kutali ndi ine; ine sindidzalola choyipa chilichonse kulowa mwa ine.
A perverse heart will be far from me. I will have nothing to do with evil.
5 Aliyense wosinjirira mnansi wake mseri ameneyo ndidzamuletsa; aliyense amene ali ndi maso amwano ndi mtima wodzikuza, ameneyo sindidzamulekerera.
I will silence whoever secretly slanders his neighbor. I won't tolerate one who is haughty and conceited.
6 Maso anga adzakhala pa okhulupirika mʼdziko, kuti akhale pamodzi ndi ine; iye amene mayendedwe ake ndi wosalakwa adzanditumikira.
My eyes will be on the faithful of the land, that they may dwell with me. He who walks in a perfect way, he will serve me.
7 Aliyense wochita chinyengo sadzakhala mʼnyumba mwanga. Aliyense woyankhula mwachinyengo sadzayima pamaso panga.
He who practices deceit won't dwell within my house. He who speaks falsehood won't be established before my eyes.
8 Mmawa uliwonse ndidzatontholetsa anthu onse oyipa mʼdziko; ndidzachotsa aliyense wochita zoyipa mu mzinda wa Yehova.
Morning by morning, I will destroy all the wicked of the land; to cut off all evildoers from the LORD's city.

< Masalimo 101 >