< Masalimo 100 >
1 Salimo. Nyimbo yothokoza. Fuwulani kwa Yehova mwachimwemwe, inu dziko lonse lapansi.
Cantád con júbilo a Dios los de toda la tierra.
2 Mulambireni Yehova mosangalala; bwerani pamaso pake ndi nyimbo zachikondwerero.
Servíd a Jehová con alegría: entrád delante de él con regocijo.
3 Dziwani kuti Yehova ndi Mulungu. Iye ndiye amene anatipanga ndipo ife ndife ake; ndife anthu ake, nkhosa za pabusa pake.
Sabéd que Jehová, él es el Dios: él nos hizo, y no nosotros a nosotros: pueblo suyo somos, y ovejas de su pasto.
4 Lowani ku zipata zake ndi chiyamiko ndi ku mabwalo ake ndi matamando; muyamikeni ndi kutamanda dzina lake.
Entrád por sus puertas con confesión, por sus patios con alabanza: alabádle, bendecíd a su nombre.
5 Pakuti Yehova ndi wabwino ndipo chikondi chake ndi chamuyaya; kukhulupirika kwake nʼkokhazikika pa mibado ndi mibado.
Porque Jehová es bueno, para siempre es su misericordia: y hasta en generación y generación su verdad.