< Masalimo 100 >

1 Salimo. Nyimbo yothokoza. Fuwulani kwa Yehova mwachimwemwe, inu dziko lonse lapansi.
Haz un alegre sonido al Señor, habitantes de toda la tierra.
2 Mulambireni Yehova mosangalala; bwerani pamaso pake ndi nyimbo zachikondwerero.
Dale culto al Señor con alegría; ven delante de él con una canción.
3 Dziwani kuti Yehova ndi Mulungu. Iye ndiye amene anatipanga ndipo ife ndife ake; ndife anthu ake, nkhosa za pabusa pake.
Asegúrate de que el Señor es Dios; es él quien nos hizo, y nosotros somos suyos; somos su pueblo, y las ovejas a quienes da de comer.
4 Lowani ku zipata zake ndi chiyamiko ndi ku mabwalo ake ndi matamando; muyamikeni ndi kutamanda dzina lake.
Ven a sus puertas con alegría, y en su casa con alabanza; denle honor, bendiciendo su nombre.
5 Pakuti Yehova ndi wabwino ndipo chikondi chake ndi chamuyaya; kukhulupirika kwake nʼkokhazikika pa mibado ndi mibado.
Porque el Señor es bueno, y su misericordia es interminable; su fe es inmutable a través de todas las generaciones.

< Masalimo 100 >