< Masalimo 101 >
1 Salimo la Davide. Ndidzayimba za chikondi ndi chiweruzo chanu cholungama; kwa Inu Yehova ndidzayimba matamando.
A PSALM OF DAVID. I sing kindness and judgment, To You, O YHWH, I sing praise.
2 Ndidzatsata njira yolungama; nanga mudzabwera liti kwa ine? Ndidzayenda mʼnyumba mwanga ndi mtima wosalakwa.
I act wisely in a perfect way, When do You come to me? I habitually walk in the integrity of my heart, In the midst of my house.
3 Sindidzayika chinthu chilichonse choyipa pamaso panga. Ine ndimadana ndi zochita za anthu opanda chikhulupiriro; iwo sadzadziphatika kwa ine.
I do not set a worthless thing before my eyes, I have hated the work of those turning aside, It does not adhere to me.
4 Anthu a mtima wokhota adzakhala kutali ndi ine; ine sindidzalola choyipa chilichonse kulowa mwa ine.
A perverse heart turns aside from me, I do not know wickedness.
5 Aliyense wosinjirira mnansi wake mseri ameneyo ndidzamuletsa; aliyense amene ali ndi maso amwano ndi mtima wodzikuza, ameneyo sindidzamulekerera.
Whoever slanders his neighbor in secret, Him I cut off, The high of eyes and proud of heart, Him I do not endure.
6 Maso anga adzakhala pa okhulupirika mʼdziko, kuti akhale pamodzi ndi ine; iye amene mayendedwe ake ndi wosalakwa adzanditumikira.
My eyes are on the faithful of the land, To dwell with me, Whoever is walking in a perfect way, he serves me.
7 Aliyense wochita chinyengo sadzakhala mʼnyumba mwanga. Aliyense woyankhula mwachinyengo sadzayima pamaso panga.
He who is working deceit does not dwell in my house, Whoever is speaking lies is not established before my eyes.
8 Mmawa uliwonse ndidzatontholetsa anthu onse oyipa mʼdziko; ndidzachotsa aliyense wochita zoyipa mu mzinda wa Yehova.
At morning I cut off all the wicked of the land, To cut off from the city of YHWH All the workers of iniquity!